< Levitiko 16 >
1 Atafa ana awiri a Aaroni amene anaphedwa atapita pamaso pa Yehova mosayenera, Yehova anayankhula ndi Mose.
Adonai spoke to Moses [Drawn out], after the death of the two sons of Aaron [Light-bringer], when they came near before Adonai, and died;
2 Yehova anawuza Mose kuti, “Uza mchimwene wako Aaroni kuti asamalowe ku Malo Wopatulika, kuseri kwa katani, pamaso pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano nthawi iliyonse imene akufuna kuopa kuti angadzafe, pakuti Ine ndimaoneka mu mtambo umene uli pamwamba pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano.
and Adonai said to Moses [Drawn out], “Tell Aaron [Light-bringer] your brother, not to come at all times into the Most Holy Place within the veil, before the mercy seat which is on the ark; lest he die: for I will appear in the cloud on the mercy seat.
3 “Aaroni azilowa Malo Wopatulika Kwambiri motere: azitenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
“Aaron [Light-bringer] shall come into the sanctuary with a young bull for a habitual sin ·miss the mark· offering, and a ram for a burnt offering.
4 Azivala mwinjiro wopatulika wa nsalu yosalala, azivalanso kabudula wa mʼkati wa nsalu yosalala, azimanga lamba wa nsalu yosalala, ndipo avalenso nduwira ya nsalu yosalala kumutu. Zimenezi ndi nsalu zopatulika ndipo atasamba thupi lonse azivala zimenezi.
He shall put on the holy linen coat. He shall have the linen breeches on his body, and shall put on the linen sash, and he shall be clothed with the linen turban. They are the holy garments. He shall bathe his body in water, and put them on.
5 Kuchokera pa gulu la Aisraeli, Aaroni azitenga mbuzi zazimuna ziwiri kuti zikhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
He shall take from the congregation of the children of Israel [God prevails] two male goats for a habitual sin ·miss the mark· offering, and one ram for a burnt offering.
6 “Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale yopepesera machimo a iye mwini kuti achite mwambo wopepesera machimo ake pamodzi ndi a banja lake.
“Aaron [Light-bringer] shall offer the bull of the habitual sin ·miss the mark· offering, which is for himself, and make atonement for himself and for his house.
7 Kenaka atenge mbuzi ziwiri zija ndipo aziyimike pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
He shall take the two goats, and set them before Adonai at the door of the Tent of Meeting.
8 Aaroni ndiye achite maere pa mbuzi ziwirizo kuti imodzi ikhale ya Yehova, ndipo inayo ikhale ya Azazele.
Aaron [Light-bringer] shall cast lots for the two goats; one lot for Adonai, and the other lot for the scapegoat.
9 Aaroni abwere ndi mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi ya Yehova, ndipo apereke kuti ikhale nsembe yopereka chifukwa cha tchimo.
Aaron [Light-bringer] shall present the goat on which the lot fell for Adonai, and offer him for a habitual sin ·miss the mark· offering.
10 Koma mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi yosenza machimo, apereke ya moyo pamaso pa Yehova, kuti achite mwambo wopepesera machimo pa mbuziyo poyitumiza ku chipululu kuti ikhale ya Azazele.
But the goat, on which the lot fell for the scapegoat, shall be presented alive before Adonai, to make atonement for him, to send him away for the scapegoat into the wilderness.
11 “Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ake. Ndiye achite mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake pamodzi ndi banja lake. Pambuyo pake aphe ngʼombe yopepesera machimo ake aja.
“Aaron [Light-bringer] shall present the bull of the habitual sin ·miss the mark· offering, which is for himself, and shall make atonement for himself and for his house, and shall kill the bull of the habitual sin ·miss the mark· offering which is for himself.
12 Kenaka iye atenge chofukizira chodzaza ndi makala a moto ochokera pa guwa lansembe pamaso pa Yehova. Atengenso lubani wonunkhira ndi woperapera wokwanira manja awiri, ndipo alowe naye kuseri kwa katani.
