< Levitiko 13 >
1 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
And Jehovah spoke to Moses and to Aaron, saying,
2 “Munthu akakhala ndi chithupsa, kapena mʼbuko, kapena chikanga pa thupi lake chimene chitha kusanduka nthenda ya khate, abwere naye munthuyo kwa Aaroni wansembe kapena kwa mmodzi mwa ana ake amene ndi ansembe.
When a man shall have in the skin of his flesh a rising, or a scab, or a bright spot, and it becomes in the skin of his flesh a leprous disease, then he shall be brought to Aaron the priest, or to one of his sons the priests.
3 Tsono wansembe ayangʼanitsitse nthendayo pa khungupo, ndipo ngati ubweya wa pamalo pamene pali nthendapo wasanduka woyera, komanso kuti nthendayo yazama mʼkati kupitirira khungu, ndiye kuti nthendayo ndi khate. Wansembe akamuonetsetsa alengeze kuti ndi wodetsedwa.
And the priest shall look on the disease in the skin of the flesh, and if the hair in the disease has turned white, and the appearance of the disease is deeper than the skin of his flesh, it is a leprous disease. And the priest shall look on him, and pronounce him unclean.
4 Ngati chikanga cha pa khungulo chikuoneka choyera, ndipo kuya kwake sikukuonekera kuti kwapitirira khungu ndi ubweya wake pamalopo sunasanduke woyera, wansembe amuyike wodwalayo padera kwa masiku asanu ndi awiri.
And if the bright spot is white in the skin of his flesh, and the appearance of it is not deeper than the skin, and the hair of it has not turned white, then the priest shall shut up the disease seven days.
5 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso bwino wodwalayo. Ndipo ngati waona kuti nthendayo sinasinthe ndipo sinafalikire pa khungu, amuyikenso wodwalayo padera kwa masiku ena asanu ndi awiri.
And the priest shall look on him the seventh day, and, behold, if in his eyes the disease is arrested, and the disease is not spread in the skin, then the priest shall shut him up seven days more.
6 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembeyo amuonenso bwino munthuyo, ndipo ngati nthendayo yazima ndi kusafalikira pa khungu, wansembe amutchule munthuyo kuti ndi woyera. Umenewo unali mʼbuko chabe. Choncho munthuyo achape zovala zake ndipo adzakhala woyera.
And the priest shall look on him again the seventh day, and, behold, if the disease is dim, and the disease has not spread in the skin, then the priest shall pronounce him clean. It is a scab, and he shall wash his clothes, and be clean.
7 Koma ngati mʼbukowo ufalikira pakhungu atakadzionetsa kale kwa wansembe ndipo wansembeyo nʼkulengeza kuti munthuyo ndi woyeretsedwa, ndiye kuti apitenso kukadzionetsa kwa wansembeyo.
But if the scab spreads abroad in the skin after he has shown himself to the priest for his cleansing, he shall show himself to the priest again.
8 Wansembe amuonetsetsenso munthuyo, ndipo ngati mʼbukowo wafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa ndi kuti nthendayo ndi khate.
And the priest shall look, and, behold, if the scab is spread in the skin, then the priest shall pronounce him unclean. It is a leprous disease.
9 “Ngati munthu aliyense ali ndi nthenda ya pakhungu yoyipitsa thupi, wodwalayo abwere naye kwa wansembe.
When the leprous disease is in a man, then he shall be brought to the priest.
10 Wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati ali ndi chithupsa chamaonekedwe woyera pa khungupo chimene chasandutsa ubweya wa pamalopo kukhala woyera, ndipo ngati pali zilonda pa chotupacho,
And the priest shall look, and, behold, if there is a white rising in the skin, and it has turned the hair white, and there is quick raw flesh in the rising,
11 limenelo ndi khate lachikhalire la pa khungu, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Asamutsekere munthu woteroyo pakuti ndi wodetsedwa kale.
it is an old leprous disease in the skin of his flesh, and the priest shall pronounce him unclean. He shall not shut him up, for he is unclean.
12 “Ndipo ngati, mʼkuona kwa wansembe, khate lija lafalikira pa khungu lonse moti lamugwira thupi lonse kuyambira kumutu mpaka kumapazi,
And if the leprous disease breaks out abroad in the skin, and the leprous disease covers all the skin of the disease from his head even to his feet, as far as appears to the priest,
13 wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati khatero lagwira thupi lake lonse, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Popeza kuti thupi lonse lasanduka loyera, munthuyo ndi woyeretsedwa.
then the priest shall look. And, behold, if the leprous disease has covered all his flesh, he shall pronounce him clean of the disease. It is all turned white; he is clean.
