< Levitiko 13 >

1 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
И рече Господь к Моисею и Аарону, глаголя:
2 “Munthu akakhala ndi chithupsa, kapena mʼbuko, kapena chikanga pa thupi lake chimene chitha kusanduka nthenda ya khate, abwere naye munthuyo kwa Aaroni wansembe kapena kwa mmodzi mwa ana ake amene ndi ansembe.
человеку емуже аще будет на кожи плоти его струп знамения или блеск, и будет на кожи плоти его язва прокажения, да приведется ко Аарону жерцу или ко единому от сынов его жерцов:
3 Tsono wansembe ayangʼanitsitse nthendayo pa khungupo, ndipo ngati ubweya wa pamalo pamene pali nthendapo wasanduka woyera, komanso kuti nthendayo yazama mʼkati kupitirira khungu, ndiye kuti nthendayo ndi khate. Wansembe akamuonetsetsa alengeze kuti ndi wodetsedwa.
и узрит жрец язву на кожи плоти его, и влас в язве изменится в бело, и взор язвы умален от кожи плоти его, язва проказы есть: и узрит жрец, и осквернит его.
4 Ngati chikanga cha pa khungulo chikuoneka choyera, ndipo kuya kwake sikukuonekera kuti kwapitirira khungu ndi ubweya wake pamalopo sunasanduke woyera, wansembe amuyike wodwalayo padera kwa masiku asanu ndi awiri.
Аще же и блеск бел будет на кожи плотней его, и не менший будет взор его от кожи, и влас его не изменися во влас бел, и той есть темен, и отлучит жрец язву на седмь дний:
5 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso bwino wodwalayo. Ndipo ngati waona kuti nthendayo sinasinthe ndipo sinafalikire pa khungu, amuyikenso wodwalayo padera kwa masiku ena asanu ndi awiri.
и узрит жрец язву в день седмый, и се, язва пребывает пред ним, и не изменися язва на кожи, и отлучит его жрец на другия седмь дний:
6 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembeyo amuonenso bwino munthuyo, ndipo ngati nthendayo yazima ndi kusafalikira pa khungu, wansembe amutchule munthuyo kuti ndi woyera. Umenewo unali mʼbuko chabe. Choncho munthuyo achape zovala zake ndipo adzakhala woyera.
и узрит его жрец в седмый день вторицею, и се, язва потемне, и не изменися язва на кожи, и очистит его жрец: знамение бо есть: и измыв ризы своя, чист будет.
7 Koma ngati mʼbukowo ufalikira pakhungu atakadzionetsa kale kwa wansembe ndipo wansembeyo nʼkulengeza kuti munthuyo ndi woyeretsedwa, ndiye kuti apitenso kukadzionetsa kwa wansembeyo.
Аще же изменяющееся изменится знамение на кожи, повнегда видети его жерцу еже очистити его, и явится второе жерцу: и узрит его жрец, и се, изменися знамение в кожи,
8 Wansembe amuonetsetsenso munthuyo, ndipo ngati mʼbukowo wafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa ndi kuti nthendayo ndi khate.
и да осквернит его жрец: проказа бо есть.
9 “Ngati munthu aliyense ali ndi nthenda ya pakhungu yoyipitsa thupi, wodwalayo abwere naye kwa wansembe.
И язва прокажения аще будет на человеце, и приидет к жерцу:
10 Wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati ali ndi chithupsa chamaonekedwe woyera pa khungupo chimene chasandutsa ubweya wa pamalopo kukhala woyera, ndipo ngati pali zilonda pa chotupacho,
и узрит жрец, и се, струп бел на кожи, и сей изменил влас бел, и от здравыя плоти живыя в струпе:
11 limenelo ndi khate lachikhalire la pa khungu, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Asamutsekere munthu woteroyo pakuti ndi wodetsedwa kale.
проказа ветха есть на кожи плоти его, и осквернит его жрец и отлучит его, яко нечист есть.
12 “Ndipo ngati, mʼkuona kwa wansembe, khate lija lafalikira pa khungu lonse moti lamugwira thupi lonse kuyambira kumutu mpaka kumapazi,
Аще же процветая процветет проказа на кожи, и покрыет прокажение всю кожу язвою, от главы да ногу его, по всему взору жерцову:
13 wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati khatero lagwira thupi lake lonse, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Popeza kuti thupi lonse lasanduka loyera, munthuyo ndi woyeretsedwa.
и узрит жрец, и се, покрыло прокажение всю кожу плоти его, да очистит жрец язву: яко вся изменися в бело, чист есть.
