< Levitiko 14 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
И сказал Господь Моисею, говоря:
2 “Malamulo a munthu wakhate pa tsiku la kuyeretsedwa kwake ndi awa: Abwere naye kwa wansembe.
вот закон о прокаженном, когда надобно его очистить: приведут его к священнику;
3 Wansembe atuluke kunja kwa msasa ndipo amuonetsetse wodwalayo. Ngati munthu wakhateyo wachira,
священник выйдет вон из стана, и если священник увидит, что прокаженный исцелился от болезни прокажения,
4 wansembe alamule anthu kuti amutengere wodwala woti ayeretsedweyo, mbalame zamoyo ziwiri zomwe Ayuda amaloledwa kudya, nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope.
то священник прикажет взять для очищаемого двух птиц живых чистых, кедрового дерева, червленую нить и иссопа,
5 Wansembe alamule anthuwo kuti mbalame imodzi ayiphere mu mʼphika wa dothi pamwamba pa madzi abwino.
и прикажет священник заколоть одну птицу над глиняным сосудом, над живою водою;
6 Kenaka wansembe atenge mbalame yamoyo ija ndi kuyinyika pamodzi ndi nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope kaja mʼmagazi ambalame imene anayiphera pamwamba pa madzi abwino.
а сам он возьмет живую птицу, кедровое дерево, червленую нить и иссоп, и омочит их и живую птицу в крови птицы заколотой над живою водою,
7 Wansembe awaze magazi kasanu ndi kawiri pa munthu woti amuyeretse khateyo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa. Kenaka wansembe awulutsire ku thengo mbalame yamoyoyo.
и покропит на очищаемого от проказы семь раз, и объявит его чистым, и пустит живую птицу в поле.
8 “Munthu amene wayeretsedwa uja achape zovala zake, amete tsitsi lake lonse, ndipo asambe mʼmadzi. Akatero adzakhala woyeretsedwa. Atatha zimenezi munthuyo apite ku msasa wake koma akhale kunja kwa msasawo kwa masiku asanu ndi awiri.
Очищаемый омоет одежды свои, острижет все волосы свои, омоется водою, и будет чист; потом войдет в стан и пробудет семь дней вне шатра своего;
9 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri amete tsitsi lake lonse: amete kumutu, ndevu zake, nsidze zake pamodzi ndi tsitsi lina lonse. Kenaka achape zovala zake ndi kusamba mʼmadzi, ndipo adzakhala woyeretsedwa.
в седьмой день обреет все волосы свои, голову свою, бороду свою, брови глаз своих, все волосы свои обреет, и омоет одежды свои, и омоет тело свое водою, и будет чист;
10 “Pa tsiku lachisanu ndi chitatu munthuyo atenge ana ankhosa aamuna awiri ndi mwana wankhosa wamkazi wa chaka chimodzi. Zonsezi zikhale zopanda chilema. Atengenso chopereka chachakudya cha ufa wosalala wa makilogalamu atatu wosakaniza ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita.
в восьмой день возьмет он двух овнов однолетних без порока, и одну овцу однолетнюю без порока, и три десятых части ефы пшеничной муки, смешанной с елеем, в приношение хлебное, и один лог елея;
11 Wansembe amene ati ayeretse munthu wodwalayo amuyimitse munthuyo ali ndi zopereka zake zonse pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
священник очищающий поставит очищаемого человека с ними пред Господом у входа скинии собрания;
12 “Ndipo wansembe atenge mwana wankhosa wamwamuna mmodzi ndi kumupereka kuti akhale nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita. Wansembe aziweyule zonsezi pamaso pa Yehova kuti zikhale chopereka choweyula.
и возьмет священник одного овна, и представит его в жертву повинности, и лог елея, и принесет это, потрясая пред Господом;
13 Mwana wankhosayo amuphere pa malo amene amaphera nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yopsereza, kutanthauza malo opatulika. Monga zimakhalira ndi chopereka chopepesera machimo, chopereka ichi ndi chake cha wansembe ndipo ndi chopereka choyera kopambana.