14 Koma pa tsiku limene zilonda zidzaoneka pa iye, munthuyo adzakhala wodetsedwa.
But whenever raw flesh appears in him, he shall be unclean.
15 Wansembe aonetsetse zilondazo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zilondazo ndi zodetsedwa ndipo ili ndi khate.
And the priest shall look on the raw flesh, and pronounce him unclean. The raw flesh is unclean; it is a leprous disease.
16 Koma zilondazo zikasinthika ndi kusanduka zoyera, munthuyo ayenera kupita kwa wansembe.
Or if the raw flesh turns again, and is changed to white, then he shall come to the priest.
17 Wansembe amuonetsetse ndipo ngati zilondazo zasanduka zoyera, wansembe amutchule wodwalayo kuti ndi woyera ndipo adzakhala woyera ndithu.
And the priest shall look on him, and, behold, if the disease is turned into white, then the priest shall pronounce him clean of the disease; he is clean.
18 “Ngati pa khungu la munthu wodwalayo pali chithupsa chimene chinapola kale,
And when the flesh has a boil in the skin of it, and it is healed,
19 ndipo pamalo pamene panali chithupsacho pakatuluka chotupa choyera kapena banga loyera mofiirira, munthuyo ayenera kukadzionetsa kwa wansembe.
and in the place of the boil there is a white rising, or a bright spot, reddish-white, then it shall be shown to the priest.
20 Wansembe aonetsetse bwino ndipo ngati chikuoneka kuti chazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka woyera, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Imeneyo ndi nthenda ya khate imene yatuluka mʼchithupsacho.
And the priest shall look, and, behold, if the appearance of it is deeper than the skin, and the hair of it has turned white, then the priest shall pronounce him unclean. It is a leprous disease; it has broken out in the boil.
21 Koma ngati wansembe waonetsetsa napeza kuti palibe ubweya woyera ndipo chithupsacho sichinazame, koma chazimirira, wansembeyo amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
But if the priest looks on it, and, behold, there are no white hairs in it, and it is not deeper than the skin, but is dim, then the priest shall shut him up seven days.
22 Ngati nthendayo ikufalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limeneli ndi khate.
And if it spreads abroad in the skin, then the priest shall pronounce him unclean; it is a disease.
23 Koma bangalo likakhala malo amodzi, wosafalikira, chimenecho ndi chipsera cha chithupsacho, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera.
But if the bright spot stays in its place, and has not spread, it is the scar of the boil, and the priest shall pronounce him clean.
24 “Munthu akakhala ndi bala lamoto pa khungu lake, ndipo chilonda cha balalo chikasanduka banga loyera mofiirira kapena loyera,
Or when the flesh has a burning by fire in the skin of it, and the quick of the burning become a bright spot, reddish-white, or white,
25 wansembe aonetsetse bangalo, ndipo ngati ubweya wa pa bangapo usanduka woyera, ndipo balalo lioneka kuti ndi lozama, limenelo ndi khate lomwe latuluka pa balalo. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate la pa khungu.
then the priest shall look upon it. And, behold, if the hair in the bright spot has turned white, and the appearance of it is deeper than the skin, it is a leprous disease. It has broken out in the burning, and the priest shall pronounce him unclean; it is a leprous disease.
26 Koma ngati wansembe waonetsetsa balalo ndipo palibe ubweya woyera, ndipo ngati balalo silinazame ndi kuti lazirala, wansembe amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
But if the priest looks on it, and, behold, there is no white hair in the bright spot, and it is no deeper than the skin, but is dim, then the priest shall shut him up seven days.
27 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso wodwalayo, ndipo ngati bangalo lafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate.
And the priest shall look upon him the seventh day. If it spread abroad in the skin, then the priest shall pronounce him unclean; it is a leprous disease.
28 Koma ngati bangalo likhala pa malo amodzi wosafalikira pa khungu, ndipo lazimirira, limenelo ndi thuza la bala lamoto, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Chimenecho ndi chipsera chamoto.
And if the bright spot stays in its place, and has not spread in the skin, but is dim, it is the rising of the burning, and the priest shall pronounce him clean, for it is the scar of the burning.