He shall take a censer full of coals of fire from off the altar before Adonai, and two handfuls of sweet incense beaten small, and bring it within the veil:
13 Athire lubani pa moto pamaso pa Yehova kuti utsi wa lubaniyo uphimbe chivundikiro chimene chili pamwamba pa Bokosi la Chipangano, kuti Aaroniyo asafe.
and he shall put the incense on the fire before Adonai, that the cloud of the incense may cover the mercy seat that is on the testimony, so that he will not die.
14 Ndipo atenge magazi ena a ngʼombeyo, awawaze ndi chala chake pa chivundikiro cha kummawa; kenaka awaze magaziwo ndi chala chake kasanu ndi kawiri patsogolo pa chivundikirocho.
He shall take some of the blood of the bull, and sprinkle it with his finger on the mercy seat on the east; and before the mercy seat he shall sprinkle some of the blood with his finger seven times.
15 “Kenaka Aaroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu, ndipo magazi ake alowe nawo kuseri kwa katani ndi kuchita chimodzimodzi monga anachitira ndi magazi a ngʼombe aja: Aaroni awaze magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho.
“Then he shall kill the goat of the habitual sin ·miss the mark· offering, that is for the people, and bring his blood within the veil, and do with his blood as he did with the blood of the bull, and sprinkle it on the mercy seat, and before the mercy seat.
16 Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika chifukwa cha kudetsedwa ndi kuwukira kwa Aisraeli pa machimo ena aliwonse amene achita. Achite chimodzimodzi ndi tenti ya msonkhano imenenso ili yodetsedwa chifukwa cha machimo awo.
He shall make atonement for the Holy Place, because of the uncleanness of the children of Israel [God prevails], and because of their rebellious breaches of relationships, even all their habitual sins ·missing the marks·; and so he shall do for the Tent of Meeting, that dwells with them in the middle of their uncleanness.
17 Mu tenti ya msonkhano musakhale munthu ndi mmodzi yemwe nthawi imene Aaroni akupita kukachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika mpaka atatulukako. Musakhale munthu mu tenti ya msonkhano mpaka atachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake, banja lake ndi gulu lonse la Aisraeli.
No one shall be in the Tent of Meeting when he enters to make atonement in the Holy Place, until he comes out, and has made atonement for himself and for his household, and for all the assembly of Israel [God prevails].
18 “Kenaka, Aaroniyo akatuluka apite ku guwa limene lili pamaso pa Yehova ndi kulichitira mwambo wolipepesera. Atengeko magazi a ngʼombe yayimuna ndiponso magazi a mbuzi ndi kuwapaka pa nyanga zonse za guwa lansembe.
“He shall go out to the altar that is before Adonai and make atonement for it, and shall take some of the bull’s blood, and some of the goat’s blood, and put it around on the horns of the altar.
19 Magazi ena awawaze pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kawiri kuliyeretsa ndi kulipatula kuchotsa zodetsa za Aisraeli.
He shall sprinkle some of the blood on it with his finger seven times, and cleanse it, and make it holy from the uncleanness of the children of Israel [God prevails].
20 “Aaroni akatsiriza mwambo wopepesera Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa, azibwera ndi mbuzi yamoyo kudzayipereka nsembe.
“When he has finished atoning for the Holy Place, the Tent of Meeting, and the altar, he shall present the live goat.
21 Aaroni asanjike manja ake pa mutu wa mbuziyo ndipo awulule pa mbuziyo zoyipa zonse ndi zowukira zonse za Aisraeli, kutanthauza machimo awo onse. Machimowo awayike pa mutu wa mbuziyo. Kenaka munthu amene anasankhidwa athamangitsire mbuziyo ku chipululu.
Aaron [Light-bringer] shall lay both his hands on the head of the live goat, and yadah ·extend hands in confession· over him confessing all the depravities (moral evils) of the children of Israel [God prevails], and all their rebellious breaches of relationships, even all their habitual sins ·missing the marks·; and he shall put them on the head of the goat, and shall send him away into the wilderness by the hand of a man who is in readiness.
22 Mbuziyo isenze machimo awo onse ndi kupita nawo kutali ndipo munthuyo aleke mbuziyo kuti ipite ku chipululuko.
The goat shall carry all their depravities (moral evils) on himself to a solitary land, and he shall let the goat go in the wilderness.
