< Levitiko 16 >

1 Atafa ana awiri a Aaroni amene anaphedwa atapita pamaso pa Yehova mosayenera, Yehova anayankhula ndi Mose.
И рече Господ Мојсију пошто погибоше два сина Аронова, а погибоше кад приступише пред Господа,
2 Yehova anawuza Mose kuti, “Uza mchimwene wako Aaroni kuti asamalowe ku Malo Wopatulika, kuseri kwa katani, pamaso pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano nthawi iliyonse imene akufuna kuopa kuti angadzafe, pakuti Ine ndimaoneka mu mtambo umene uli pamwamba pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano.
И каза Господ Мојсију: Реци Арону, брату свом, да не улази у свако доба у светињу за завес пред заклопац који је на ковчегу, да не погине, јер ћу се у облаку над заклопцем јављати.
3 “Aaroni azilowa Malo Wopatulika Kwambiri motere: azitenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
С овим нека улази Арон у светињу: с јунцем за жртву ради греха и с овном за жртву паљеницу.
4 Azivala mwinjiro wopatulika wa nsalu yosalala, azivalanso kabudula wa mʼkati wa nsalu yosalala, azimanga lamba wa nsalu yosalala, ndipo avalenso nduwira ya nsalu yosalala kumutu. Zimenezi ndi nsalu zopatulika ndipo atasamba thupi lonse azivala zimenezi.
Свету кошуљу ланену нека обуче, и гаће ланене нека су на телу његовом, и нека се опаше појасом ланеним и капу ланену нека метне на главу; то су хаљине свете, и нека опере тело своје водом, па онда нека их обуче.
5 Kuchokera pa gulu la Aisraeli, Aaroni azitenga mbuzi zazimuna ziwiri kuti zikhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
А од збора синова Израиљевих нека узме два јарца за жртву ради греха, и једног овна за жртву паљеницу.
6 “Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale yopepesera machimo a iye mwini kuti achite mwambo wopepesera machimo ake pamodzi ndi a banja lake.
И нека принесе Арон јунца свог на жртву за грех и очисти себе и дом свој.
7 Kenaka atenge mbuzi ziwiri zija ndipo aziyimike pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
Потом нека узме два јарца, и нека их метне пред Господа на врата шатора од састанка.
8 Aaroni ndiye achite maere pa mbuzi ziwirizo kuti imodzi ikhale ya Yehova, ndipo inayo ikhale ya Azazele.
И нека Арон баци жреб за та два јарца, један жреб Господу а други жреб Азазелу.
9 Aaroni abwere ndi mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi ya Yehova, ndipo apereke kuti ikhale nsembe yopereka chifukwa cha tchimo.
И нека Арон принесе на жртву јарца на ког падне жреб Господњи, нека га принесе на жртву за грех.
10 Koma mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi yosenza machimo, apereke ya moyo pamaso pa Yehova, kuti achite mwambo wopepesera machimo pa mbuziyo poyitumiza ku chipululu kuti ikhale ya Azazele.
А јарца на ког падне жреб Азазелов нека метне жива пред Господа, да учини очишћење на њему, па нека га пусти у пустињу Азазелу.
11 “Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ake. Ndiye achite mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake pamodzi ndi banja lake. Pambuyo pake aphe ngʼombe yopepesera machimo ake aja.
И нека Арон принесе јунца свог на жртву за грех и очисти себе и дом свој, и нека закоље јунца свог на жртву за грех.
12 Kenaka iye atenge chofukizira chodzaza ndi makala a moto ochokera pa guwa lansembe pamaso pa Yehova. Atengenso lubani wonunkhira ndi woperapera wokwanira manja awiri, ndipo alowe naye kuseri kwa katani.
И нека узме кадионицу пуну жеравице с олтара, који је пред Господом, и пуне прегршти када мирисног истуцаног, и нека унесе за завес.
13 Athire lubani pa moto pamaso pa Yehova kuti utsi wa lubaniyo uphimbe chivundikiro chimene chili pamwamba pa Bokosi la Chipangano, kuti Aaroniyo asafe.
И нека метне кад на огањ пред Господом, да дим од када заклони заклопац који је на сведочанству; тако неће погинути.
14 Ndipo atenge magazi ena a ngʼombeyo, awawaze ndi chala chake pa chivundikiro cha kummawa; kenaka awaze magaziwo ndi chala chake kasanu ndi kawiri patsogolo pa chivundikirocho.
После нека узме крви од јунца и покропи с прста свог по заклопцу према истоку, а пред заклопцем нека седам пута покропи том крвљу с прста свог.
15 “Kenaka Aaroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu, ndipo magazi ake alowe nawo kuseri kwa katani ndi kuchita chimodzimodzi monga anachitira ndi magazi a ngʼombe aja: Aaroni awaze magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho.
И нека закоље јарца на жртву за грех народни, и нека учини с крвљу његовом као што је учинио с крвљу јунчијом, и покропи њом по заклопцу и пред заклопцем.
16 Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika chifukwa cha kudetsedwa ndi kuwukira kwa Aisraeli pa machimo ena aliwonse amene achita. Achite chimodzimodzi ndi tenti ya msonkhano imenenso ili yodetsedwa chifukwa cha machimo awo.
И тако ће очистити светињу од нечистота синова Израиљевих и од преступа њихових у свим гресима њиховим; тако ће учинити и у шатору од састанка, који је међу њима усред нечистота њихових.
17 Mu tenti ya msonkhano musakhale munthu ndi mmodzi yemwe nthawi imene Aaroni akupita kukachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika mpaka atatulukako. Musakhale munthu mu tenti ya msonkhano mpaka atachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake, banja lake ndi gulu lonse la Aisraeli.
