< Levitiko 14 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Och Herren talade med Mose, och sade:
2 “Malamulo a munthu wakhate pa tsiku la kuyeretsedwa kwake ndi awa: Abwere naye kwa wansembe.
Detta är lagen om den spitelska, när han skall rensad varda: Han skall komma till Presten;
3 Wansembe atuluke kunja kwa msasa ndipo amuonetsetse wodwalayo. Ngati munthu wakhateyo wachira,
Och Presten skall gå utu lägret, och bese huru spitelskosårnaden är på dem spitelsko hel vorden;
4 wansembe alamule anthu kuti amutengere wodwala woti ayeretsedweyo, mbalame zamoyo ziwiri zomwe Ayuda amaloledwa kudya, nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope.
Och skall bjuda honom, som rensas skall, att han tager två lefvande foglar, de som rene äro, och cederträ, och rosenfärgoull, och isop;
5 Wansembe alamule anthuwo kuti mbalame imodzi ayiphere mu mʼphika wa dothi pamwamba pa madzi abwino.
Och skall bjuda att slagta den ena foglen uti ett lerkärile vid rinnande vatten;
6 Kenaka wansembe atenge mbalame yamoyo ija ndi kuyinyika pamodzi ndi nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope kaja mʼmagazi ambalame imene anayiphera pamwamba pa madzi abwino.
Och skall taga den lefvande foglen med cederträt, rosenfärgoullen, och isopen, och doppa uti den slagtade foglens blod vid rinnande vatten;
7 Wansembe awaze magazi kasanu ndi kawiri pa munthu woti amuyeretse khateyo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa. Kenaka wansembe awulutsire ku thengo mbalame yamoyoyo.
Och stänka på honom, som af spitelskone rensas skall, sju resor; och rensa honom alltså, och låta den lefvande foglen flyga i fria markena.
8 “Munthu amene wayeretsedwa uja achape zovala zake, amete tsitsi lake lonse, ndipo asambe mʼmadzi. Akatero adzakhala woyeretsedwa. Atatha zimenezi munthuyo apite ku msasa wake koma akhale kunja kwa msasawo kwa masiku asanu ndi awiri.
Men den rensade skall två sin kläder, och raka allt sitt hår af, och bada sig i vattne, och så är han ren; sedan gånge han in i lägret, dock skall han blifva utan sitt tjäll i sju dagar.
9 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri amete tsitsi lake lonse: amete kumutu, ndevu zake, nsidze zake pamodzi ndi tsitsi lina lonse. Kenaka achape zovala zake ndi kusamba mʼmadzi, ndipo adzakhala woyeretsedwa.
Och på sjunde dagen skall han raka allt sitt hår af hufvudet, skägget och ögonbrynen, så att allt hår blifver afrakadt; och skall två sin kläder, och bada sitt kött i vattne, och så är han ren.
10 “Pa tsiku lachisanu ndi chitatu munthuyo atenge ana ankhosa aamuna awiri ndi mwana wankhosa wamkazi wa chaka chimodzi. Zonsezi zikhale zopanda chilema. Atengenso chopereka chachakudya cha ufa wosalala wa makilogalamu atatu wosakaniza ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita.
Och på åttonde dagen skall han taga tu lamb, de utan vank äro, och ett årsgammalt får utan vank, och tre tiungar semlomjöl till spisoffer, blandadt med oljo, och en log oljo.
11 Wansembe amene ati ayeretse munthu wodwalayo amuyimitse munthuyo ali ndi zopereka zake zonse pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
Då skall Presten ställa den rensada och dessa ting fram för Herran, för dörrena af vittnesbördsens tabernakel;
12 “Ndipo wansembe atenge mwana wankhosa wamwamuna mmodzi ndi kumupereka kuti akhale nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita. Wansembe aziweyule zonsezi pamaso pa Yehova kuti zikhale chopereka choweyula.
Och skall taga det ena lambet, och offra det till ett skuldoffer med den log oljo, och skall sådant veftoffra för Herranom;
13 Mwana wankhosayo amuphere pa malo amene amaphera nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yopsereza, kutanthauza malo opatulika. Monga zimakhalira ndi chopereka chopepesera machimo, chopereka ichi ndi chake cha wansembe ndipo ndi chopereka choyera kopambana.
Och sedan slagta lambet, der man slagtar syndoffret och bränneoffret, som är på heligt rum; ty såsom syndoffret, så hörer ock skuldoffret Prestenom till; ty det är det aldrahelgasta.
