< Levitiko 16 >

1 Atafa ana awiri a Aaroni amene anaphedwa atapita pamaso pa Yehova mosayenera, Yehova anayankhula ndi Mose.
HERREN talede til Moses, efter at Døden havde ramt Arons to Sønner, da de traadte frem for HERRENS Aasyn og døde,
2 Yehova anawuza Mose kuti, “Uza mchimwene wako Aaroni kuti asamalowe ku Malo Wopatulika, kuseri kwa katani, pamaso pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano nthawi iliyonse imene akufuna kuopa kuti angadzafe, pakuti Ine ndimaoneka mu mtambo umene uli pamwamba pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano.
og HERREN sagde til Moses: Sig til din Broder Aron, at han ikke til enhver Tid maa gaa ind i Helligdommen inden for Forhænget foran Sonedækket paa Arken, ellers skal han dø, thi jeg kommer til Syne i Skyen over Sonedækket.
3 “Aaroni azilowa Malo Wopatulika Kwambiri motere: azitenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
Kun saaledes maa Aron komme ind i Helligdommen: Med en ung Tyr til Syndoffer og en Væder til Brændoffer;
4 Azivala mwinjiro wopatulika wa nsalu yosalala, azivalanso kabudula wa mʼkati wa nsalu yosalala, azimanga lamba wa nsalu yosalala, ndipo avalenso nduwira ya nsalu yosalala kumutu. Zimenezi ndi nsalu zopatulika ndipo atasamba thupi lonse azivala zimenezi.
han skal iføre sig en hellig Linnedkjortel, bære Linnedbenklæder over sin Blusel, omgjorde sig med et Linnedbælte og binde et Linned Hovedklæde om sit Hoved; det er hellige Klæder; og han skal bade sit Legeme i Vand, før han ifører sig dem.
5 Kuchokera pa gulu la Aisraeli, Aaroni azitenga mbuzi zazimuna ziwiri kuti zikhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
Af Israeliternes Menighed skal han tage to Gedebukke til Syndoffer og en Væder til Brændoffer.
6 “Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale yopepesera machimo a iye mwini kuti achite mwambo wopepesera machimo ake pamodzi ndi a banja lake.
Saa skal Aron ofre sin egen Syndoffertyr og skaffe sig og sit Hus Soning.
7 Kenaka atenge mbuzi ziwiri zija ndipo aziyimike pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
Derefter skal han tage de to Bukke og stille dem frem for HERRENS Aasyn ved Indgangen til Aabenbaringsteltet.
8 Aaroni ndiye achite maere pa mbuzi ziwirizo kuti imodzi ikhale ya Yehova, ndipo inayo ikhale ya Azazele.
Og Aron skal kaste Lod om de to Bukke, et Lod for HERREN og et for Azazel;
9 Aaroni abwere ndi mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi ya Yehova, ndipo apereke kuti ikhale nsembe yopereka chifukwa cha tchimo.
og den Buk, der ved Loddet tilfalder HERREN, skal Aron føre frem og ofre som Syndoffer;
10 Koma mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi yosenza machimo, apereke ya moyo pamaso pa Yehova, kuti achite mwambo wopepesera machimo pa mbuziyo poyitumiza ku chipululu kuti ikhale ya Azazele.
men den Buk, der ved Loddet tilfalder Azazel, skal fremstilles levende for HERRENS Aasyn, for at man kan fuldbyrde Soningen over den og sende den ud i Ørkenen til Azazel.
11 “Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ake. Ndiye achite mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake pamodzi ndi banja lake. Pambuyo pake aphe ngʼombe yopepesera machimo ake aja.
Aron skal da føre sin egen Syndoffertyr frem og skaffe sig og sit Hus Soning og slagte sin egen Syndoffertyr.
12 Kenaka iye atenge chofukizira chodzaza ndi makala a moto ochokera pa guwa lansembe pamaso pa Yehova. Atengenso lubani wonunkhira ndi woperapera wokwanira manja awiri, ndipo alowe naye kuseri kwa katani.
Derpaa skal han tage en Pandefuld Gløder fra Alteret for HERRENS Aasyn og to Haandfulde stødt, vellugtende Røgelse og bære det inden for Forhænget.