23 “Pambuyo pake Aaroni alowe mu tenti ya msonkhano ndi kuvula zovala zosalala zija zimene anavala polowa ku Malo Wopatulika ndi kuzisiya komweko.
“Aaron [Light-bringer] shall come into the Tent of Meeting, and shall take off the linen garments, which he put on when he went into the Holy Place, and shall leave them there.
24 Asambe thupi lonse ku Malo Wopatulika ndi kuvala zovala zake za nthawi zonse. Kenaka atuluke ndi kukapereka nsembe yopsereza ya iye mwini, ndiponso nsembe yopsereza yoperekera anthu. Akatero ndiye kuti wachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake ndi a anthu.
Then he shall bathe himself in water in a holy place, and put on his garments, and come out and offer his burnt offering and the burnt offering of the people, and make atonement for himself and for the people.
25 Mafuta a nyama yopepesera machimo awatenthe pa guwa lansembe.
The fat of the habitual sin ·miss the mark· offering he shall burn on the altar.
26 “Tsono munthu amene anaperekeza mbuzi yosenza machimo ija achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe ku msasa.
“He who lets the goat go for the scapegoat shall wash his clothes, and bathe his flesh in water, and afterward he shall come into the camp.
27 Ngʼombe ndi mbuzi zoperekera nsembe yopepesera machimo zimene magazi ake anabwera nawo kuti achitire mwambo wopepesera Malo Wopatulika, azitulutsire kunja kwa msasa. Koma zikopa zake, nyama yake ndi matumbo ake azitenthe.
The bull for the habitual sin ·miss the mark· offering, and the goat for the habitual sin ·miss the mark· offering, whose blood was brought in to make atonement in the Holy Place, shall be carried outside the camp; and they shall burn their skins, their flesh, and their dung with fire.
28 Munthu amene azitenthe achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe mu msasa.
He who burns them shall wash his clothes, and bathe his flesh in water, and afterward he shall come into the camp.
29 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya: Mwezi wachisanu ndi chiwiri, pa tsiku la khumi la mwezi, mugonje pamaso pa Yehova. Musamagwire ntchito iliyonse, kaya ndinu mbadwa kapena mlendo amene akukhala pakati panu,
“It shall be a regulation to you forever: in the seventh month Ethanim ·Ever-flowing durable stream (in Hebrew), 7· or Tishrei ·[Beginning (in Babylonian)]·, on the tenth day of the month, you shall afflict your souls, and shall do no kind of work, the native-born, or the stranger who lives as a foreigner among you:
30 chifukwa tsiku limeneli kudzachitika mwambo wopepesera machimo anu, kukuyeretsani kuti mukhale oyeretsedwa ku machimo anu pamaso pa Yehova.
for on this day shall atonement be made for you, to cleanse you; from all your habitual sins ·missing the marks· you shall be clean before Adonai.
31 Limeneli ndi tsiku lanu la Sabata lopumula, ndipo muzigonja pamaso pa Yehova. Limeneli ndi lamulo lanu la muyaya.
It is a Shabath ·Intermission· of solemn rest to you, and you shall afflict your souls. It is a regulation forever.
32 Wansembe amene wadzozedwa ndi kupatulidwa kuti akhale wansembe kulowa mʼmalo mwa abambo ake ndiye azichita mwambo wopepesera machimo atavala zovala zake zosalala ndi zopatulika.
The priest, who is anointed and who is consecrated to be priest in his father’s place, shall make the atonement, and shall put on the linen garments, even the holy garments.
33 Adzachite mwambo wopepesera machimo Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Adzachitenso mwambo wopepesera anzake ndi gulu lonse la anthu.
Then he shall make atonement for the Holy Sanctuary; and he shall make atonement for the Tent of Meeting and for the altar; and he shall make atonement for the priests and for all the people of the assembly.
34 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya. Mwambo wopepesera machimo uzichitika kamodzi pa chaka chifukwa cha machimo a anthu onse.” Ndipo Mose anachita monga momwe Yehova analamulira.
“This shall be an everlasting regulation for you, to make atonement for the children of Israel [God prevails] once in the year because of all their habitual sins ·missing the marks·.” It was done as Adonai enjoined Moses [Drawn out].