14 Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera kupalamula ndi kuwapaka pa msonga pa khutu lakumanja la munthu woti ayeretsedweyo. Apakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndi chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
Och Presten skall taga af skuldoffrens blod, och stryka på högra örnatimpen af den rensada, och på tumman af hans högra hand, och på största tåna af hans högra fot.
15 Wansembe atengeko mafuta pangʼono, nʼkuwathira mʼdzanja lake lamanzere,
Sedan skall han taga af oljone utu logen, och gjuta den i sin venstra hand;
16 aviyike chala chake cha ku dzanja lamanja mʼmafuta amene ali mʼdzanja lamanzerewo, ndi kuwaza mafutawo ndi chala chakecho kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
Och doppa med sitt högra finger i oljona, den i hans venstra hand är, och stänka oljona med sitt finger sju resor för Herranom.
17 Wansembe apake mafuta otsala mʼdzanja lake pa khutu lakumanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Awapakenso pa chala chake chachikulu cha ku dzanja lamanja ndiponso pa chala chake chachikulu cha ku phazi lakumanja, pamalo pamene anali atapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula paja.
Men det öfver blifver af oljone i hans hand, skall han gjuta på den högra örnatimpen af honom, som rensad är, och på den högra tumman, och på den stora tåna af hans högra fot, ofvanuppå skuldoffrens blod.
18 Mafuta onse otsala mʼdzanja la wansembe awathire pamutu pa munthu woti ayeretsedwe uja, ndipo potero adzachita mwambo womupepesera pamaso pa Yehova.
Det qvart är af oljone i hans hand, skall han slå på hans hufvud, som rensader är, och försona honom för Herranom;
19 “Kenaka wansembe apereke nsembe yopepesera machimo kuti achite mwambo womupepesera munthu woti ayeretsedwe khate lake uja. Atatha kuchita zimenezi, wansembe aphe nyama ya nsembe yopsereza
Och skall göra syndoffer, och försona den rensada för hans orenlighets skull; och skall sedan slagta bränneoffret;
20 ndi kuyipereka pa guwa, pamodzi ndi nsembe yachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera munthu wodzayeretsedwayo, ndipo adzakhala woyera.
Och skall offra det på altaret samt med spisoffret, och försona honom, så är han ren.
21 “Ngati munthu woti ayeretsedweyo ndi wosauka ndipo sangathe kupeza zinthu zimenezi, apereke mwana wankhosa wamwamuna monga nsembe yopepesera kupalamula ndipo ayiweyule pochita mwambo womupepesera. Aperekenso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala osakaniza ndi mafuta kuti ikhale nsembe yachakudya, pamodzi ndi mafuta wokwanira limodzi mwa magawo atatu a lita.
Är han fattig, och icke så mycket förvärfvar med sine hand, så tage ett lamb för sitt skuldoffer, till att veftoffra, till att försona honom, och en tiung af semlomjöl, blandad med oljo till spisoffer, och en log oljo;
22 Aperekenso njiwa ziwiri kapena mawunda awiri zomwe iye angathe kuzipeza. Imodzi ikhale nsembe yopepesera machimo, ndi inayo ikhale ya nsembe yopsereza.
Och två turturdufvor, eller två unga dufvor, de han med sine hand förvärfva kan; den ena vare till ett syndoffer, den andra till ett bränneoffer;
23 “Pa tsiku lachisanu ndi chitatu zonsezo abwere nazo kwa wansembe, pa khomo pa tenti ya msonkhano, pamaso pa Yehova kuti munthuyo ayeretsedwe.
Och bäre dem till Presten, på åttonde dagen efter hans renselse, inför dörrena af vittnesbördsens tabernakel för Herranom.
24 Wansembe atenge mwana wankhosa wopereka nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta aja, ndipo aziweyule kuti zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
Då skall Presten taga skuldoffrens lamb, och den log oljo, och skall det allt veftoffra för Herranom;
25 Wansembe aphe nkhosa yopereka nsembe yopepesera kupalamula ndipo atenge magazi ake ndi kuwapaka pa msonga ya khutu lakumanja la munthu amene ayeretsedweyo. Awapakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndiponso pa chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
Och slagta skuldoffrens lamb, och taga af samma skuldoffers blod, och stryka den rensada på hans högra örnatimp, och på tumman af hans högra hand, och på den stora tåna af hans högra fot;
26 Kenaka wansembe athire mafuta mʼdzanja lake lamanzere,
Och gjuta oljona i sina venstra hand;
27 ndipo ndi chala chake cha ku dzanja lamanja awaze mafutawo kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
Och stänka med sitt högra finger oljona, som i hans venstra hand är, sju resor för Herranom.
