< Levitiko 13 >

1 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
UThixo wathi kuMosi lo-Aroni,
2 “Munthu akakhala ndi chithupsa, kapena mʼbuko, kapena chikanga pa thupi lake chimene chitha kusanduka nthenda ya khate, abwere naye munthuyo kwa Aaroni wansembe kapena kwa mmodzi mwa ana ake amene ndi ansembe.
“Loba ngubani ozabe evuvukile, loba equbukile, loba elechatha elicazimulayo ejwabini lakhe okungasuka kube ngumkhuhlane wobulephero, kumele alethwe ku-Aroni umphristi loba komunye wamadodana akhe ongumphristi.
3 Tsono wansembe ayangʼanitsitse nthendayo pa khungupo, ndipo ngati ubweya wa pamalo pamene pali nthendapo wasanduka woyera, komanso kuti nthendayo yazama mʼkati kupitirira khungu, ndiye kuti nthendayo ndi khate. Wansembe akamuonetsetsa alengeze kuti ndi wodetsedwa.
Umphristi kahlole lesisilonda esisejwabini lakhe, kuthi kungabonakala ukuthi uboya obusesilondeni sebumhlophe, lokuthi lesilonda laso sizikile enyameni, kuyabe kungumkhuhlane wobulephero. Nxa umphristi emhlola, uzamtshela ukuthi ungcolile ngokomlayo.
4 Ngati chikanga cha pa khungulo chikuoneka choyera, ndipo kuya kwake sikukuonekera kuti kwapitirira khungu ndi ubweya wake pamalopo sunasanduke woyera, wansembe amuyike wodwalayo padera kwa masiku asanu ndi awiri.
Kanti-ke lanxa ibala elisejwabini limhlophe kodwa libonakala ukuthi alijulanga enyameni njalo loboya obukhonapho bungakabimhlophe, umphristi kamsuse ebantwini, ahlale yedwa okwensuku eziyisikhombisa.
5 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso bwino wodwalayo. Ndipo ngati waona kuti nthendayo sinasinthe ndipo sinafalikire pa khungu, amuyikenso wodwalayo padera kwa masiku ena asanu ndi awiri.
Ngosuku lwesikhombisa umphristi kumele amhlole, kuthi-ke nxa ebona ukuthi isilonda lokhu sinjalo njalo kasiqhelanga ejwabini, kumele amehlukanise kwabanye okwezinye njalo insuku eziyisikhombisa.
6 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembeyo amuonenso bwino munthuyo, ndipo ngati nthendayo yazima ndi kusafalikira pa khungu, wansembe amutchule munthuyo kuti ndi woyera. Umenewo unali mʼbuko chabe. Choncho munthuyo achape zovala zake ndipo adzakhala woyera.
Ngosuku lwesikhombisa umphristi uzamhlola njalo, kuthi-ke nxa isilonda sesifiphele singaqhelanga ejwabini, umphristi uzamtshela lowomuntu ukuthi usehlambulukile, bekukade kuyikuqubuka kodwa nje. Leyondoda izagezisa izigqoko zayo njalo iyabe isihlambulukile.
7 Koma ngati mʼbukowo ufalikira pakhungu atakadzionetsa kale kwa wansembe ndipo wansembeyo nʼkulengeza kuti munthuyo ndi woyeretsedwa, ndiye kuti apitenso kukadzionetsa kwa wansembeyo.
Kodwa ukuqubuka kungaqhela ejwabini lakhe ngemva kokuba eseke waziveza kumphristi ukuba kuthiwe usehlambulukile, kumele aziveze njalo kumphristi.
8 Wansembe amuonetsetsenso munthuyo, ndipo ngati mʼbukowo wafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa ndi kuti nthendayo ndi khate.
Umphristi uzamhlola, kuthi-ke nxa ukuqubuka kuqhelile ejwabini, umphristi kumele amtshele ukuthi kakahlambuluki; yibulephero.
9 “Ngati munthu aliyense ali ndi nthenda ya pakhungu yoyipitsa thupi, wodwalayo abwere naye kwa wansembe.
Nxa kulomuntu olobulephero, kumele alethwe kumphristi.
10 Wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati ali ndi chithupsa chamaonekedwe woyera pa khungupo chimene chasandutsa ubweya wa pamalopo kukhala woyera, ndipo ngati pali zilonda pa chotupacho,
Umphristi kamhlole, kuthi nxa kuleqhubu elimhlophe eseliphendule uboya babamhlophe njalo lilomlomo,
11 limenelo ndi khate lachikhalire la pa khungu, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Asamutsekere munthu woteroyo pakuti ndi wodetsedwa kale.
yibulephero, ngakho umphristi uzakuthi ungcolile. Kangamehlukanisi labanye, ngoba uvele esengongcolileyo.
