< Levitiko 14 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
LEUM GOD El sang nu sel Moses
2 “Malamulo a munthu wakhate pa tsiku la kuyeretsedwa kwake ndi awa: Abwere naye kwa wansembe.
oakwuk ten inge nu ke aknasnas lun sie mwet ma kwela liki sie mas sensenkinyuk ke manol. Ke len se ma ac fwackyang mu el nasnasla uh, ac fah utuku el nu yurin mwet tol,
3 Wansembe atuluke kunja kwa msasa ndipo amuonetsetse wodwalayo. Ngati munthu wakhateyo wachira,
ac mwet tol fah usalla nu likin nien aktuktuk uh ac tuni manol. Mas lal uh fin wanginla,
4 wansembe alamule anthu kuti amutengere wodwala woti ayeretsedweyo, mbalame zamoyo ziwiri zomwe Ayuda amaloledwa kudya, nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope.
na mwet tol el fah sap in utuku luo won ma nasnas uh, wi sie ipin sak cedar, sie polo ah srusra, ac sie lah srisrik ke sak hyssop.
5 Wansembe alamule anthuwo kuti mbalame imodzi ayiphere mu mʼphika wa dothi pamwamba pa madzi abwino.
Na mwet tol el fah sap in anwuki sie sin won luo ah luin sie pol eot ma kof in unon nasnas oan loac.
6 Kenaka wansembe atenge mbalame yamoyo ija ndi kuyinyika pamodzi ndi nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope kaja mʼmagazi ambalame imene anayiphera pamwamba pa madzi abwino.
El fah eis won se ma moul ah, wi ipin sak cedar sac, polo ah srusra sac, ac sak hyssop sac, ac isongya ma inge kewa nu in srah ke won se ma anwuki ah.
7 Wansembe awaze magazi kasanu ndi kawiri pa munthu woti amuyeretse khateyo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa. Kenaka wansembe awulutsire ku thengo mbalame yamoyoyo.
El fah aksroksrokye mwet se ma ac aknasnasyeyuk liki mas ke manol pacl itkosr ke srah, na el fah fahkak lah mwet sac nasnasla. El fah fuhlela won se ma moul ah in sohkla.
8 “Munthu amene wayeretsedwa uja achape zovala zake, amete tsitsi lake lonse, ndipo asambe mʼmadzi. Akatero adzakhala woyeretsedwa. Atatha zimenezi munthuyo apite ku msasa wake koma akhale kunja kwa msasawo kwa masiku asanu ndi awiri.
Mwet sac fah ohlla nuknuk lal uh, resaela aunsuf kacl uh nufon, ac yihla; na el fah nasnas. El ac ku in ilyak nu ke nien aktuktuk uh, tusruktu el enenu in mutana likin lohm nuknuk sel ke len itkosr.
9 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri amete tsitsi lake lonse: amete kumutu, ndevu zake, nsidze zake pamodzi ndi tsitsi lina lonse. Kenaka achape zovala zake ndi kusamba mʼmadzi, ndipo adzakhala woyeretsedwa.
Ke len se akitkosr el fah sifilpa resaela sifal, altal, inyal, ac unac nukewa ke manol. El fah ohlla nuknuk lal ac yihla, na el fah nasnasla.
10 “Pa tsiku lachisanu ndi chitatu munthuyo atenge ana ankhosa aamuna awiri ndi mwana wankhosa wamkazi wa chaka chimodzi. Zonsezi zikhale zopanda chilema. Atengenso chopereka chachakudya cha ufa wosalala wa makilogalamu atatu wosakaniza ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita.
Ke len se akoalkosr el fah use lukwa sheep fusr mukul ac soko ma mutan ma yac se matwa su wangin kutena ma koluk ke mano, wi paun limekosr ke flao ma kulamisyak ke oil in olive, ac sie cup ke oil in olive.
11 Wansembe amene ati ayeretse munthu wodwalayo amuyimitse munthuyo ali ndi zopereka zake zonse pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
Mwet tol el fah eis mwet sac ac mwe kisa inge nukewa nu ke acn in utyak nu ke Lohm Nuknuk Mutal, nien muta lun LEUM GOD.
