< Levitiko 14 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
L'Éternel parla à Moïse, en disant:
2 “Malamulo a munthu wakhate pa tsiku la kuyeretsedwa kwake ndi awa: Abwere naye kwa wansembe.
Voici la loi touchant le lépreux, pour le jour de sa purification: on l'amènera au sacrificateur;
3 Wansembe atuluke kunja kwa msasa ndipo amuonetsetse wodwalayo. Ngati munthu wakhateyo wachira,
Le sacrificateur sortira du camp et l'examinera. Si la plaie de la lèpre du lépreux est guérie,
4 wansembe alamule anthu kuti amutengere wodwala woti ayeretsedweyo, mbalame zamoyo ziwiri zomwe Ayuda amaloledwa kudya, nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope.
Le sacrificateur ordonnera de prendre pour celui qui doit être purifié, deux oiseaux vivants et purs, du bois de cèdre, du cramoisi et de l'hysope.
5 Wansembe alamule anthuwo kuti mbalame imodzi ayiphere mu mʼphika wa dothi pamwamba pa madzi abwino.
Et le sacrificateur commandera qu'on égorge l'un des oiseaux sur un vase de terre, sur de l'eau vive.
6 Kenaka wansembe atenge mbalame yamoyo ija ndi kuyinyika pamodzi ndi nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope kaja mʼmagazi ambalame imene anayiphera pamwamba pa madzi abwino.
Quant à l'oiseau vivant, il le prendra, avec le bois de cèdre, le cramoisi et l'hysope, et il les trempera, avec l'oiseau vivant, dans le sang de l'oiseau égorgé sur l'eau vive;
7 Wansembe awaze magazi kasanu ndi kawiri pa munthu woti amuyeretse khateyo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa. Kenaka wansembe awulutsire ku thengo mbalame yamoyoyo.
Il en fera aspersion sept fois sur celui qui se purifie de la lèpre, il le déclarera pur, et il lâchera dans les champs l'oiseau vivant.
8 “Munthu amene wayeretsedwa uja achape zovala zake, amete tsitsi lake lonse, ndipo asambe mʼmadzi. Akatero adzakhala woyeretsedwa. Atatha zimenezi munthuyo apite ku msasa wake koma akhale kunja kwa msasawo kwa masiku asanu ndi awiri.
Et celui qui se purifie lavera ses vêtements, rasera tout son poil, se lavera dans l'eau et il sera pur. Ensuite il entrera dans le camp, mais il demeurera hors de sa tente pendant sept jours.
9 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri amete tsitsi lake lonse: amete kumutu, ndevu zake, nsidze zake pamodzi ndi tsitsi lina lonse. Kenaka achape zovala zake ndi kusamba mʼmadzi, ndipo adzakhala woyeretsedwa.
Et au septième jour, il rasera tout son poil, sa tête, sa barbe, ses sourcils, il rasera tout son poil. Il lavera ses vêtements et baignera son corps dans l'eau, et il sera pur.
10 “Pa tsiku lachisanu ndi chitatu munthuyo atenge ana ankhosa aamuna awiri ndi mwana wankhosa wamkazi wa chaka chimodzi. Zonsezi zikhale zopanda chilema. Atengenso chopereka chachakudya cha ufa wosalala wa makilogalamu atatu wosakaniza ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita.
Le huitième jour, il prendra deux agneaux sans défaut, et une brebis de l'année sans défaut, trois dixièmes d'épha de fine farine en offrande, arrosée d'huile, et un log d'huile;
11 Wansembe amene ati ayeretse munthu wodwalayo amuyimitse munthuyo ali ndi zopereka zake zonse pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
Et le sacrificateur qui fait la purification, présentera l'homme qui se purifie et ces choses devant l'Éternel, à l'entrée du tabernacle d'assignation.
12 “Ndipo wansembe atenge mwana wankhosa wamwamuna mmodzi ndi kumupereka kuti akhale nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita. Wansembe aziweyule zonsezi pamaso pa Yehova kuti zikhale chopereka choweyula.
Ensuite le sacrificateur prendra l'un des agneaux, et l'offrira en sacrifice pour le délit, avec le log d'huile, et il les agitera en oblation devant l'Éternel.
13 Mwana wankhosayo amuphere pa malo amene amaphera nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yopsereza, kutanthauza malo opatulika. Monga zimakhalira ndi chopereka chopepesera machimo, chopereka ichi ndi chake cha wansembe ndipo ndi chopereka choyera kopambana.
Puis il égorgera l'agneau, au lieu où l'on égorge le sacrifice pour le péché et l'holocauste, dans le lieu saint; car le sacrifice pour le délit appartient au sacrificateur, comme le sacrifice pour le péché; c'est une chose très sainte.
