< Levitiko 16 >

1 Atafa ana awiri a Aaroni amene anaphedwa atapita pamaso pa Yehova mosayenera, Yehova anayankhula ndi Mose.
After the two sons of Aaron died because they burned incense to Yahweh [in a manner that was contrary to what Yahweh commanded], Yahweh spoke to Moses/me.
2 Yehova anawuza Mose kuti, “Uza mchimwene wako Aaroni kuti asamalowe ku Malo Wopatulika, kuseri kwa katani, pamaso pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano nthawi iliyonse imene akufuna kuopa kuti angadzafe, pakuti Ine ndimaoneka mu mtambo umene uli pamwamba pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano.
He said to him/me, “Warn your [older] brother Aaron that he must not enter the Very Holy Place inside the curtain that is in the Sacred Tent whenever he wants to, because the cover of the sacred chest is there. That is the place where the priest (makes atonement for/requests me to forgive) sins. I am present in the cloud that is over the cover of the sacred chest. If Aaron goes in that room when it is not the proper time, he will die!
3 “Aaroni azilowa Malo Wopatulika Kwambiri motere: azitenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
“When Aaron enters the Sacred Tent area, he must bring a bull that [will be killed] to become an offering/sacrifice for sins, and a ram [to be killed] to be an offering that will be completely burned [on the altar].
4 Azivala mwinjiro wopatulika wa nsalu yosalala, azivalanso kabudula wa mʼkati wa nsalu yosalala, azimanga lamba wa nsalu yosalala, ndipo avalenso nduwira ya nsalu yosalala kumutu. Zimenezi ndi nsalu zopatulika ndipo atasamba thupi lonse azivala zimenezi.
Then he must bathe his whole body, and put on the linen underwear/undershorts and the linen gown. He must tie the linen sash/waistbands around his waist and wrap the turban around his head. Those are his sacred garments.
5 Kuchokera pa gulu la Aisraeli, Aaroni azitenga mbuzi zazimuna ziwiri kuti zikhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
The Israeli people must then bring to him two male goats [to be killed] as an offering/sacrifice for sin, and a ram to be [killed and] burned completely [on the altar].
6 “Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale yopepesera machimo a iye mwini kuti achite mwambo wopepesera machimo ake pamodzi ndi a banja lake.
“Aaron must offer the bull [to me] to be a sacrifice in order that (I will forgive his sins and the sins of his family/his sins and the sins of his family will be forgiven).
7 Kenaka atenge mbuzi ziwiri zija ndipo aziyimike pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
Then he must bring the two male goats to me at the entrance to the Sacred Tent.
8 Aaroni ndiye achite maere pa mbuzi ziwirizo kuti imodzi ikhale ya Yehova, ndipo inayo ikhale ya Azazele.
He must (cast lots/throw down stones that have been marked) to determine which goat will be [sacrificed] to me, and which will be the goat that will be set free.
9 Aaroni abwere ndi mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi ya Yehova, ndipo apereke kuti ikhale nsembe yopereka chifukwa cha tchimo.
Aaron must bring to me the goat that was chosen to be sacrificed. It will be an offering for the people’s sins.
10 Koma mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi yosenza machimo, apereke ya moyo pamaso pa Yehova, kuti achite mwambo wopepesera machimo pa mbuziyo poyitumiza ku chipululu kuti ikhale ya Azazele.
Aaron must also bring to me the other goat, but it is not to be killed. It will be freed while it is still alive. As a result of Aaron sending it into the desert, the people’s sins will be forgiven.
11 “Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ake. Ndiye achite mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake pamodzi ndi banja lake. Pambuyo pake aphe ngʼombe yopepesera machimo ake aja.
“Then Aaron must bring the young bull to me, to be an offering/sacrifice for himself and for his family. He must slaughter that bull to be an offering for their sins, [and he must drain the blood into a basin].
12 Kenaka iye atenge chofukizira chodzaza ndi makala a moto ochokera pa guwa lansembe pamaso pa Yehova. Atengenso lubani wonunkhira ndi woperapera wokwanira manja awiri, ndipo alowe naye kuseri kwa katani.
Then he must take some burning coals from the [bronze] altar and put them in the incense burner. Then he must fill his hands with fragrant finely-ground incense. Then he must take the incense and the incense burner inside the curtain into the Very Holy Place [of the Sacred Tent].