12 “Ndipo wansembe atenge mwana wankhosa wamwamuna mmodzi ndi kumupereka kuti akhale nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita. Wansembe aziweyule zonsezi pamaso pa Yehova kuti zikhale chopereka choweyula.
Na mwet tol el fah eis soko sin sheep fusr mukul inge, wi cup se ke oil in olive, ac kisakin tuh in sie mwe kisa in akfalye ma koluk lukma. El fah kisakin ma inge tuh in sie mwe sang sriyukla nu sin LEUM GOD.
13 Mwana wankhosayo amuphere pa malo amene amaphera nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yopsereza, kutanthauza malo opatulika. Monga zimakhalira ndi chopereka chopepesera machimo, chopereka ichi ndi chake cha wansembe ndipo ndi chopereka choyera kopambana.
El fah uniya sheep fusr soko ah in acn mutal ma mwe kisa lun ma koluk ac mwe kisa firir uh anwuki we. El enenu in oru ouinge mweyen kisa in akfalye ma koluk lukma uh oapana kisa ke ma koluk, kewana ma lun mwet tol, ac ma inge arulana mutal.
14 Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera kupalamula ndi kuwapaka pa msonga pa khutu lakumanja la munthu woti ayeretsedweyo. Apakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndi chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
Mwet tol el fah eis kutu srah ke sheep fusr soko ah, ac sang mosrwela acn fisrasrsrasr ke lac srac layot, fin kuf lulap lac po layot, ac fin kufinne lulap ke lac ne layot lun mwet se su ac fah akkalemyeyuk mu el nasnasla.
15 Wansembe atengeko mafuta pangʼono, nʼkuwathira mʼdzanja lake lamanzere,
Ac mwet tol el fah eis kutu oil in olive ac okoaung nu in paol lasa,
16 aviyike chala chake cha ku dzanja lamanja mʼmafuta amene ali mʼdzanja lamanzerewo, ndi kuwaza mafutawo ndi chala chakecho kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
isongya soko kufinpaol layot nu loac, ac usrokya kutu srah inge pacl itkosr ye mutun LEUM GOD.
17 Wansembe apake mafuta otsala mʼdzanja lake pa khutu lakumanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Awapakenso pa chala chake chachikulu cha ku dzanja lamanja ndiponso pa chala chake chachikulu cha ku phazi lakumanja, pamalo pamene anali atapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula paja.
El fah eis kutu oil ma oan inpaol uh ac kutu srahn sheep fusr soko ah, ac mosrwela acn fisrasrsrasr ke lac srac layot, kuflap ke lac po layot, ac kuflap ke lac ne layot lun mwet se su ac fah akkalemyeyuk mu el nasnasla.
18 Mafuta onse otsala mʼdzanja la wansembe awathire pamutu pa munthu woti ayeretsedwe uja, ndipo potero adzachita mwambo womupepesera pamaso pa Yehova.
Na el fah sang oil ma lula inpaol uh nu fin sifen mwet sac. Ke el oru ouinge uh, el orala ouiya lun aknasnas.
19 “Kenaka wansembe apereke nsembe yopepesera machimo kuti achite mwambo womupepesera munthu woti ayeretsedwe khate lake uja. Atatha kuchita zimenezi, wansembe aphe nyama ya nsembe yopsereza
Na mwet tol el fah kisakin mwe kisa ke ma koluk, ac oru ouiya nu ke aknasnas. Toko el fah uniya sheep fusr soko nu ke kisa firir,
20 ndi kuyipereka pa guwa, pamodzi ndi nsembe yachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera munthu wodzayeretsedwayo, ndipo adzakhala woyera.
ac kisakin wi mwe kisa wheat fin loang uh. In lumah se inge mwet tol el fah oru ouiya lun aknasnas, na mwet sac fah nasnasla.
21 “Ngati munthu woti ayeretsedweyo ndi wosauka ndipo sangathe kupeza zinthu zimenezi, apereke mwana wankhosa wamwamuna monga nsembe yopepesera kupalamula ndipo ayiweyule pochita mwambo womupepesera. Aperekenso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala osakaniza ndi mafuta kuti ikhale nsembe yachakudya, pamodzi ndi mafuta wokwanira limodzi mwa magawo atatu a lita.