29 “Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi nthenda kumutu kapena ku chibwano,
And when a man or woman has a disease upon the head or upon the beard,
30 wansembe aonetsetse balalo ndipo likaoneka kuti lazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka wachikasu ndi wonyololoka, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zimenezo ndi mfundu zonyerenyetsa, khate lakumutu kapena ku chibwano.
then the priest shall look on the disease. And, behold, if the appearance of it is deeper than the skin, and there is yellow thin hair in it, then the priest shall pronounce him unclean; it is a scall. It is a leprous disease of the head or of the beard.
31 Koma wansembe akaonetsetsa mfundu zonyerenyetsazo, ndipo zikaoneka kuti sizinazame ndi kuti palibe ubweya wakuda, wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku asanu ndi awiri.
And if the priest looks on the disease of the scall, and, behold, the appearance of it is not deeper than the skin, and there is no black hair in it, then the priest shall shut up the disease of the scall seven days.
32 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo, ndipo ngati sizinafalikire ndipo palibe ubweya wachikasu pamalopo ndiponso sizinazame,
And in the seventh day the priest shall look on the disease, and, behold, if the scall has not spread, and there is in it no yellow hair, and the appearance of the scall is not deeper than the skin,
33 wodwalayo ametedwe, koma pamene pali mfunduyo pasametedwe. Wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
then he shall be shaven, but the scall he shall not shave, and the priest shall shut up him who has the scall seven days more.
34 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo ndipo ngati sizinafalikire pa khungu ndi kuti sizinazame, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Tsono achape zovala zake, ndipo adzakhala woyera.
And in the seventh day the priest shall look on the scall, and, behold, if the scall has not spread in the skin, and the appearance of it is not deeper than the skin, then the priest shall pronounce him clean. And he shall wash his clothes, and be clean.
35 Koma mfundu zonyerenyetsazo zikafalikira pa khungu, wansembe atalengeza kuti ndi woyera,
But if the scall spreads abroad in the skin after his cleansing,
36 wansembe amuonetsetsenso wodwalayo ndipo ngati mfunduzo zafalikira pa khungu, iye asalabadirenso zoyangʼana ngati ubweya uli wachikasu. Munthuyo ndi wodetsedwa.
then the priest shall look on him. And, behold, if the scall has spread in the skin, the priest shall not seek for the yellow hair, he is unclean.
37 Koma ngati wansembe waonetsetsa kuti mfunduzo sizinasinthe ndipo ubweya wakuda wamera pa mfundupo, ndiye kuti wodwalayo wachira. Tsono wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa.
But if in his eyes the scall is arrested, and black hair is grown up in it, the scall is healed. He is clean, and the priest shall pronounce him clean.
38 “Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi mawanga woyera pa khungu,
And when a man or a woman has bright spots in the skin of the flesh, even white bright spots,
39 wansembe aonetsetse mawangawo, ndipo ngati ali otuwa, ndiye kuti ndi mibuko chabe yotuluka pa khungu. Munthuyo ndi woyera.
then the priest shall look. And, behold, if the bright spots in the skin of their flesh are of a dull white, it is a tetter. It has broken out in the skin; he is clean.
40 “Tsitsi la munthu likayoyoka kumutu ndiye kuti ndi dazi limenelo koma munthuyo ndi woyeretsedwa.
And if a man's hair is fallen off his head, he is bald; he is clean.
41 Ngati tsitsi lake layoyoka chapamphumi ndiye kuti ndi dazi la pa chipumi limenelo koma munthuyo ndi woyera.
And if his hair is fallen off from the front part of his head, he is forehead bald; he is clean.
42 Koma ngati pa dazi la pamutu kapena la pa chipumi pakhala chithupsa choyera mofiirira, ndiye kuti ndi khate limenelo lochokera mu dazi la pamutu lija kapena pa chipumi lija.
But if there is a reddish-white disease in the bald head, or the bald forehead, it is a leprous disease breaking out in his bald head, or his bald forehead.
43 Tsono wansembe amuonetsetse wodwalayo ndipo ngati chithupsa cha pa dazi lapankhongo kapena pa dazi lapachipumicho ndi choyera mofiirira monga nthenda ya khate imaonekera,
Then the priest shall look upon him, and, behold, if the rising of the disease is reddish-white in his bald head, or in his bald forehead, as the appearance of a leprous disease in the skin of the flesh,
44 ndiye kuti munthuyo ali ndi khate, motero ndi wodetsedwa. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa chifukwa cha chithupsa cha pamutu pakepo.
he is a leprous man; he is unclean. The priest shall surely pronounce him unclean; his disease is on his head.