12 “Ndipo ngati, mʼkuona kwa wansembe, khate lija lafalikira pa khungu lonse moti lamugwira thupi lonse kuyambira kumutu mpaka kumapazi,
Nxa ubulephero sobumemetheka umzimba wonke okubonwa ngumphristi ukuthi sobugcwele kusukela ekhanda kuze kube sezinyaweni,
13 wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati khatero lagwira thupi lake lonse, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Popeza kuti thupi lonse lasanduka loyera, munthuyo ndi woyeretsedwa.
umphristi uzamhlola, kuthi nxa bugcwele umzimba wonke, atsho athi lowomuntu uhlambulukile. Njengoba ijwabu seliphenduke labamhlophe lonke, uyabe ehlambulukile.
14 Koma pa tsiku limene zilonda zidzaoneka pa iye, munthuyo adzakhala wodetsedwa.
Kodwa nxa kubonakala sekupetuka inyama esilondeni uzabe engongcolileyo.
15 Wansembe aonetsetse zilondazo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zilondazo ndi zodetsedwa ndipo ili ndi khate.
Umphristi nxa ebona inyama isipetuka uzakuthi ungcolile. Inyama epetukileyo ingcolile; ulobulephero.
16 Koma zilondazo zikasinthika ndi kusanduka zoyera, munthuyo ayenera kupita kwa wansembe.
Kodwa leyonyama epetukileyo ingaguquka ibemhlophe kufanele onjalo aye kumphristi.
17 Wansembe amuonetsetse ndipo ngati zilondazo zasanduka zoyera, wansembe amutchule wodwalayo kuti ndi woyera ndipo adzakhala woyera ndithu.
Umphristi amhlole, kuthi nxa izilonda sezisuke zaba mhlophe, umphristi uzakuthi lowo olazo uhlambulukile; ngakho uzabe esehlambulukile.
18 “Ngati pa khungu la munthu wodwalayo pali chithupsa chimene chinapola kale,
Nxa kulomuntu olethumba ejwabini lakhe libe seliphola,
19 ndipo pamalo pamene panali chithupsacho pakatuluka chotupa choyera kapena banga loyera mofiirira, munthuyo ayenera kukadzionetsa kwa wansembe.
kuthi lapho obekulethumba khona kubonakale kumhlotshana kuvuvukile loba iqhubu elibomvana, kumele azilethe kumphristi.
20 Wansembe aonetsetse bwino ndipo ngati chikuoneka kuti chazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka woyera, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Imeneyo ndi nthenda ya khate imene yatuluka mʼchithupsacho.
Umphristi alihlole, kuthi nxa kubonakala lijulile loboya obuphezu kwalo sebumhlophe, umphristi uzakuthi ungcolile. Yibulephero obuvela lapho obekulethumba khona.
21 Koma ngati wansembe waonetsetsa napeza kuti palibe ubweya woyera ndipo chithupsacho sichinazame, koma chazimirira, wansembeyo amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
Kodwa nxa khona laphayana ekuhlolweni kwalo ngumphristi kungelaboya obumhlophe phezu kwalo, njalo lingajulanga selifiphele, kulapho umphristi azamehlukanisa khona labanye okwensuku eziyisikhombisa.
22 Ngati nthendayo ikufalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limeneli ndi khate.
Nxa liqhela ejwabini, umphristi uzakuthi ungcolile, lona liyisifo esithelelwanayo.
23 Koma bangalo likakhala malo amodzi, wosafalikira, chimenecho ndi chipsera cha chithupsacho, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera.
Kodwa nxa umbala walo ulokhu unjalo, njalo lingaqhelanga, kuyabe kulitshisa elatshiywa lithumba, ngakho umphristi uzakuthi uhlambulukile.
24 “Munthu akakhala ndi bala lamoto pa khungu lake, ndipo chilonda cha balalo chikasanduka banga loyera mofiirira kapena loyera,
Nxa umuntu elethuthuva ejwabini lakhe besekuvela itshatha elibomvana loba elimhlophe enyameni epetukileyo yetshisa,
25 wansembe aonetsetse bangalo, ndipo ngati ubweya wa pa bangapo usanduka woyera, ndipo balalo lioneka kuti ndi lozama, limenelo ndi khate lomwe latuluka pa balalo. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate la pa khungu.
umphristi kalihlole, kuzakuthi nxa uboya obuphezu kwalo sebumhlophe, kubonakale kungani kujulile, yibulephero obuvela ngethuthuva. Umphristi uzakutsho ukuthi ungcolile, yibulephero.