14 Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera kupalamula ndi kuwapaka pa msonga pa khutu lakumanja la munthu woti ayeretsedweyo. Apakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndi chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
Et le sacrificateur prendra du sang du sacrifice pour le délit; il en mettra sur le bout de l'oreille droite de celui qui se purifie, sur le pouce de sa main droite, et sur le gros orteil de son pied droit.
15 Wansembe atengeko mafuta pangʼono, nʼkuwathira mʼdzanja lake lamanzere,
Le sacrificateur prendra du log d'huile et en versera dans sa main gauche;
16 aviyike chala chake cha ku dzanja lamanja mʼmafuta amene ali mʼdzanja lamanzerewo, ndi kuwaza mafutawo ndi chala chakecho kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
Ensuite le sacrificateur trempera le doigt de sa main droite dans l'huile qui sera dans sa main gauche, et fera aspersion de l'huile avec son doigt sept fois devant l'Éternel.
17 Wansembe apake mafuta otsala mʼdzanja lake pa khutu lakumanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Awapakenso pa chala chake chachikulu cha ku dzanja lamanja ndiponso pa chala chake chachikulu cha ku phazi lakumanja, pamalo pamene anali atapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula paja.
Et du reste de l'huile qui sera dans sa main, le sacrificateur en mettra sur le bout de l'oreille droite de celui qui se purifie, sur le pouce de sa main droite, et sur le gros orteil de son pied droit, par-dessus le sang du sacrifice pour le délit.
18 Mafuta onse otsala mʼdzanja la wansembe awathire pamutu pa munthu woti ayeretsedwe uja, ndipo potero adzachita mwambo womupepesera pamaso pa Yehova.
Ce qui restera de l'huile qui sera dans sa main, le sacrificateur le mettra sur la tête de celui qui se purifie; et le sacrificateur fera pour lui l'expiation devant l'Éternel.
19 “Kenaka wansembe apereke nsembe yopepesera machimo kuti achite mwambo womupepesera munthu woti ayeretsedwe khate lake uja. Atatha kuchita zimenezi, wansembe aphe nyama ya nsembe yopsereza
Puis le sacrificateur offrira le sacrifice pour le péché, et fera l'expiation pour celui qui se purifie de sa souillure; ensuite il égorgera l'holocauste.
20 ndi kuyipereka pa guwa, pamodzi ndi nsembe yachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera munthu wodzayeretsedwayo, ndipo adzakhala woyera.
Le sacrificateur offrira l'holocauste et l'offrande sur l'autel; et il fera l'expiation pour cet homme, et il sera pur.
21 “Ngati munthu woti ayeretsedweyo ndi wosauka ndipo sangathe kupeza zinthu zimenezi, apereke mwana wankhosa wamwamuna monga nsembe yopepesera kupalamula ndipo ayiweyule pochita mwambo womupepesera. Aperekenso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala osakaniza ndi mafuta kuti ikhale nsembe yachakudya, pamodzi ndi mafuta wokwanira limodzi mwa magawo atatu a lita.
Mais s'il est pauvre et que ses moyens n'y suffisent pas, il prendra un agneau comme sacrifice pour le délit en offrande agitée pour faire l'expiation pour lui, et un dixième de fine farine arrosée d'huile pour l'offrande, et un log d'huile,
22 Aperekenso njiwa ziwiri kapena mawunda awiri zomwe iye angathe kuzipeza. Imodzi ikhale nsembe yopepesera machimo, ndi inayo ikhale ya nsembe yopsereza.
Et deux tourterelles ou deux pigeonneaux, selon ses moyens, l'un pour le sacrifice pour le péché, l'autre pour l'holocauste.
23 “Pa tsiku lachisanu ndi chitatu zonsezo abwere nazo kwa wansembe, pa khomo pa tenti ya msonkhano, pamaso pa Yehova kuti munthuyo ayeretsedwe.
Il apportera ces choses le huitième jour au sacrificateur, pour sa purification, à l'entrée du tabernacle d'assignation, devant l'Éternel.
24 Wansembe atenge mwana wankhosa wopereka nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta aja, ndipo aziweyule kuti zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
Le sacrificateur prendra l'agneau pour le sacrifice pour le délit, et le log d'huile; et le sacrificateur les agitera en offrande devant l'Éternel.
25 Wansembe aphe nkhosa yopereka nsembe yopepesera kupalamula ndipo atenge magazi ake ndi kuwapaka pa msonga ya khutu lakumanja la munthu amene ayeretsedweyo. Awapakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndiponso pa chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
Puis il égorgera l'agneau du sacrifice pour le délit. Le sacrificateur prendra du sang du sacrifice pour le délit et en mettra sur le bout de l'oreille droite de celui qui se purifie, sur le pouce de sa main droite, et sur le gros orteil de son pied droit.