Mwet sac fin sukasrup ac tia ku in akfalye ma inge, el fah use sokofanna sheep fusr mukul nu ke aknasnas lal, tuh in mwe kisa ke ma koluk lukma lal, sie mwe kite sriyukla nu sin LEUM GOD. El fah use paun luo na ke flao ma karyak ke oil in olive nu ke mwe kisa wheat, ac sie cup ke oil in olive.
22 Aperekenso njiwa ziwiri kapena mawunda awiri zomwe iye angathe kuzipeza. Imodzi ikhale nsembe yopepesera machimo, ndi inayo ikhale ya nsembe yopsereza.
El fah oayapa use luo wule ku luo wuleoa, sie nu ke mwe kisa ke ma koluk, ac sie nu ke mwe kisa firir.
23 “Pa tsiku lachisanu ndi chitatu zonsezo abwere nazo kwa wansembe, pa khomo pa tenti ya msonkhano, pamaso pa Yehova kuti munthuyo ayeretsedwe.
Ke len se akoalkosr ke len in aknasnas lal, el fah use ma inge nu yurin mwet tol, nu ke acn in utyak nu ke Lohm Nuknuk Mutal.
24 Wansembe atenge mwana wankhosa wopereka nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta aja, ndipo aziweyule kuti zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
Mwet tol el fah eis sheep fusr soko ah, ac oil in olive uh, ac sang tuh in sie mwe kite srisrila nu sin LEUM GOD.
25 Wansembe aphe nkhosa yopereka nsembe yopepesera kupalamula ndipo atenge magazi ake ndi kuwapaka pa msonga ya khutu lakumanja la munthu amene ayeretsedweyo. Awapakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndiponso pa chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
El fah uniya sheep fusr soko ah, eis kutu srah kac uh, ac sang mosrwela acn fisrasrsrasr ke lac srac layot, fin kufinpo lulap ke lac po layot, ac fin kufinne lulap ke lac ne layot ke mwet sac.
26 Kenaka wansembe athire mafuta mʼdzanja lake lamanzere,
Mwet tol el fah ukuiya kutu oil uh nu inpaol layen lasa,
27 ndipo ndi chala chake cha ku dzanja lamanja awaze mafutawo kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
ac sang soko kufinpo ke lac paol layot, osrokang kutu oil uh pacl itkosr ye mutun LEUM GOD.
28 Apakenso mafuta omwewo amene ali mʼdzanja lake lamanja pa msonga ya khutu la kudzanja lamanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Apakenso pa chala chachikulu cha phazi lakumanja, pamalo pamene anapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula.
El fah sang kutu oil nu fin acn na ma el sang srah uh nu kac: fin acn fisrasrsrasr layen layot ke insren mwet sac, fin kuflap ke la paol layot, ac fin kuflap ke la nial layot.
29 Mafuta onse otsala amene ali mʼdzanja la wansembe awapake pamutu pa munthu amene ayeretsedweyo kuti amuchitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.
Oil ma lula inpaol uh el fah ukuiya fin sifen mwet sac, ac ke el oru ouinge el orala ouiya nu ke aknasnas.
30 Ndipo munthuyo apereke njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri, molingana ndi mmene anapezeramo,
Na el fah sang sie sin wule uh ku wuleoa uh
31 imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza, pamodzi ndi chopereka chachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera machimo a munthu woti ayeretsedwe.
tuh in mwe kisa ke ma koluk, ac ma se saya uh nu ke mwe kisa firir, wi mwe kisa wheat. In lumah se inge mwet tol el orala ouiya nu ke aknasnas.
32 “Amenewa ndi malamulo a munthu wakhate amene alibe zinthu zoti apereke pamene akuyeretsedwa.
Pa inge ma sap nu ke sie mwet su oasr mas na sensenkinyuk ke mano, su tia ku in srukak mwe kisa ma ac fal nu ke aknasnas lal.