28 Apakenso mafuta omwewo amene ali mʼdzanja lake lamanja pa msonga ya khutu la kudzanja lamanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Apakenso pa chala chachikulu cha phazi lakumanja, pamalo pamene anapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula.
Det qvart blifver i hans hand, skall han låta på högra örnatimpen af den rensada, och på tumman af hans högra hand, och på stora tåna af hans högra fot, ofvanuppå skuldoffrens blod.
29 Mafuta onse otsala amene ali mʼdzanja la wansembe awapake pamutu pa munthu amene ayeretsedweyo kuti amuchitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.
Det qvart är i hans hand af oljone, skall han låta på hufvudet af den rensada, till att försona honom för Herranom;
30 Ndipo munthuyo apereke njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri, molingana ndi mmene anapezeramo,
Och sedan göra ett syndoffer utaf den ena turturdufvone, eller unga dufvone, såsom hans hand hafver kunnat förvärfva;
31 imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza, pamodzi ndi chopereka chachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera machimo a munthu woti ayeretsedwe.
Utaf den andra ett bränneoffer, samt med spisoffret. Och alltså skall Presten försona den rensada för Herranom.
32 “Amenewa ndi malamulo a munthu wakhate amene alibe zinthu zoti apereke pamene akuyeretsedwa.
Detta vare lagen för den spitelska, som icke kan med sine hand förvärfva det till hans renselse hörer.
33 “Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
Och Herren talade med Mose och Aaron, och sade:
34 Mukakalowa mʼdziko la Kanaani limene ndikukupatsani kuti likhale lanu, ndipo Ine ndikakabweretsa ndere zoyanga mʼnyumba mʼdziko limenelo,
När I kommen in uti Canaans land, det jag eder till besittning gifva skall, och jag der i någro edor besittninges huse en spitelskosårnad gifver;
35 mwini wake nyumbayo adzapite kwa wansembe ndi kukamuwuza kuti, ‘Ndaona chinthu chooneka ngati ndere mʼnyumba mwanga.’
Så skall han, som huset tillhörer, komma, undervisa det Prestenom, och säga: Det synes såsom en spitelskosårnad är i mino huse.
36 Tsono wansembe alamule kuti anthu atulutse zinthu zonse mʼnyumbamo iye asanalowemo ndi kukaonetsetsa ndereyo kuti mʼnyumbamo musapezeke chinthu choti achitchule chodetsedwa. Izi zitachitika, wansembe alowe mʼnyumbamo ndi kukaonamo.
Då skall Presten säga dem, att de skola rymma utu huset förra än Presten går derin, till att bese sårnaden; på det att allt, det i huset är, icke skall varda orent. Sedan skall Presten gå in till att bese huset.
37 Iye aonetsetse nderezo. Tsono akapeza kuti nderezo zili mʼkhoma la nyumba, ndipo ngati zili ndi mawanga obiriwira kapena ofiirira, komanso zikuoneka kuti zalowerera mpaka mʼkati mwa khoma,
När han nu ser sårnaden, och finner att på husens väggar gula eller rödletta gropar äro, och deras anseende djupare in är än väggen eljest är;
38 wansembe atuluke mʼnyumbamo ndi kupita pa khomo, ndipo ayitseke nyumbayo masiku asanu ndi awiri.
Så skall han gå utu huset genom dörrena, och igenlycka huset i sju dagar.
39 Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri wansembe abwerenso kudzayangʼana mʼnyumbamo. Ngati ndere yafalikira mʼmakoma a nyumbayo,
Och när han på sjunde dagen igenkommer, och ser att sårnaden hafver ätit sig vidare på väggene af huset;
40 wansembe alamule kuti anthu agumule miyala imene muli nderezo ndipo akayitaye kudzala la kunja kwa mzinda.
Så skall han bjuda dem utbryta stenarna, der den sårnaden uti är, och kasta det ut för staden på ett orent rum.
41 Wansembe awuze anthu kuti apale makoma onse a mʼkati mwa nyumbayo, ndipo zopalidwazo akazitaye ku malo odetsedwa a kunja kwa mudzi.