26 Kenaka wansembe athire mafuta mʼdzanja lake lamanzere,
Ensuite le sacrificateur se versera de l'huile dans la paume de sa main gauche.
27 ndipo ndi chala chake cha ku dzanja lamanja awaze mafutawo kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
Et de l'huile qui sera dans sa main gauche, le sacrificateur fera aspersion avec le doigt de sa main droite, sept fois devant l'Éternel.
28 Apakenso mafuta omwewo amene ali mʼdzanja lake lamanja pa msonga ya khutu la kudzanja lamanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Apakenso pa chala chachikulu cha phazi lakumanja, pamalo pamene anapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula.
Et le sacrificateur mettra de l'huile qui sera dans sa main sur le bout de l'oreille droite de celui qui se purifie, sur le pouce de sa main droite, et sur le gros orteil de son pied droit, à l'endroit où il a mis du sang du sacrifice pour le délit.
29 Mafuta onse otsala amene ali mʼdzanja la wansembe awapake pamutu pa munthu amene ayeretsedweyo kuti amuchitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.
Ce qui restera de l'huile qui sera dans sa main, le sacrificateur le mettra sur la tête de celui qui se purifie, pour faire l'expiation pour lui, devant l'Éternel.
30 Ndipo munthuyo apereke njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri, molingana ndi mmene anapezeramo,
Puis, il sacrifiera l'une des tourterelles ou l'un des pigeonneaux, suivant ce qu'il pourra présenter,
31 imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza, pamodzi ndi chopereka chachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera machimo a munthu woti ayeretsedwe.
Selon ses moyens, l'un en sacrifice pour le péché, l'autre en holocauste, avec l'offrande. Et le sacrificateur fera l'expiation devant l'Éternel pour celui qui se purifie.
32 “Amenewa ndi malamulo a munthu wakhate amene alibe zinthu zoti apereke pamene akuyeretsedwa.
Telle est la loi concernant celui qui a une plaie de lèpre, et dont les ressources sont insuffisantes quant à sa purification.
33 “Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
L'Éternel parla encore à Moïse et à Aaron, en disant:
34 Mukakalowa mʼdziko la Kanaani limene ndikukupatsani kuti likhale lanu, ndipo Ine ndikakabweretsa ndere zoyanga mʼnyumba mʼdziko limenelo,
Quand vous serez entrés au pays de Canaan, dont je vous donne la possession, si je mets une plaie de lèpre dans une maison du pays que vous posséderez,
35 mwini wake nyumbayo adzapite kwa wansembe ndi kukamuwuza kuti, ‘Ndaona chinthu chooneka ngati ndere mʼnyumba mwanga.’
Celui à qui la maison appartient viendra et le déclarera au sacrificateur, en disant: J'aperçois comme une plaie dans la maison.
36 Tsono wansembe alamule kuti anthu atulutse zinthu zonse mʼnyumbamo iye asanalowemo ndi kukaonetsetsa ndereyo kuti mʼnyumbamo musapezeke chinthu choti achitchule chodetsedwa. Izi zitachitika, wansembe alowe mʼnyumbamo ndi kukaonamo.
Alors le sacrificateur commandera qu'on vide la maison, avant qu'il y entre pour voir la plaie, afin que tout ce qui est dans la maison ne soit pas souillé; après cela, le sacrificateur entrera pour voir la maison.
37 Iye aonetsetse nderezo. Tsono akapeza kuti nderezo zili mʼkhoma la nyumba, ndipo ngati zili ndi mawanga obiriwira kapena ofiirira, komanso zikuoneka kuti zalowerera mpaka mʼkati mwa khoma,
Et il examinera la plaie; et si la plaie qui est aux parois de la maison a des cavités verdâtres ou rougeâtres, paraissant plus enfoncées que la paroi,
38 wansembe atuluke mʼnyumbamo ndi kupita pa khomo, ndipo ayitseke nyumbayo masiku asanu ndi awiri.
Le sacrificateur sortira de la maison; et à la porte, il fermera la maison pendant sept jours.
39 Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri wansembe abwerenso kudzayangʼana mʼnyumbamo. Ngati ndere yafalikira mʼmakoma a nyumbayo,
Le septième jour, le sacrificateur y retournera; et s'il voit que la plaie s'est étendue sur les parois de la maison,
40 wansembe alamule kuti anthu agumule miyala imene muli nderezo ndipo akayitaye kudzala la kunja kwa mzinda.
Le sacrificateur commandera d'arracher les pierres infectées de la plaie, et de les jeter hors de la ville, dans un lieu souillé.
41 Wansembe awuze anthu kuti apale makoma onse a mʼkati mwa nyumbayo, ndipo zopalidwazo akazitaye ku malo odetsedwa a kunja kwa mudzi.