13 Athire lubani pa moto pamaso pa Yehova kuti utsi wa lubaniyo uphimbe chivundikiro chimene chili pamwamba pa Bokosi la Chipangano, kuti Aaroniyo asafe.
There he must put the incense on the burning coals, with the result that a cloud of burning incense will rise up over the lid of the sacred chest. If he obeys these instructions, he will not die [like Korah’s two sons did because of offering incense incorrectly] (OR, [because of being in God’s presence]).
14 Ndipo atenge magazi ena a ngʼombeyo, awawaze ndi chala chake pa chivundikiro cha kummawa; kenaka awaze magaziwo ndi chala chake kasanu ndi kawiri patsogolo pa chivundikirocho.
Then he must dip his finger into [the basin] and sprinkle some blood on the lid of the sacred chest, and also sprinkle some blood seven times against the front of the chest.
15 “Kenaka Aaroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu, ndipo magazi ake alowe nawo kuseri kwa katani ndi kuchita chimodzimodzi monga anachitira ndi magazi a ngʼombe aja: Aaroni awaze magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho.
[“Aaron must then go outside the Sacred Tent] and slaughter the goat to be an offering for the sins of the people. Then he must bring its blood into the Very Holy Place behind the curtain. There he must sprinkle [some of] that blood on the lid of the sacred chest and against the front of the chest, like he did with the bull’s blood.
16 Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika chifukwa cha kudetsedwa ndi kuwukira kwa Aisraeli pa machimo ena aliwonse amene achita. Achite chimodzimodzi ndi tenti ya msonkhano imenenso ili yodetsedwa chifukwa cha machimo awo.
By doing that, he will purify the Very Holy Place. And he must sprinkle more of the blood on the Sacred Tent, because the tent is in the midst of the camp of the Israeli people who have become unacceptable to me [because of their sins].
17 Mu tenti ya msonkhano musakhale munthu ndi mmodzi yemwe nthawi imene Aaroni akupita kukachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika mpaka atatulukako. Musakhale munthu mu tenti ya msonkhano mpaka atachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake, banja lake ndi gulu lonse la Aisraeli.
When Aaron goes into the Very Holy Place [in the Sacred Tent] to purify it, no one else is permitted to enter [the other part of] the Sacred Tent. Only after Aaron has performed rituals to enable me to forgive him and his family, and all the Israeli people, is any priest permitted to enter the Sacred Tent.
18 “Kenaka, Aaroniyo akatuluka apite ku guwa limene lili pamaso pa Yehova ndi kulichitira mwambo wolipepesera. Atengeko magazi a ngʼombe yayimuna ndiponso magazi a mbuzi ndi kuwapaka pa nyanga zonse za guwa lansembe.
“Then Aaron must go outside the tent to purify my altar. He must do this by smearing some of the blood from the bull and some of the blood from the goat on each of the projections at the corners of the altar.
19 Magazi ena awawaze pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kawiri kuliyeretsa ndi kulipatula kuchotsa zodetsa za Aisraeli.
Then Aaron must dip his finger into the [basin of] blood and sprinkle some of the blood over the altar seven times. By doing that, he will cleanse it from being unholy [because of the sins] of the Israeli people, and it will become holy again.
20 “Aaroni akatsiriza mwambo wopepesera Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa, azibwera ndi mbuzi yamoyo kudzayipereka nsembe.
“When Aaron has finished purifying the Very Holy Place [inside the Sacred Tent] and all of the Sacred Tent and the altar, he must bring the goat that was chosen to be set free.
21 Aaroni asanjike manja ake pa mutu wa mbuziyo ndipo awulule pa mbuziyo zoyipa zonse ndi zowukira zonse za Aisraeli, kutanthauza machimo awo onse. Machimowo awayike pa mutu wa mbuziyo. Kenaka munthu amene anasankhidwa athamangitsire mbuziyo ku chipululu.
He must put both of his hands on the head of the goat and confess all the sins [DOU] of the Israeli people. By doing that, he will put [the guilt of] their sins on the head of the goat. Then he must give the goat to a man who is chosen, and that man will send the goat out into the desert.
22 Mbuziyo isenze machimo awo onse ndi kupita nawo kutali ndipo munthuyo aleke mbuziyo kuti ipite ku chipululuko.
[It is as though] the goat will carry away into the desert [the guilt for] the sins of all the people.