А нико да не буде у шатору од састанка кад он уђе да чини очишћење у светињи, докле не изађе и сврши очишћење за се и за дом свој и за сав збор израиљски.
18 “Kenaka, Aaroniyo akatuluka apite ku guwa limene lili pamaso pa Yehova ndi kulichitira mwambo wolipepesera. Atengeko magazi a ngʼombe yayimuna ndiponso magazi a mbuzi ndi kuwapaka pa nyanga zonse za guwa lansembe.
А нека изађе к олтару који је пред Господом, и очисти га; и узевши крви од јунца и крви од јарца нека помаже рогове олтару унаоколо;
19 Magazi ena awawaze pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kawiri kuliyeretsa ndi kulipatula kuchotsa zodetsa za Aisraeli.
И нека га покропи одозго истом крвљу с прста свог седам пута; тако ће га очистити и посветити га од нечистота синова Израиљевих.
20 “Aaroni akatsiriza mwambo wopepesera Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa, azibwera ndi mbuzi yamoyo kudzayipereka nsembe.
А кад очисти светињу и шатор од састанка и олтар, тада нека доведе јарца живог.
21 Aaroni asanjike manja ake pa mutu wa mbuziyo ndipo awulule pa mbuziyo zoyipa zonse ndi zowukira zonse za Aisraeli, kutanthauza machimo awo onse. Machimowo awayike pa mutu wa mbuziyo. Kenaka munthu amene anasankhidwa athamangitsire mbuziyo ku chipululu.
И метнувши Арон обе руке своје на главу јарцу живом, нека исповеди над њим сва безакоња синова Израиљевих и све преступе њихове у свим гресима њиховим, и метнувши их на главу јарцу нека га да човеку спремном да га истера у пустињу.
22 Mbuziyo isenze machimo awo onse ndi kupita nawo kutali ndipo munthuyo aleke mbuziyo kuti ipite ku chipululuko.
И јарац ће однети на себи сва безакоња њихова у пустињу; и пустиће оног јарца у пустињу.
23 “Pambuyo pake Aaroni alowe mu tenti ya msonkhano ndi kuvula zovala zosalala zija zimene anavala polowa ku Malo Wopatulika ndi kuzisiya komweko.
Потом нека опет уђе Арон у шатор од састанка и свуче хаљине ланене које је обукао када је ишао у светињу, и онде нека их остави.
24 Asambe thupi lonse ku Malo Wopatulika ndi kuvala zovala zake za nthawi zonse. Kenaka atuluke ndi kukapereka nsembe yopsereza ya iye mwini, ndiponso nsembe yopsereza yoperekera anthu. Akatero ndiye kuti wachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake ndi a anthu.
Па нека опере тело своје на светом месту и обуче своје хаљине; и изашав нека принесе своју жртву паљеницу, и очисти себе и народ.
25 Mafuta a nyama yopepesera machimo awatenthe pa guwa lansembe.
А сало од жртве за грех нека запали на олтару.
26 “Tsono munthu amene anaperekeza mbuzi yosenza machimo ija achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe ku msasa.
А ко одведе јарца за Азазела, нека опере хаљине своје и окупа тело своје у води, па онда нека уђе у логор.
27 Ngʼombe ndi mbuzi zoperekera nsembe yopepesera machimo zimene magazi ake anabwera nawo kuti achitire mwambo wopepesera Malo Wopatulika, azitulutsire kunja kwa msasa. Koma zikopa zake, nyama yake ndi matumbo ake azitenthe.
А јунца за грех и јарца за грех, од којих је крв унесена да се учини очишћење у светињи, нека изнесу напоље из логора, и нека спале огњем коже њихове и месо њихово и балегу њихову.
28 Munthu amene azitenthe achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe mu msasa.
А ко их спали, нека опере хаљине своје и окупа тело своје у води, па онда нека дође у логор.
29 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya: Mwezi wachisanu ndi chiwiri, pa tsiku la khumi la mwezi, mugonje pamaso pa Yehova. Musamagwire ntchito iliyonse, kaya ndinu mbadwa kapena mlendo amene akukhala pakati panu,
И ово нека вам буде вечна уредба: десети дан седмог месеца мучите душе своје, и не радите никакав посао, ни домородац ни дошљак који се бави међу вама.
30 chifukwa tsiku limeneli kudzachitika mwambo wopepesera machimo anu, kukuyeretsani kuti mukhale oyeretsedwa ku machimo anu pamaso pa Yehova.
Јер у тај дан бива очишћење за вас, да се очистите; бићете очишћени од свих греха својих пред Господом.
31 Limeneli ndi tsiku lanu la Sabata lopumula, ndipo muzigonja pamaso pa Yehova. Limeneli ndi lamulo lanu la muyaya.
То нека вам је почивање суботно, и мучите душе своје по уредби вечној.
32 Wansembe amene wadzozedwa ndi kupatulidwa kuti akhale wansembe kulowa mʼmalo mwa abambo ake ndiye azichita mwambo wopepesera machimo atavala zovala zake zosalala ndi zopatulika.
А свештеник који буде помазан и који буде освећен да врши службу свештеничку на место оца свог, он нека очишћа обукавши се у хаљине ланене, хаљине свете.
33 Adzachite mwambo wopepesera machimo Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Adzachitenso mwambo wopepesera anzake ndi gulu lonse la anthu.
И нека очисти светињу свету и шатор од састанка; и олтар нека очисти; и свештенике и сав народ сабрани нека очисти.
34 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya. Mwambo wopepesera machimo uzichitika kamodzi pa chaka chifukwa cha machimo a anthu onse.” Ndipo Mose anachita monga momwe Yehova analamulira.
И ово нека вам је вечна уредба да очишћате синове Израиљеве од свих греха њихових један пут у години. И учини Мојсије како му заповеди Господ.

< Levitiko 16 >