26 Koma ngati wansembe waonetsetsa balalo ndipo palibe ubweya woyera, ndipo ngati balalo silinazame ndi kuti lazirala, wansembe amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
Kodwa umphristi angalihlola kubonakale kungelaboya obumhlophe, kungajulanga njalo sekufiphele, yikho lapho umphristi azamehlukanisa labanye okwensuku eziyisikhombisa.
27 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso wodwalayo, ndipo ngati bangalo lafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate.
Ngosuku lwesikhombisa umphristi uzamhlola, kuthi nxa liqhela ejwabini, umphristi athi ungcolile, yibulephero.
28 Koma ngati bangalo likhala pa malo amodzi wosafalikira pa khungu, ndipo lazimirira, limenelo ndi thuza la bala lamoto, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Chimenecho ndi chipsera chamoto.
Kodwa nxa itshatha lilokhu linjalo futhi lingaqhelanga ejwabini kodwa selifiphele, kuyabe kulithuthuva elivuvukileyo, umphristi uzakuthi uhlambulukile, bekulitshisa nje kuphela.
29 “Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi nthenda kumutu kapena ku chibwano,
Nxa owesilisa loba owesifazane elesilonda ekhanda loba esilevini,
30 wansembe aonetsetse balalo ndipo likaoneka kuti lazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka wachikasu ndi wonyololoka, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zimenezo ndi mfundu zonyerenyetsa, khate lakumutu kapena ku chibwano.
umphristi kasihlole, kuthi nxa kubonakala sijulile enyameni, inwele phezu kwaso sezimpofana njalo zingakhuli, umphristi uzakuthi lowomuntu ungcolile, yibulephero bekhanda loba obesilevu.
31 Koma wansembe akaonetsetsa mfundu zonyerenyetsazo, ndipo zikaoneka kuti sizinazame ndi kuti palibe ubweya wakuda, wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku asanu ndi awiri.
Kodwa nxa umphristi angasihlola isilonda leso abone singajulanga, kungelanwele ezimnyama kuso, umphristi uzamsusa lowomuntu ebantwini okwensuku eziyisikhombisa.
32 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo, ndipo ngati sizinafalikire ndipo palibe ubweya wachikasu pamalopo ndiponso sizinazame,
Ngosuku lwesikhombisa, umphristi kumele asihlole leso silonda, kuthi nxa singaqhelanga ejwabini, njalo kungelaboya obulithanga phezu kwaso, khona kubonakala ukuthi asijulanga enyameni,
33 wodwalayo ametedwe, koma pamene pali mfunduyo pasametedwe. Wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
kufanele aphucwe kutshiywe indawo elesifo, umphristi aphinde amehlukanise kwabanye okwensuku eziyisikhombisa.
34 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo ndipo ngati sizinafalikire pa khungu ndi kuti sizinazame, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Tsono achape zovala zake, ndipo adzakhala woyera.
Ngosuku lwesikhombisa umphristi kumele asihlole, kuthi nxa singaqhelanga njalo kukhanya singajulanga enyameni, umphristi kathi uhlambulukile. Kufanele agezise izigqoko zakhe, abesesiba ngohlambulukileyo.
35 Koma mfundu zonyerenyetsazo zikafalikira pa khungu, wansembe atalengeza kuti ndi woyera,
Kodwa nxa isilonda siqhela ejwabini emva kokuba sekuthiwe usehlambulukile,
36 wansembe amuonetsetsenso wodwalayo ndipo ngati mfunduzo zafalikira pa khungu, iye asalabadirenso zoyangʼana ngati ubweya uli wachikasu. Munthuyo ndi wodetsedwa.
umphristi uzamhlola, kanti-ke nxa isilonda sisuke saqhela ejwabini, akudingakali ukuthi umphristi adinge ukubona uboya obulithanga; lowomuntu ungcolile.
37 Koma ngati wansembe waonetsetsa kuti mfunduzo sizinasinthe ndipo ubweya wakuda wamera pa mfundupo, ndiye kuti wodwalayo wachira. Tsono wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa.