14 Koma pa tsiku limene zilonda zidzaoneka pa iye, munthuyo adzakhala wodetsedwa.
И в оньже день аще явится на нем плоть жива, осквернится:
15 Wansembe aonetsetse zilondazo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zilondazo ndi zodetsedwa ndipo ili ndi khate.
и узрит жрец плоть здраву, и осквернит его плоть здрава, яко нечиста есть, прокажение есть.
16 Koma zilondazo zikasinthika ndi kusanduka zoyera, munthuyo ayenera kupita kwa wansembe.
Аще же составится плоть здрава, и изменится в бело, и приидет к жерцу:
17 Wansembe amuonetsetse ndipo ngati zilondazo zasanduka zoyera, wansembe amutchule wodwalayo kuti ndi woyera ndipo adzakhala woyera ndithu.
и узрит жрец, и се, изменися язва в бело, и очистит жрец язву, чист есть.
18 “Ngati pa khungu la munthu wodwalayo pali chithupsa chimene chinapola kale,
И тело аще будет на кожи его болячка гнойна, и исцелеет,
19 ndipo pamalo pamene panali chithupsacho pakatuluka chotupa choyera kapena banga loyera mofiirira, munthuyo ayenera kukadzionetsa kwa wansembe.
и будет на месте болячки струп бел, или блеск белеющься или рдящься, и явится жерцу:
20 Wansembe aonetsetse bwino ndipo ngati chikuoneka kuti chazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka woyera, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Imeneyo ndi nthenda ya khate imene yatuluka mʼchithupsacho.
и узрит жрец, и се, взор нижае кожи, и влас его изменися в бело, и осквернит его жрец, яко блеск прокажения есть, на болячке процвете.
21 Koma ngati wansembe waonetsetsa napeza kuti palibe ubweya woyera ndipo chithupsacho sichinazame, koma chazimirira, wansembeyo amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
Аще же увидит жрец, и се, несть в нем влас бел, и не нижае есть от кожи плотския, и сей есть темен, и отлучит его жрец на седмь дний.
22 Ngati nthendayo ikufalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limeneli ndi khate.
Аще ли разсыпанием разсыплется по кожи, и осквернит его жрец, блеск прокажения есть, на болячке процвете.
23 Koma bangalo likakhala malo amodzi, wosafalikira, chimenecho ndi chipsera cha chithupsacho, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera.
Аще ли на месте своем пребывает блеск и не разсыпается, струп болячки есть, и очистит его жрец.
24 “Munthu akakhala ndi bala lamoto pa khungu lake, ndipo chilonda cha balalo chikasanduka banga loyera mofiirira kapena loyera,
И плоть аще будет на кожи его жжение огнено, и будет на кожи его исцелевшее от жжения блещащееся бело или червлено или пробелующееся:
25 wansembe aonetsetse bangalo, ndipo ngati ubweya wa pa bangapo usanduka woyera, ndipo balalo lioneka kuti ndi lozama, limenelo ndi khate lomwe latuluka pa balalo. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate la pa khungu.
и узрит его жрец, и се, пременися влас бел в блещащийся, и взор ему нижае от кожи, прокажение есть, во жжении процвете, и осквернит его жрец, язва прокажения есть.
26 Koma ngati wansembe waonetsetsa balalo ndipo palibe ubweya woyera, ndipo ngati balalo silinazame ndi kuti lazirala, wansembe amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
Аще же увидит его жрец, и се, несть на блещащемся влас бел, и не нижае есть от кожи, само же темно, и отлучит его жрец на седмь дний:
27 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso wodwalayo, ndipo ngati bangalo lafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate.
и узрит его жрец в день седмый, и аще разсыпанием разсыплется по кожи, и осквернит его жрец: язва прокажения есть, бо гной процвете.
28 Koma ngati bangalo likhala pa malo amodzi wosafalikira pa khungu, ndipo lazimirira, limenelo ndi thuza la bala lamoto, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Chimenecho ndi chipsera chamoto.
Аще же на месте пребудет блещание и не разсыплется по кожи, сие же темно есть, струп сожжения есть, да очистит его жрец: образ бо сожжения есть.
29 “Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi nthenda kumutu kapena ku chibwano,
Мужу же или жене, аще будет на них язва прокажения на главе или на браде,
30 wansembe aonetsetse balalo ndipo likaoneka kuti lazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka wachikasu ndi wonyololoka, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zimenezo ndi mfundu zonyerenyetsa, khate lakumutu kapena ku chibwano.
и узрит жрец язву, и се, обличие ея глубочае кожи, в нейже влас желтуяся тонок, и осквернит его жрец: вред есть, прокажение главы или прокажение брады есть.