33 “Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
LEUM GOD El kaskas nu sel Moses ac Aaron, ac fahk:
34 Mukakalowa mʼdziko la Kanaani limene ndikukupatsani kuti likhale lanu, ndipo Ine ndikakabweretsa ndere zoyanga mʼnyumba mʼdziko limenelo,
“Ke kowos fin mau tuku nu in facl Canaan, su nga ac fah sot tuh in ma lowos, ac nga filiya tuhnyohu nu ke sie lohm in acn suwos uh,
35 mwini wake nyumbayo adzapite kwa wansembe ndi kukamuwuza kuti, ‘Ndaona chinthu chooneka ngati ndere mʼnyumba mwanga.’
na mwet se la lohm sac enenu in tuku nu yurin mwet tol ac fahk nu sel ouinge: ‘Nga liye tuh luman oasr tuhnyohu ke lohm sik uh.’
36 Tsono wansembe alamule kuti anthu atulutse zinthu zonse mʼnyumbamo iye asanalowemo ndi kukaonetsetsa ndereyo kuti mʼnyumbamo musapezeke chinthu choti achitchule chodetsedwa. Izi zitachitika, wansembe alowe mʼnyumbamo ndi kukaonamo.
Na mwet tol sac fah sap tuh ma nukewa in lohm sac in titila nu sayen lohm sac meet liki el som ac tuni tuhnyohu kac uh. Fin tia ouinge, na ma nukewa in lohm sac fah fwackyak mu tia nasnas. Na tok mwet tol el fah som nu ke lohm sac,
37 Iye aonetsetse nderezo. Tsono akapeza kuti nderezo zili mʼkhoma la nyumba, ndipo ngati zili ndi mawanga obiriwira kapena ofiirira, komanso zikuoneka kuti zalowerera mpaka mʼkati mwa khoma,
ac tuni tuhnyohu kac. Fin oasr acn ma luman tuhn folfolsra ku srusrsrusra kac, ma luman ac kulweya sinka in lohm sac,
38 wansembe atuluke mʼnyumbamo ndi kupita pa khomo, ndipo ayitseke nyumbayo masiku asanu ndi awiri.
na el fah illa liki lohm sac ac kaliya ke len itkosr.
39 Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri wansembe abwerenso kudzayangʼana mʼnyumbamo. Ngati ndere yafalikira mʼmakoma a nyumbayo,
Ke len se akitkosr el fah folokla ac sifilpa tuni lah fuka. Tuhnyohu sac fin yokelik,
40 wansembe alamule kuti anthu agumule miyala imene muli nderezo ndipo akayitaye kudzala la kunja kwa mzinda.
na el fah sap eot ma tuhnyohula inge in itukla ac sisila nu in sie acn tia nasnas likin siti sac.
41 Wansembe awuze anthu kuti apale makoma onse a mʼkati mwa nyumbayo, ndipo zopalidwazo akazitaye ku malo odetsedwa a kunja kwa mudzi.
Toko, el fah sap sinka loac ke lohm sac nufon in koekoela, ac kutkut kac nukewa in sisila nu in sie acn tia nasnas likin siti sac.
42 Tsono anthuwo atenge miyala ina ndi kuyilowetsa mʼmalo mwa miyala imene anagumula ija ndipo atenge dothi latsopano ndi kumata nyumbayo.
Na kutu pac eot sasu ac fah orekmakinyuk in aolla eot ma itukla, ac akmusra sasu fah sang afinya acn ma koekoela ke sinka ah.
43 “Ngati ndere iwonekanso mʼnyumbamo atagumula kale miyala ndiponso atayipala kale ndi kuyimatanso,
“Fin tuhnyohu sac sifilpa folokyak in lohm sac tukun ayaolla eot ma kolukla ac koekoela sinka kac ac akmusralla,
44 wansembe apite kukayionetsetsenso ndipo ngati nderezo zafalikira mʼnyumbamo, ndiye kuti ndere zimenezo ndi zoopsa. Nyumba imeneyo ndi yodetsedwa.
na mwet tol el enenu in sifilpa som ac liye. Fin tuhnyohu sac tuh yokelik, na lohm sac tia nasnas.