13 Athire lubani pa moto pamaso pa Yehova kuti utsi wa lubaniyo uphimbe chivundikiro chimene chili pamwamba pa Bokosi la Chipangano, kuti Aaroniyo asafe.
Og han skal komme Røgelse paa Ilden for HERRENS Aasyn, saa at Røgelsesskyen skjuler Sonedækket oven over Vidnesbyrdet, for at han ikke skal dø.
14 Ndipo atenge magazi ena a ngʼombeyo, awawaze ndi chala chake pa chivundikiro cha kummawa; kenaka awaze magaziwo ndi chala chake kasanu ndi kawiri patsogolo pa chivundikirocho.
Saa skal han tage noget af Tyrens Blod og stænke det med sin Finger fortil paa Sonedækket, og foran Sonedækket skal han syv Gange stænke noget af Blodet med sin Finger.
15 “Kenaka Aaroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu, ndipo magazi ake alowe nawo kuseri kwa katani ndi kuchita chimodzimodzi monga anachitira ndi magazi a ngʼombe aja: Aaroni awaze magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho.
Derefter skal han slagte Folkets Syndofferbuk, bære dens Blod inden for Forhænget og gøre med det som med Tyrens Blod, stænke det paa Sonedækket og foran Sonedækket.
16 Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika chifukwa cha kudetsedwa ndi kuwukira kwa Aisraeli pa machimo ena aliwonse amene achita. Achite chimodzimodzi ndi tenti ya msonkhano imenenso ili yodetsedwa chifukwa cha machimo awo.
Saaledes skal han skaffe Helligdommen Soning for Israeliternes Urenhed og deres Overtrædelser, alle deres Synder, og paa samme Maade skal han gøre med Aabenbaringsteltet, der har sin Plads hos dem midt i deres Urenhed.
17 Mu tenti ya msonkhano musakhale munthu ndi mmodzi yemwe nthawi imene Aaroni akupita kukachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika mpaka atatulukako. Musakhale munthu mu tenti ya msonkhano mpaka atachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake, banja lake ndi gulu lonse la Aisraeli.
Intet Menneske maa komme i Aabenbaringsteltet, naar han gaar ind for at skaffe Soning i Helligdommen, før han gaar ud igen. Saaledes skal han skaffe sig selv, sit Hus og hele Israels Forsamling Soning.
18 “Kenaka, Aaroniyo akatuluka apite ku guwa limene lili pamaso pa Yehova ndi kulichitira mwambo wolipepesera. Atengeko magazi a ngʼombe yayimuna ndiponso magazi a mbuzi ndi kuwapaka pa nyanga zonse za guwa lansembe.
Saa skal han gaa ud til Alteret, som staar for HERRENS Aasyn, og skaffe det Soning; han skal tage noget af Tyrens og Bukkens Blod og stryge det rundt om paa Alterets Horn,
19 Magazi ena awawaze pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kawiri kuliyeretsa ndi kulipatula kuchotsa zodetsa za Aisraeli.
og han skal syv Gange stænke noget af Blodet derpaa med sin Finger og saaledes rense det og hellige det for Israeliternes Urenheder.
20 “Aaroni akatsiriza mwambo wopepesera Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa, azibwera ndi mbuzi yamoyo kudzayipereka nsembe.
Naar han saa er færdig med at skaffe Helligdommen, Aabenbaringsteltet og Alteret Soning, skal han føre den levende Buk frem.
21 Aaroni asanjike manja ake pa mutu wa mbuziyo ndipo awulule pa mbuziyo zoyipa zonse ndi zowukira zonse za Aisraeli, kutanthauza machimo awo onse. Machimowo awayike pa mutu wa mbuziyo. Kenaka munthu amene anasankhidwa athamangitsire mbuziyo ku chipululu.
Aron skal lægge begge sine Hænder paa Hovedet af den levende Buk og over den bekende alle Israeliternes Misgerninger og alle deres Overtrædelser, alle deres Synder, og lægge dem paa Bukkens Hoved og saa sende den ud i Ørkenen ved en Mand, der holdes rede dertil.
22 Mbuziyo isenze machimo awo onse ndi kupita nawo kutali ndipo munthuyo aleke mbuziyo kuti ipite ku chipululuko.
Bukken skal da bære alle deres Misgerninger til et øde Land, og saa skal han slippe Bukken løs i Ørkenen.