Kodwa nxa ngokubona kwakhe isilonda leso silokhu singaguqukanga sekulenwele ezimnyama kuso, siyabe sesipholile. Uyabe esehlambulukile, umphristi uzakuthi uhlambulukile.
38 “Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi mawanga woyera pa khungu,
Nxa indoda loba owesifazane elamabala amhlotshana ejwabini,
39 wansembe aonetsetse mawangawo, ndipo ngati ali otuwa, ndiye kuti ndi mibuko chabe yotuluka pa khungu. Munthuyo ndi woyera.
umphristi kumele awahlole, kuthi nxa amabala lawo emhlotshana okungani kufiphele, kuyabe kuyikuqubuka okumveleleyo ejwabini; ngakho lowomuntu uhlambulukile.
40 “Tsitsi la munthu likayoyoka kumutu ndiye kuti ndi dazi limenelo koma munthuyo ndi woyeretsedwa.
Nxa indoda ingaselanwele isilempabanga, ihlambulukile.
41 Ngati tsitsi lake layoyoka chapamphumi ndiye kuti ndi dazi la pa chipumi limenelo koma munthuyo ndi woyera.
Nxa ingaselanwele phezu kwebunzi, isilempabanga ihlambulukile.
42 Koma ngati pa dazi la pamutu kapena la pa chipumi pakhala chithupsa choyera mofiirira, ndiye kuti ndi khate limenelo lochokera mu dazi la pamutu lija kapena pa chipumi lija.
Kodwa nxa ilesilonda esibomvana-okumhlotshana ekhanda elilempabanga loba ebunzini, yibulephero obuyabe buqalisa ekhanda loba ebunzini.
43 Tsono wansembe amuonetsetse wodwalayo ndipo ngati chithupsa cha pa dazi lapankhongo kapena pa dazi lapachipumicho ndi choyera mofiirira monga nthenda ya khate imaonekera,
Umphristi kayihlole leyondoda, kuthi nxa isilonda esivuvukayo ekhanda layo loba ebunzini sibomvana-okumhlotshana njengobulephero,
44 ndiye kuti munthuyo ali ndi khate, motero ndi wodetsedwa. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa chifukwa cha chithupsa cha pamutu pakepo.
leyondoda isilabo njalo isingcolile. Umphristi uzakuthi leyondoda ingcolile ngenxa yaleso silonda esisekhanda layo.
45 “Munthu wa khate lotere avale sanza, tsitsi lake alilekerere, aphimbe mlomo wake wapamwamba ndipo azifuwula kuti, ‘Ndine wodetsedwa, ndine wodetsedwa!’
Umuntu olobulephero kumele agqoke izigqoko ezidabukileyo, ayekele inwele zakhe zingakanywanga, embese ingxenye yangaphansi kobuso bakhe amemeze athi: ‘Ngingcolile! Ngingcolile!’
46 Munthu wodwalayo adzakhala wodetsedwa kwa nthawi yonse imene ali ndi nthendayo. Iye ayenera kumakhala payekha kunja kwa msasa.
Kuzakuthi nxa elokhu elaleso sifo, ahlale engongcolileyo. Kumele ahlale yedwa, ahlale ngaphandle kwesihonqo.”
47 “Nsalu iliyonse ikakhala ndi nguwi,
“Nxa isigqoko sagqokwa ngumuntu olobulephero, isembatho sewulu loba eselembu,
48 kaya ndi chovala chopangidwa ndi nsalu yathonje kapena yaubweya, yoluka ndi thonje kapena ubweya, yachikopa kapena yopangidwa ndi chikopa,
eselukiweyo loba esiphothiweyo kuyiwulu loba ilembu, isikhumba loba yini eyenziwe ngesikhumba,
49 ndipo ngati pamalo pamene pachita nguwiyo pali ndi maonekedwe obiriwira kapena ofiirira imeneyo ndi nguwi yoyipitsa chovala ndipo chovalacho chikaonetsedwe kwa wansembe.
nxa lokhu kungcola kusesembathweni selembu, isikhumba, loba yini eyelukiweyo, loba ephothiweyo loba kuyini okwesikhumba, kubonakala kuluhlazana loba kubomvana, yibulephero; kufanele kutshengiswe umphristi.
50 Wansembeyo ayionetsetse nguwiyo ndipo chovalacho achiyike padera kwa masiku asanu ndi awiri.
Umphristi kahlole ukungcola lokhu abesesehlukanisa leyonto esingcolile, ibekwe yodwa okwensuku eziyisikhombisa.