31 Koma wansembe akaonetsetsa mfundu zonyerenyetsazo, ndipo zikaoneka kuti sizinazame ndi kuti palibe ubweya wakuda, wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku asanu ndi awiri.
И аще увидит жрец язву вреда, и се, не будет обличие нижае кожи, и влас желтуяся не будет в нем, да отлучит жрец язву вреда на седмь дний:
32 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo, ndipo ngati sizinafalikire ndipo palibe ubweya wachikasu pamalopo ndiponso sizinazame,
и узрит жрец язву в день седмый, и се, не разсыпася вред, и влас желтуяся несть в нем, и обличие вреда несть нижае кожи:
33 wodwalayo ametedwe, koma pamene pali mfunduyo pasametedwe. Wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
и острижет кожу, вред же да не острижется, и отлучит жрец вред на седмь дний второе:
34 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo ndipo ngati sizinafalikire pa khungu ndi kuti sizinazame, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Tsono achape zovala zake, ndipo adzakhala woyera.
и узрит жрец вред в день седмый, и се, не разсыпася вред по кожи по острижении его, и обличие вреда несть нижае кожи, и очистит его жрец, и измыв ризы, чист будет.
35 Koma mfundu zonyerenyetsazo zikafalikira pa khungu, wansembe atalengeza kuti ndi woyera,
Аще же разсыпанием разсыплется вред по кожи по очищении его:
36 wansembe amuonetsetsenso wodwalayo ndipo ngati mfunduzo zafalikira pa khungu, iye asalabadirenso zoyangʼana ngati ubweya uli wachikasu. Munthuyo ndi wodetsedwa.
и узрит его жрец, и се, не разсыпася вред по кожи, да не присетит жрец о власе желтеющемся, яко нечист есть.
37 Koma ngati wansembe waonetsetsa kuti mfunduzo sizinasinthe ndipo ubweya wakuda wamera pa mfundupo, ndiye kuti wodwalayo wachira. Tsono wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa.
Аще же пред ним будет на месте вред, и влас черн явится в нем, исцеле вред, чист есть, и очистит его жрец.
38 “Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi mawanga woyera pa khungu,
Мужу же или жене, аще будут на кожи плоти его блещания блещащая белеющаяся:
39 wansembe aonetsetse mawangawo, ndipo ngati ali otuwa, ndiye kuti ndi mibuko chabe yotuluka pa khungu. Munthuyo ndi woyera.
и увидит жрец, и се, на кожи плоти его блещания и блещащая белеющаяся, лишай есть, процвете на кожи плоти его, чист есть.
40 “Tsitsi la munthu likayoyoka kumutu ndiye kuti ndi dazi limenelo koma munthuyo ndi woyeretsedwa.
Аще же кому облезе глава, плешив есть, чист есть:
41 Ngati tsitsi lake layoyoka chapamphumi ndiye kuti ndi dazi la pa chipumi limenelo koma munthuyo ndi woyera.
аще же спреди облезе глава, взлыс есть, чист есть:
42 Koma ngati pa dazi la pamutu kapena la pa chipumi pakhala chithupsa choyera mofiirira, ndiye kuti ndi khate limenelo lochokera mu dazi la pamutu lija kapena pa chipumi lija.
аще же будет на плеши его или на взлысине его блеск бел или червленуяся, прокажение процветающее на плеши его или на взлысине его:
43 Tsono wansembe amuonetsetse wodwalayo ndipo ngati chithupsa cha pa dazi lapankhongo kapena pa dazi lapachipumicho ndi choyera mofiirira monga nthenda ya khate imaonekera,
и увидит его жрец, и се, обличие блеска бело или червлено на плеши его или на взлысине его, яко обличие прокажения на кожи плоти его:
44 ndiye kuti munthuyo ali ndi khate, motero ndi wodetsedwa. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa chifukwa cha chithupsa cha pamutu pakepo.
человек прокажен есть, осквернением осквернит его жрец, на главе его блеск его.
45 “Munthu wa khate lotere avale sanza, tsitsi lake alilekerere, aphimbe mlomo wake wapamwamba ndipo azifuwula kuti, ‘Ndine wodetsedwa, ndine wodetsedwa!’
И прокажен, на немже есть язва, ризы его да будут раздраны, и глава его не покровена, и около уст своих да обвиется, и нечист прозовется:
46 Munthu wodwalayo adzakhala wodetsedwa kwa nthawi yonse imene ali ndi nthendayo. Iye ayenera kumakhala payekha kunja kwa msasa.
вся дни, в няже будет на нем язва, нечист сый, нечист будет: отлучен да седит, вне полка да будет ему пребывание.