45 Agwetse nyumbayo, ndipo miyala yake, matabwa pamodzi ndi dothi lake lonse, zonse akazitaye kudzala lodetsedwa, kunja kwa mzinda.
Enenu na in kunanui lohm sac, ac eot kac, sak kac, ac fasr kac nukewa fah utukla nu likin siti uh, nu in sie acn ma tia nasnas.
46 “Aliyense amene alowa mʼnyumbamo itatsekedwa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
Kutena mwet su utyak nu in lohm sac ke pacl se kauli uh, ac fah lumweyuk el tia nasnas nwe ke ekela.
47 Munthu amene wagona mʼnyumbamo kapena kudyeramo ayenera kuchapa zovala zake.
Kutena mwet su ona ku mongo in lohm sac enenu na in ohlla nuknuk lal.
48 “Koma ngati pambuyo pa kuyimata, wansembe abwera kudzaonetsetsa mʼnyumbamo napeza kuti ndereyo sinafalikire, iye alengeze kuti nyumbayo ndi yoyeretsedwa, chifukwa ndereyo yatha.
“Ke pacl se ma mwet tol el tuku in liye uh, tuh na tuhnyohu sac tiana sifil folokyak tukun lohm sac akwoyeyukla, na el fah fahkak lah lohm sac nasnas, mweyen tuhnyohu sac wanginla na pwaye.
49 Kuti nyumbayo iyeretsedwe, mwini wake atenge mbalame ziwiri, kanthambi kamkungudza, kansalu kofiirira ndi kachitsamba ka hisope.
In aknasnasye lohm sac, el fah us luo won, sie ipin sak cedar, sie polo ah srusra, ac sie lesak srisrik ke hyssop.
50 Wansembe aphe mbalame imodzi pamwamba pa madzi abwino mu mʼphika wa dothi.
El fah uniya sie sin won luo ah fin sie pol eot ma oasr kof nasnas oan loac.
51 Kenaka atenge kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope, kansalu kofiirira pamodzi ndi mbalame yamoyo ija, zonsezi aziviyike mʼmagazi a mbalame yophedwa ija, ndiponso mʼmadzi abwino aja, ndipo awaze nyumbayo kasanu ndi kawiri
Na el fah eis sak cedar sac, lesak hyssop sac, polo ah srusra sac, ac won se ma srakna moul uh, ac isongya ma inge nukewa in srahn won se ma anwuki ac oan in kof nasnas sac, na sang aksroksrokye lohm sac pacl itkosr.
52 Akatero ndiye kuti wayeretsa nyumbayo ndi magazi a mbalame, madzi abwino, mbalame yamoyo, kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope ndi kansalu kofiirira.
Ke el oru ma inge uh el ac aknasnasyela lohm sac ke srahn won sac, kof nasnas sac, won moul sac, sak cedar sac, lesak hyssop sac, ac polo ah srusra sac.
53 Kenaka ayiwulutsire mbalame yamoyo ija kuthengo, kunja kwa mzinda. Pamenepo ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera nyumbayo, ndipo idzakhala yoyeretsedwa.”
Na el fah fuhlela won se ma moul ah in sohkla. Ke el oru ouinge, na el orala ouiya lun aknasnas nu ke lohm sac, na lohm sac fah nasnasla.
54 Amenewa ndiwo malamulo a nthenda ya khate, bala lonyerenyetsa,
“Pa inge ma sap nu ke mas ma sensenkinyuk nu ke mano:
55 nguwi za pa zovala, ndere za mʼnyumba,
ku nu ke tuhnyohu ma oan ke nuknuk ku ke lohm,
56 khate la chithupsa, khate la mʼbuko ndi khate la banga
ac nu ke faf, ku acn ma aryurla ke mano, ku ke tuhn koluk ke mano.
57 kuti mudziwe ngati chinthucho ndi choyeretsedwa kapena chodetsedwa. Amenewa ndiwo malamulo a nthenda zonse za khate.
Ma sap inge pa fahkak inmasrlon ma su tia nasnas ac ma su nasnas.”