Il fera racler la maison à l'intérieur, tout autour, et l'on jettera la poussière qu'on aura raclée, hors de la ville, dans un lieu souillé.
42 Tsono anthuwo atenge miyala ina ndi kuyilowetsa mʼmalo mwa miyala imene anagumula ija ndipo atenge dothi latsopano ndi kumata nyumbayo.
On prendra d'autres pierres et on les mettra à la place des premières, et l'on prendra d'autre enduit pour recrépir la maison.
43 “Ngati ndere iwonekanso mʼnyumbamo atagumula kale miyala ndiponso atayipala kale ndi kuyimatanso,
Mais si la plaie revient et fait éruption dans la maison après qu'on aura arraché les pierres, après qu'on aura raclé la maison et après qu'on l'aura recrépie,
44 wansembe apite kukayionetsetsenso ndipo ngati nderezo zafalikira mʼnyumbamo, ndiye kuti ndere zimenezo ndi zoopsa. Nyumba imeneyo ndi yodetsedwa.
Le sacrificateur reviendra. S'il voit que la plaie s'est étendue dans la maison, c'est une lèpre rongeante dans la maison; elle est souillée.
45 Agwetse nyumbayo, ndipo miyala yake, matabwa pamodzi ndi dothi lake lonse, zonse akazitaye kudzala lodetsedwa, kunja kwa mzinda.
On abattra donc la maison, ses pierres, ses bois, et tous les enduits de la maison, et on transportera le tout hors de la ville, dans un lieu souillé.
46 “Aliyense amene alowa mʼnyumbamo itatsekedwa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
Celui qui sera entré dans la maison pendant tout le temps qu'elle était fermée sera souillé jusqu'au soir.
47 Munthu amene wagona mʼnyumbamo kapena kudyeramo ayenera kuchapa zovala zake.
Celui qui aura couché dans la maison, lavera ses vêtements. Celui qui aura mangé dans la maison, lavera ses vêtements.
48 “Koma ngati pambuyo pa kuyimata, wansembe abwera kudzaonetsetsa mʼnyumbamo napeza kuti ndereyo sinafalikire, iye alengeze kuti nyumbayo ndi yoyeretsedwa, chifukwa ndereyo yatha.
Mais si le sacrificateur vient et voit que la plaie ne s'est pas étendue dans la maison, après que la maison a été recrépie, le sacrificateur déclarera la maison pure; car la plaie est guérie.
49 Kuti nyumbayo iyeretsedwe, mwini wake atenge mbalame ziwiri, kanthambi kamkungudza, kansalu kofiirira ndi kachitsamba ka hisope.
Il prendra, pour purifier la maison, deux oiseaux, du bois de cèdre, du cramoisi et de l'hysope;
50 Wansembe aphe mbalame imodzi pamwamba pa madzi abwino mu mʼphika wa dothi.
Il égorgera l'un des oiseaux sur un vase de terre, sur de l'eau vive;
51 Kenaka atenge kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope, kansalu kofiirira pamodzi ndi mbalame yamoyo ija, zonsezi aziviyike mʼmagazi a mbalame yophedwa ija, ndiponso mʼmadzi abwino aja, ndipo awaze nyumbayo kasanu ndi kawiri
Il prendra le bois de cèdre, l'hysope, le cramoisi et l'oiseau vivant; il les trempera dans le sang de l'oiseau égorgé, et dans l'eau vive, et il en fera aspersion sur la maison, sept fois.
52 Akatero ndiye kuti wayeretsa nyumbayo ndi magazi a mbalame, madzi abwino, mbalame yamoyo, kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope ndi kansalu kofiirira.
Il purifiera ainsi la maison avec le sang de l'oiseau, avec l'eau vive, avec l'oiseau vivant, le bois de cèdre, l'hysope et le cramoisi.
53 Kenaka ayiwulutsire mbalame yamoyo ija kuthengo, kunja kwa mzinda. Pamenepo ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera nyumbayo, ndipo idzakhala yoyeretsedwa.”
Puis il lâchera l'oiseau vivant hors de la ville dans les champs; et il fera l'expiation pour la maison, et elle sera pure.
54 Amenewa ndiwo malamulo a nthenda ya khate, bala lonyerenyetsa,
Telle est la loi concernant toute plaie de lèpre et la teigne,
55 nguwi za pa zovala, ndere za mʼnyumba,
Pour la lèpre du vêtement et de la maison;
56 khate la chithupsa, khate la mʼbuko ndi khate la banga
Pour la tumeur, l'éruption et les taches;
57 kuti mudziwe ngati chinthucho ndi choyeretsedwa kapena chodetsedwa. Amenewa ndiwo malamulo a nthenda zonse za khate.
Afin d'enseigner quand il y a souillure, et quand il y a pureté. Telle est la loi concernant la lèpre.

< Levitiko 14 >