и заколет овна на том месте, где заколают жертву за грех и всесожжение, на месте святом, ибо сия жертва повинности, подобно жертве за грех, принадлежит священнику: это великая святыня;
14 Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera kupalamula ndi kuwapaka pa msonga pa khutu lakumanja la munthu woti ayeretsedweyo. Apakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndi chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
и возьмет священник крови жертвы повинности, и возложит священник на край правого уха очищаемого и на большой палец правой руки его и на большой палец правой ноги его;
15 Wansembe atengeko mafuta pangʼono, nʼkuwathira mʼdzanja lake lamanzere,
и возьмет священник из лога елея и польет на левую свою ладонь;
16 aviyike chala chake cha ku dzanja lamanja mʼmafuta amene ali mʼdzanja lamanzerewo, ndi kuwaza mafutawo ndi chala chakecho kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
и омочит священник правый перст свой в елей, который на левой ладони его, и покропит елеем с перста своего семь раз пред лицем Господа;
17 Wansembe apake mafuta otsala mʼdzanja lake pa khutu lakumanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Awapakenso pa chala chake chachikulu cha ku dzanja lamanja ndiponso pa chala chake chachikulu cha ku phazi lakumanja, pamalo pamene anali atapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula paja.
оставшийся же елей, который на ладони его, возложит священник на край правого уха очищаемого, на большой палец правой руки его и на большой палец правой ноги его, на места, где кровь жертвы повинности;
18 Mafuta onse otsala mʼdzanja la wansembe awathire pamutu pa munthu woti ayeretsedwe uja, ndipo potero adzachita mwambo womupepesera pamaso pa Yehova.
а остальной елей, который на ладони священника, возложит он на голову очищаемого, и очистит его священник пред лицем Господа.
19 “Kenaka wansembe apereke nsembe yopepesera machimo kuti achite mwambo womupepesera munthu woti ayeretsedwe khate lake uja. Atatha kuchita zimenezi, wansembe aphe nyama ya nsembe yopsereza
И совершит священник жертву за грех, и очистит очищаемого от нечистоты его; после того заколет жертву всесожжения;
20 ndi kuyipereka pa guwa, pamodzi ndi nsembe yachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera munthu wodzayeretsedwayo, ndipo adzakhala woyera.
и возложит священник всесожжение и приношение хлебное на жертвенник; и очистит его священник, и он будет чист.
21 “Ngati munthu woti ayeretsedweyo ndi wosauka ndipo sangathe kupeza zinthu zimenezi, apereke mwana wankhosa wamwamuna monga nsembe yopepesera kupalamula ndipo ayiweyule pochita mwambo womupepesera. Aperekenso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala osakaniza ndi mafuta kuti ikhale nsembe yachakudya, pamodzi ndi mafuta wokwanira limodzi mwa magawo atatu a lita.
Если же он беден и не имеет достатка, то пусть возьмет одного овна в жертву повинности для потрясания, чтоб очистить себя, и одну десятую часть ефы пшеничной муки, смешанной с елеем, в приношение хлебное, и лог елея,
22 Aperekenso njiwa ziwiri kapena mawunda awiri zomwe iye angathe kuzipeza. Imodzi ikhale nsembe yopepesera machimo, ndi inayo ikhale ya nsembe yopsereza.
и двух горлиц или двух молодых голубей, что достанет рука его, одну из птиц в жертву за грех, а другую во всесожжение;
23 “Pa tsiku lachisanu ndi chitatu zonsezo abwere nazo kwa wansembe, pa khomo pa tenti ya msonkhano, pamaso pa Yehova kuti munthuyo ayeretsedwe.
и принесет их в восьмой день очищения своего к священнику ко входу скинии собрания, пред лице Господа;
24 Wansembe atenge mwana wankhosa wopereka nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta aja, ndipo aziweyule kuti zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
священник возьмет овна жертвы повинности и лог елея, и принесет это священник, потрясая пред Господом;
25 Wansembe aphe nkhosa yopereka nsembe yopepesera kupalamula ndipo atenge magazi ake ndi kuwapaka pa msonga ya khutu lakumanja la munthu amene ayeretsedweyo. Awapakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndiponso pa chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
и заколет овна в жертву повинности, и возьмет священник крови жертвы повинности, и возложит на край правого уха очищаемого и на большой палец правой руки его и на большой палец правой ноги его;
26 Kenaka wansembe athire mafuta mʼdzanja lake lamanzere,
и нальет священник елея на левую свою ладонь,
27 ndipo ndi chala chake cha ku dzanja lamanja awaze mafutawo kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
и елеем, который на левой ладони его, покропит священник с правого перста своего семь раз пред лицем Господним;
28 Apakenso mafuta omwewo amene ali mʼdzanja lake lamanja pa msonga ya khutu la kudzanja lamanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Apakenso pa chala chachikulu cha phazi lakumanja, pamalo pamene anapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula.