23 “Pambuyo pake Aaroni alowe mu tenti ya msonkhano ndi kuvula zovala zosalala zija zimene anavala polowa ku Malo Wopatulika ndi kuzisiya komweko.
“When Aaron approaches the Sacred Tent, he must take off the linen clothes that he wore when he [previously] entered the Very Holy Place, and he must leave those clothes there.
24 Asambe thupi lonse ku Malo Wopatulika ndi kuvala zovala zake za nthawi zonse. Kenaka atuluke ndi kukapereka nsembe yopsereza ya iye mwini, ndiponso nsembe yopsereza yoperekera anthu. Akatero ndiye kuti wachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake ndi a anthu.
Then he must bathe in a sacred place, put on his regular/ordinary clothes, and sacrifice the animals that will be burned completely on the altar for his own sins and for the sins of the Israeli people. By doing that he will enable me to forgive him and them.
25 Mafuta a nyama yopepesera machimo awatenthe pa guwa lansembe.
He must also burn on the altar all the fat of the bull and the goat that were sacrificed.
26 “Tsono munthu amene anaperekeza mbuzi yosenza machimo ija achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe ku msasa.
“The man who was chosen to send the other goat into the desert and free it there must afterwards wash his clothes and bathe. Then he may return to the camp.
27 Ngʼombe ndi mbuzi zoperekera nsembe yopepesera machimo zimene magazi ake anabwera nawo kuti achitire mwambo wopepesera Malo Wopatulika, azitulutsire kunja kwa msasa. Koma zikopa zake, nyama yake ndi matumbo ake azitenthe.
The carcasses of the bull and the goat that were slaughtered to be an offering/sacrifice for the people’s sins, whose blood was taken inside the Very Holy Place to enable Yahweh to forgive the Israeli people, must be carried outside the camp and burned. The hides/skins of the animals, the inner organs, and the dung must also be burned.
28 Munthu amene azitenthe achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe mu msasa.
The man who burns those things must then wash his clothes and bathe before he returns to the camp.
29 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya: Mwezi wachisanu ndi chiwiri, pa tsiku la khumi la mwezi, mugonje pamaso pa Yehova. Musamagwire ntchito iliyonse, kaya ndinu mbadwa kapena mlendo amene akukhala pakati panu,
“On (October/the month after the dry season ends), on the day that I have appointed, you all must (fast/abstain from eating food) and not do any work. This is a rule/law that will never end. It must be obeyed by you people who have been Israelis all your lives, and also by foreigners who are living among you.
30 chifukwa tsiku limeneli kudzachitika mwambo wopepesera machimo anu, kukuyeretsani kuti mukhale oyeretsedwa ku machimo anu pamaso pa Yehova.
On that day, Aaron will perform rituals to enable me to forgive you all, and then I will cleanse/free you all from [the guilt of] all your sins and you will become acceptable to me.
31 Limeneli ndi tsiku lanu la Sabata lopumula, ndipo muzigonja pamaso pa Yehova. Limeneli ndi lamulo lanu la muyaya.
That will be a day for you to rest and not do any work, like the Sabbath days, and you must (fast/abstain from eating food) all that day. That is a permanent command/law for you all to obey.
32 Wansembe amene wadzozedwa ndi kupatulidwa kuti akhale wansembe kulowa mʼmalo mwa abambo ake ndiye azichita mwambo wopepesera machimo atavala zovala zake zosalala ndi zopatulika.
In future years, [after Aaron has died], this ritual/ceremony to enable me to forgive you all [DOU] will be performed by the Supreme Priest who is anointed [with olive oil] and appointed to serve instead of his ancestor Aaron. He must put on the sacred clothes made of linen
33 Adzachite mwambo wopepesera machimo Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Adzachitenso mwambo wopepesera anzake ndi gulu lonse la anthu.
and offer sacrifices to purify the Very Holy Place, all of the Sacred Tent, the altar, the priests, and all the Israel people [like Aaron did].
34 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya. Mwambo wopepesera machimo uzichitika kamodzi pa chaka chifukwa cha machimo a anthu onse.” Ndipo Mose anachita monga momwe Yehova analamulira.
This will be a permanent command/law for you to obey once every year, to enable me to forgive you Israeli people for the sins that you have committed.” Moses/I obeyed all those instructions/commands that Yahweh had given to him/me.

< Levitiko 16 >