Och huset skall man skrapa innantill allt omkring, och kasta det afskrapade stoftet ut för staden på ett orent rum;
42 Tsono anthuwo atenge miyala ina ndi kuyilowetsa mʼmalo mwa miyala imene anagumula ija ndipo atenge dothi latsopano ndi kumata nyumbayo.
Och taga andra stenar, och sätta dem i samma staden; och taga annan kalk, och bestryka huset med.
43 “Ngati ndere iwonekanso mʼnyumbamo atagumula kale miyala ndiponso atayipala kale ndi kuyimatanso,
Om då sårnaden igenkommer, och brister ut på huset, sedan man hafver uttagit stenarna, skrapat huset, och bestrukit det på nytt;
44 wansembe apite kukayionetsetsenso ndipo ngati nderezo zafalikira mʼnyumbamo, ndiye kuti ndere zimenezo ndi zoopsa. Nyumba imeneyo ndi yodetsedwa.
Så skall Presten gå derin. Och när han ser att sårnaden hafver vidare ätit sig på husena, så är det visserliga en frätande spitelska på huset; och är orent.
45 Agwetse nyumbayo, ndipo miyala yake, matabwa pamodzi ndi dothi lake lonse, zonse akazitaye kudzala lodetsedwa, kunja kwa mzinda.
Derföre skall man bryta huset ned, både sten och trä, och allt stoftet af husena föra ut för staden på ett orent rum.
46 “Aliyense amene alowa mʼnyumbamo itatsekedwa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
Och den som går in i huset, så länge det tillslutet är, han är oren intill aftonen.
47 Munthu amene wagona mʼnyumbamo kapena kudyeramo ayenera kuchapa zovala zake.
Och den derinne ligger, eller äter derinne, han skall två sin kläder.
48 “Koma ngati pambuyo pa kuyimata, wansembe abwera kudzaonetsetsa mʼnyumbamo napeza kuti ndereyo sinafalikire, iye alengeze kuti nyumbayo ndi yoyeretsedwa, chifukwa ndereyo yatha.
Hvar nu Presten ser, då han går derin, att sårnaden icke vidare hafver ätit sig på huset, sedan huset bestruket är; så skall han säga det rent; ty sårnaden är hel vorden;
49 Kuti nyumbayo iyeretsedwe, mwini wake atenge mbalame ziwiri, kanthambi kamkungudza, kansalu kofiirira ndi kachitsamba ka hisope.
Och skall taga till syndoffer för huset, två foglar, cedreträ, och rosenfärgad ull, och isop;
50 Wansembe aphe mbalame imodzi pamwamba pa madzi abwino mu mʼphika wa dothi.
Och slagta den ena foglen uti ett lerkäril vid rinnande vatten;
51 Kenaka atenge kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope, kansalu kofiirira pamodzi ndi mbalame yamoyo ija, zonsezi aziviyike mʼmagazi a mbalame yophedwa ija, ndiponso mʼmadzi abwino aja, ndipo awaze nyumbayo kasanu ndi kawiri
Och skall taga det cederträt, rosenfärgada ullen, isopen och den lefvande foglen, och doppa honom uti den slagtada foglens blod vid rinnande vatten, och stänka huset sju resor;
52 Akatero ndiye kuti wayeretsa nyumbayo ndi magazi a mbalame, madzi abwino, mbalame yamoyo, kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope ndi kansalu kofiirira.
Och skall alltså skära huset med foglens blod, och med det rinnande vattnet, med den lefvande foglen, med cedreträt, med isopen, och med rosenfärgada ullen;
53 Kenaka ayiwulutsire mbalame yamoyo ija kuthengo, kunja kwa mzinda. Pamenepo ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera nyumbayo, ndipo idzakhala yoyeretsedwa.”
Och skall låta den lefvande foglen flyga ut för staden i fria markena, och försona huset; så är det rent.
54 Amenewa ndiwo malamulo a nthenda ya khate, bala lonyerenyetsa,
Detta är lagen om all spitelskos och skabbs sårnad;
55 nguwi za pa zovala, ndere za mʼnyumba,
Om kläders spitelsko, och huses;
56 khate la chithupsa, khate la mʼbuko ndi khate la banga
Om blemmor, skabb och etterhvitt;
57 kuti mudziwe ngati chinthucho ndi choyeretsedwa kapena chodetsedwa. Amenewa ndiwo malamulo a nthenda zonse za khate.
På det man skall veta, när något orent eller rent är. Detta är lagen om spitelsko.

< Levitiko 14 >