и возложит священник елея, который на ладони его, на край правого уха очищаемого, на большой палец правой руки его и на большой палец правой ноги его, на места, где кровь жертвы повинности;
29 Mafuta onse otsala amene ali mʼdzanja la wansembe awapake pamutu pa munthu amene ayeretsedweyo kuti amuchitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.
а остальной елей, который на ладони священника, возложит он на голову очищаемого, чтоб очистить его пред лицем Господа;
30 Ndipo munthuyo apereke njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri, molingana ndi mmene anapezeramo,
и принесет одну из горлиц или одного из молодых голубей, что достанет рука очищаемого,
31 imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza, pamodzi ndi chopereka chachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera machimo a munthu woti ayeretsedwe.
из того, что достанет рука его, одну птицу в жертву за грех, а другую во всесожжение, вместе с приношением хлебным; и очистит священник очищаемого пред лицем Господа.
32 “Amenewa ndi malamulo a munthu wakhate amene alibe zinthu zoti apereke pamene akuyeretsedwa.
Вот закон о прокаженном, который во время очищения своего не имеет достатка.
33 “Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
И сказал Господь Моисею и Аарону, говоря:
34 Mukakalowa mʼdziko la Kanaani limene ndikukupatsani kuti likhale lanu, ndipo Ine ndikakabweretsa ndere zoyanga mʼnyumba mʼdziko limenelo,
когда войдете в землю Ханаанскую, которую Я даю вам во владение, и Я наведу язву проказы на домы в земле владения вашего,
35 mwini wake nyumbayo adzapite kwa wansembe ndi kukamuwuza kuti, ‘Ndaona chinthu chooneka ngati ndere mʼnyumba mwanga.’
тогда тот, чей дом, должен пойти и сказать священнику: у меня на доме показалась как бы язва.
36 Tsono wansembe alamule kuti anthu atulutse zinthu zonse mʼnyumbamo iye asanalowemo ndi kukaonetsetsa ndereyo kuti mʼnyumbamo musapezeke chinthu choti achitchule chodetsedwa. Izi zitachitika, wansembe alowe mʼnyumbamo ndi kukaonamo.
Священник прикажет опорожнить дом, прежде нежели войдет священник осматривать язву, чтобы не сделалось нечистым все, что в доме; после сего придет священник осматривать дом.
37 Iye aonetsetse nderezo. Tsono akapeza kuti nderezo zili mʼkhoma la nyumba, ndipo ngati zili ndi mawanga obiriwira kapena ofiirira, komanso zikuoneka kuti zalowerera mpaka mʼkati mwa khoma,
Если он, осмотрев язву, увидит, что язва на стенах дома состоит из зеленоватых или красноватых ямин, которые окажутся углубленными в стене,
38 wansembe atuluke mʼnyumbamo ndi kupita pa khomo, ndipo ayitseke nyumbayo masiku asanu ndi awiri.
то священник выйдет из дома к дверям дома и запрет дом на семь дней.
39 Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri wansembe abwerenso kudzayangʼana mʼnyumbamo. Ngati ndere yafalikira mʼmakoma a nyumbayo,
В седьмой день опять придет священник, и если увидит, что язва распространилась по стенам дома,
40 wansembe alamule kuti anthu agumule miyala imene muli nderezo ndipo akayitaye kudzala la kunja kwa mzinda.
то священник прикажет выломать камни, на которых язва, и бросить их вне города на место нечистое;
41 Wansembe awuze anthu kuti apale makoma onse a mʼkati mwa nyumbayo, ndipo zopalidwazo akazitaye ku malo odetsedwa a kunja kwa mudzi.