23 “Pambuyo pake Aaroni alowe mu tenti ya msonkhano ndi kuvula zovala zosalala zija zimene anavala polowa ku Malo Wopatulika ndi kuzisiya komweko.
Derpaa skal Aron gaa ind i Aabenbaringsteltet, afføre sig Linnedklæderne, som han tog paa, da han gik ind i Helligdommen, og lægge dem der;
24 Asambe thupi lonse ku Malo Wopatulika ndi kuvala zovala zake za nthawi zonse. Kenaka atuluke ndi kukapereka nsembe yopsereza ya iye mwini, ndiponso nsembe yopsereza yoperekera anthu. Akatero ndiye kuti wachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake ndi a anthu.
saa skal han bade sit Legeme i Vand paa et helligt Sted, iføre sig sine sædvanlige Klæder og gaa ud og ofre sit eget Brændoffer og Folkets Brændoffer og saaledes skaffe sig og Folket Soning.
25 Mafuta a nyama yopepesera machimo awatenthe pa guwa lansembe.
Og Syndofferets Fedt skal han bringe som Røgoffer paa Alteret.
26 “Tsono munthu amene anaperekeza mbuzi yosenza machimo ija achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe ku msasa.
Men den, som fører Bukken ud til Azazel, skal tvætte sine Klæder og bade sit Legeme i Vand; derefter maa han komme ind i Lejren.
27 Ngʼombe ndi mbuzi zoperekera nsembe yopepesera machimo zimene magazi ake anabwera nawo kuti achitire mwambo wopepesera Malo Wopatulika, azitulutsire kunja kwa msasa. Koma zikopa zake, nyama yake ndi matumbo ake azitenthe.
Men Syndoffertyren og Syndofferbukken, hvis Blod blev baaret ind for at skaffe Soning i Helligdommen, skal man bringe uden for Lejren, og man skal brænde deres Hud og deres Kød og Skarn.
28 Munthu amene azitenthe achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe mu msasa.
Og den, der brænder dem, skal tvætte sine Klæder og bade sit Legeme; derefter maa han komme ind i Lejren.
29 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya: Mwezi wachisanu ndi chiwiri, pa tsiku la khumi la mwezi, mugonje pamaso pa Yehova. Musamagwire ntchito iliyonse, kaya ndinu mbadwa kapena mlendo amene akukhala pakati panu,
Det skal være eder en evig gyldig Anordning. Den tiende Dag i den syvende Maaned skal I faste og afholde eder fra alt Arbejde, baade den indfødte og den fremmede, der bor iblandt eder.
30 chifukwa tsiku limeneli kudzachitika mwambo wopepesera machimo anu, kukuyeretsani kuti mukhale oyeretsedwa ku machimo anu pamaso pa Yehova.
Thi den Dag skaffes der eder Soning til eders Renselse; fra alle eders Synder renses I for HERRENS Aasyn.
31 Limeneli ndi tsiku lanu la Sabata lopumula, ndipo muzigonja pamaso pa Yehova. Limeneli ndi lamulo lanu la muyaya.
Det skal være eder en fuldkommen Hviledag, og I skal faste: det skal være en evig gyldig Anordning.
32 Wansembe amene wadzozedwa ndi kupatulidwa kuti akhale wansembe kulowa mʼmalo mwa abambo ake ndiye azichita mwambo wopepesera machimo atavala zovala zake zosalala ndi zopatulika.
Præsten, som salves og indsættes til at gøre Præstetjeneste i. Stedet for sin Fader, skal skaffe Soning, han skal iføre sig Linnedklæderne, de hellige Klæder,
33 Adzachite mwambo wopepesera machimo Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Adzachitenso mwambo wopepesera anzake ndi gulu lonse la anthu.
og han skal skaffe det Allerhelligste Soning; og Aabenbaringsteltet og Alteret skal han skaffe Soning; og Præsterne og alt Folkets Forsamling skal han skaffe Soning.
34 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya. Mwambo wopepesera machimo uzichitika kamodzi pa chaka chifukwa cha machimo a anthu onse.” Ndipo Mose anachita monga momwe Yehova analamulira.
Det skal være eder en evig gyldig Anordning, for at der kan skaffes Israeliterne Soning for alle deres Synder een Gang om Aaret. Og Aron gjorde som HERREN bød Moses.

< Levitiko 16 >