47 “Nsalu iliyonse ikakhala ndi nguwi,
И риза аще будет на ней язва прокажения, на ризе сукняне, или на изгребийней,
48 kaya ndi chovala chopangidwa ndi nsalu yathonje kapena yaubweya, yoluka ndi thonje kapena ubweya, yachikopa kapena yopangidwa ndi chikopa,
или на прядене, или на кроках, или на льнех, или на волне, или на кожи, или на всякой кожи деланей,
49 ndipo ngati pamalo pamene pachita nguwiyo pali ndi maonekedwe obiriwira kapena ofiirira imeneyo ndi nguwi yoyipitsa chovala ndipo chovalacho chikaonetsedwe kwa wansembe.
и явится язва зелена или червленуяся на кожи, или на ризе, или на пряденех, или на кроках, или на всяком деле кожанем, язва прокажения есть, и покажет жерцу:
50 Wansembeyo ayionetsetse nguwiyo ndipo chovalacho achiyike padera kwa masiku asanu ndi awiri.
и увидит жрец язву, и отлучит жрец язву на седмь дний.
51 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri ayionetsetsenso nguwiyo ndipo ngati nguwiyo yafalikira pa chovalacho, chathonje kapena chaubweya, kapena pa chikopacho, kaya ndi cha ntchito ya mtundu wanji, imeneyo ndi nguwi yoopsa ndipo chovalacho ndi chodetsedwa.
И да увидит жрец язву в день седмый: аще же разсыпася язва по ризе, или по прядене, или по кроках, или по кожи, по всему елика творятся кожы в делании, прокажение исто есть язва, нечист есть:
52 Wansembe atenthe chovala chathonje kapena chaubweya chija, ngakhalenso chinthu chachikopa chija popeza nguwiyo yachidetsa. Nguwiyo ndi yoopsa choncho chinthucho achitenthe.
да сожжет ризу, или прядения, или кроки, или на волне, или на льне, или на всяком сосуде кожане, на немже аще будет язва: понеже прокажение исто есть, на огни да сожжется.
53 “Koma ngati wansembe akayangʼanitsitsa nguwiyo apeza kuti sinafalikire pa chovalacho kapena pa chinthu chilichonse chachikopa,
Аще ли узрит жрец, и не разсыплется язва по ризе, или по прядене, или по кроках, или по всякому сосуду кожану:
54 iye alamulire kuti chinthu choyipitsidwacho achichape. Akatero achiyike padera kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
и повелит жрец, и измыет, на немже будет язва, и да отлучит жрец язву на другия седмь дний:
55 Chovalacho chitachapidwa, wansembe achionenso ndipo ngati nguwiyo sinasinthe maonekedwe ake, ngakhale kuti sinafalikire, chovalacho ndi chodetsedwa ndithu. Muchitenthe, ngakhale kuti nguwiyo ili kumbuyo kapena kumaso kwa chinthucho.
и увидит жрец по измытии его язву, и аще не изменила язва лица своего, и язва не разсыпася, нечисто есть, на огни да сожжется: утвердися бо на ризе, или на прядене, или на кроках.
56 Koma ngati wansembe aonetsetsa nʼkupeza kuti nguwi ija yathimbirira pa chovala chija kapena pa chinthu chachikopa chija atachichapa, ndiye angʼambeko chinthucho pa banga la nguwiyo.
И аще увидит жрец, и будет темна язва по испрании ея, да отторгнет е от ризы, или от прядена, или от крок, или от кожи.
57 Koma ngati nguwiyo iwonekanso pa chovala chathonje kapena chaubweya ndiye kuti nguwiyo ikufalikira. Chilichonse chimene chili ndi nguwi chiyenera kutenthedwa.
И аще явится еще на ризе или на прядене, или на кроках, или на всяком сосуде кожане, прокажение процветающее есть, на огни да сожжется, на немже есть язва.
58 Chovala chathonje kapena chaubweya, ngakhale chinthu china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, mukachichapa nguwi yake nʼkuchoka muchichapenso kawiri ndipo chidzakhala choyeretsedwa.”
И риза, или прядено, или кроки, или всяк сосуд кожан, еже исперется, и отступит от него язва, и измыется второе, и чисто будет.
59 Amenewa ndiwo malamulo a nguwi yokhala pa chovala chaubweya kapena pa chovala chathonje, kapenanso pa chinthu chilichonse chopangidwa ndi chikopa kuti muzitha kulekanitsa choyeretsedwa ndi chodetsedwa.
Сей закон язве прокажения ризы сукняны, или изгребийны, или прядены, или куделныя, или всякаго сосуда кожана, во еже очистити е, или осквернити е.

< Levitiko 13 >