а дом внутри пусть весь оскоблят, и обмазку, которую отскоблят, высыпят вне города на место нечистое;
42 Tsono anthuwo atenge miyala ina ndi kuyilowetsa mʼmalo mwa miyala imene anagumula ija ndipo atenge dothi latsopano ndi kumata nyumbayo.
и возьмут другие камни, и вставят вместо тех камней, и возьмут другую обмазку, и обмажут дом.
43 “Ngati ndere iwonekanso mʼnyumbamo atagumula kale miyala ndiponso atayipala kale ndi kuyimatanso,
Если язва опять появится и будет цвести на доме после того, как выломали камни и оскоблили дом и обмазали,
44 wansembe apite kukayionetsetsenso ndipo ngati nderezo zafalikira mʼnyumbamo, ndiye kuti ndere zimenezo ndi zoopsa. Nyumba imeneyo ndi yodetsedwa.
то священник придет и осмотрит, и если язва на доме распространилась, то это едкая проказа на доме, нечист он;
45 Agwetse nyumbayo, ndipo miyala yake, matabwa pamodzi ndi dothi lake lonse, zonse akazitaye kudzala lodetsedwa, kunja kwa mzinda.
должно разломать сей дом, и камни его и дерево его и всю обмазку дома вынести вне города на место нечистое;
46 “Aliyense amene alowa mʼnyumbamo itatsekedwa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
кто входит в дом во все время, когда он заперт, тот нечист до вечера;
47 Munthu amene wagona mʼnyumbamo kapena kudyeramo ayenera kuchapa zovala zake.
и кто спит в доме том, тот должен вымыть одежды свои и нечист будет до вечера; и кто ест в доме том, тот должен вымыть одежды свои и нечист будет до вечера.
48 “Koma ngati pambuyo pa kuyimata, wansembe abwera kudzaonetsetsa mʼnyumbamo napeza kuti ndereyo sinafalikire, iye alengeze kuti nyumbayo ndi yoyeretsedwa, chifukwa ndereyo yatha.
Если же священник придет и увидит, что язва на доме не распространилась после того, как обмазали дом, то священник объявит дом чистым, потому что язва прошла.
49 Kuti nyumbayo iyeretsedwe, mwini wake atenge mbalame ziwiri, kanthambi kamkungudza, kansalu kofiirira ndi kachitsamba ka hisope.
И чтобы очистить дом, возьмет он две птицы, кедрового дерева, червленую нить и иссопа,
50 Wansembe aphe mbalame imodzi pamwamba pa madzi abwino mu mʼphika wa dothi.
и заколет одну птицу над глиняным сосудом, над живою водою;
51 Kenaka atenge kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope, kansalu kofiirira pamodzi ndi mbalame yamoyo ija, zonsezi aziviyike mʼmagazi a mbalame yophedwa ija, ndiponso mʼmadzi abwino aja, ndipo awaze nyumbayo kasanu ndi kawiri
и возьмет кедровое дерево и иссоп, и червленую нить и живую птицу, и омочит их в крови птицы заколотой и в живой воде, и покропит дом семь раз;
52 Akatero ndiye kuti wayeretsa nyumbayo ndi magazi a mbalame, madzi abwino, mbalame yamoyo, kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope ndi kansalu kofiirira.
и очистит дом кровью птицы и живою водою, и живою птицею и кедровым деревом, и иссопом и червленою нитью;
53 Kenaka ayiwulutsire mbalame yamoyo ija kuthengo, kunja kwa mzinda. Pamenepo ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera nyumbayo, ndipo idzakhala yoyeretsedwa.”
и пустит живую птицу вне города в поле и очистит дом, и будет чист.
54 Amenewa ndiwo malamulo a nthenda ya khate, bala lonyerenyetsa,
Вот закон о всякой язве проказы и о паршивости,
55 nguwi za pa zovala, ndere za mʼnyumba,
и о проказе на одежде и на доме,
56 khate la chithupsa, khate la mʼbuko ndi khate la banga
и об опухоли, и о лишаях, и о пятнах,
57 kuti mudziwe ngati chinthucho ndi choyeretsedwa kapena chodetsedwa. Amenewa ndiwo malamulo a nthenda zonse za khate.
чтобы указать, когда это нечисто и когда чисто. Вот закон о проказе.

< Levitiko 14 >