51 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri ayionetsetsenso nguwiyo ndipo ngati nguwiyo yafalikira pa chovalacho, chathonje kapena chaubweya, kapena pa chikopacho, kaya ndi cha ntchito ya mtundu wanji, imeneyo ndi nguwi yoopsa ndipo chovalacho ndi chodetsedwa.
Ngosuku lwesikhombisa kuzamele akuhlole, kuthi nxa ukungcola sekuqhelile esembathweni, eselukiweyo loba esithungiweyo, loba isikhumba, loba sisetshenziswani, lokho kuyibulephero, isembatho leso singcolile.
52 Wansembe atenthe chovala chathonje kapena chaubweya chija, ngakhalenso chinthu chachikopa chija popeza nguwiyo yachidetsa. Nguwiyo ndi yoopsa choncho chinthucho achitenthe.
Kumele asitshise isembatho leso, loba eselukiweyo lesithungiweyo, kuyiwulu loba ilembu, loba kuyinto yesikhumba elesifo sokungcola, njengoba kuyibulephero; leyonto kumele itshiswe.
53 “Koma ngati wansembe akayangʼanitsitsa nguwiyo apeza kuti sinafalikire pa chovalacho kapena pa chinthu chilichonse chachikopa,
Kodwa, nxa kuyikuthi ekuhlolweni kwaso ngumphristi, kubonakale ukuthi isifo asiqhelanga ezigqokweni, loba eselukiweyo loba esithungiweyo, loba esesikhumba,
54 iye alamulire kuti chinthu choyipitsidwacho achichape. Akatero achiyike padera kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
uzalaya ukuthi lololutho olungcolileyo lugeziswe. Kulapho-ke azakwehlukanisa khona kwezinye okwensuku eziyisikhombisa.
55 Chovalacho chitachapidwa, wansembe achionenso ndipo ngati nguwiyo sinasinthe maonekedwe ake, ngakhale kuti sinafalikire, chovalacho ndi chodetsedwa ndithu. Muchitenthe, ngakhale kuti nguwiyo ili kumbuyo kapena kumaso kwa chinthucho.
Ngemva kokuba lesosembatho esingcolileyo sesigezisiwe, umphristi uzasihlola, kuthi nxa isifo sokungcola esisesigqokweni singaguqukanga umbala waso lanxa siyabe singaqhelanga, singcolile. Kasitshiswe ngomlilo, loba isifo sokungcola sihlasele nganxanye.
56 Koma ngati wansembe aonetsetsa nʼkupeza kuti nguwi ija yathimbirira pa chovala chija kapena pa chinthu chachikopa chija atachichapa, ndiye angʼambeko chinthucho pa banga la nguwiyo.
Nxa, lapho umphristi esihlola, kubonakale isilonda sesifiphele ngemva kokugeziswa kwesigqoko, umphristi kadabule ingxenye ebilesifo esigqokweni loba yisikhumba loba ngeselukiweyo loba esiphothiweyo.
57 Koma ngati nguwiyo iwonekanso pa chovala chathonje kapena chaubweya ndiye kuti nguwiyo ikufalikira. Chilichonse chimene chili ndi nguwi chiyenera kutenthedwa.
Kodwa nxa isifo sibonakala futhi esigqokweni, ingabe eselukiweyo loba esiphothiweyo, loba kungesesikhumba, siyabe siyaqhela, akuthi konke okulesifo kutshiswe ngomlilo.
58 Chovala chathonje kapena chaubweya, ngakhale chinthu china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, mukachichapa nguwi yake nʼkuchoka muchichapenso kawiri ndipo chidzakhala choyeretsedwa.”
Isigqoko siphi lasiphi, kungaba ngesokwelukwa, esokuphothwa loba esesikhumba esesike sageziswa sahlanzwa lesosifo kumele sigeziswe futhi, kube yikho ukuhlanzeka kwaso.”
59 Amenewa ndiwo malamulo a nguwi yokhala pa chovala chaubweya kapena pa chovala chathonje, kapenanso pa chinthu chilichonse chopangidwa ndi chikopa kuti muzitha kulekanitsa choyeretsedwa ndi chodetsedwa.
Le yiyo imilayo emayelana lokungcoliswa yibulephero ezigqokweni loba ngezewulu kumbe ezelembu, kungaba ngezelukiweyo loba eziphothiweyo, loba isikhumba; ukuze kuthiwe zihlambulukile loba zingcolile.

< Levitiko 13 >