45 “Munthu wa khate lotere avale sanza, tsitsi lake alilekerere, aphimbe mlomo wake wapamwamba ndipo azifuwula kuti, ‘Ndine wodetsedwa, ndine wodetsedwa!’
And the man with a leprous disease in whom the disease is, his clothes shall be torn, and the hair of his head shall go loose, and he shall cover his upper lip, and shall cry, Unclean, unclean.
46 Munthu wodwalayo adzakhala wodetsedwa kwa nthawi yonse imene ali ndi nthendayo. Iye ayenera kumakhala payekha kunja kwa msasa.
All the days in which the disease is in him he shall be unclean; he is unclean. He shall dwell alone; his dwelling shall be outside the camp.
47 “Nsalu iliyonse ikakhala ndi nguwi,
The garment also that a leprous disease is in, whether it be a woolen garment, or a linen garment,
48 kaya ndi chovala chopangidwa ndi nsalu yathonje kapena yaubweya, yoluka ndi thonje kapena ubweya, yachikopa kapena yopangidwa ndi chikopa,
whether it be in warp, or woof, of linen, or of woolen, whether in a skin, or in anything made of skin,
49 ndipo ngati pamalo pamene pachita nguwiyo pali ndi maonekedwe obiriwira kapena ofiirira imeneyo ndi nguwi yoyipitsa chovala ndipo chovalacho chikaonetsedwe kwa wansembe.
if the disease is greenish or reddish in the garment, or in the skin, or in the warp, or in the woof, or in anything of skin, it is a leprous disease, and shall be shown to the priest.
50 Wansembeyo ayionetsetse nguwiyo ndipo chovalacho achiyike padera kwa masiku asanu ndi awiri.
And the priest shall look upon the disease, and shut up the disease seven days.
51 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri ayionetsetsenso nguwiyo ndipo ngati nguwiyo yafalikira pa chovalacho, chathonje kapena chaubweya, kapena pa chikopacho, kaya ndi cha ntchito ya mtundu wanji, imeneyo ndi nguwi yoopsa ndipo chovalacho ndi chodetsedwa.
And he shall look on the disease on the seventh day. If the disease has spread in the garment, either in the warp, or in the woof, or in the skin, whatever service skin is used for, the disease is a fretting leprosy, it is unclean.
52 Wansembe atenthe chovala chathonje kapena chaubweya chija, ngakhalenso chinthu chachikopa chija popeza nguwiyo yachidetsa. Nguwiyo ndi yoopsa choncho chinthucho achitenthe.
And he shall burn the garment, whether the warp or the woof, in woolen or in linen, or anything of skin, in which the disease is, for it is a fretting leprosy. It shall be burnt in the fire.
53 “Koma ngati wansembe akayangʼanitsitsa nguwiyo apeza kuti sinafalikire pa chovalacho kapena pa chinthu chilichonse chachikopa,
And if the priest shall look, and, behold, the disease has not spread in the garment, either in the warp, or in the woof, or in anything of skin,
54 iye alamulire kuti chinthu choyipitsidwacho achichape. Akatero achiyike padera kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
then the priest shall command that they wash the thing in which the disease is, and he shall shut it up seven more days.
55 Chovalacho chitachapidwa, wansembe achionenso ndipo ngati nguwiyo sinasinthe maonekedwe ake, ngakhale kuti sinafalikire, chovalacho ndi chodetsedwa ndithu. Muchitenthe, ngakhale kuti nguwiyo ili kumbuyo kapena kumaso kwa chinthucho.
And the priest shall look, after the disease is washed, and, behold, if the disease has not changed its color, and the disease has not spread, it is unclean. Thou shall burn it in the fire. It is a fret, whether the bareness be inside or outside.
56 Koma ngati wansembe aonetsetsa nʼkupeza kuti nguwi ija yathimbirira pa chovala chija kapena pa chinthu chachikopa chija atachichapa, ndiye angʼambeko chinthucho pa banga la nguwiyo.
And if the priest looks, and, behold, the disease is dim after the washing of it, then he shall tear it out of the garment, or out of the skin, or out of the warp, or out of the woof.
57 Koma ngati nguwiyo iwonekanso pa chovala chathonje kapena chaubweya ndiye kuti nguwiyo ikufalikira. Chilichonse chimene chili ndi nguwi chiyenera kutenthedwa.
And if it still appears in the garment, either in the warp, or in the woof, or in anything of skin, it is breaking out. Thou shall burn that in which the disease is with fire.
58 Chovala chathonje kapena chaubweya, ngakhale chinthu china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, mukachichapa nguwi yake nʼkuchoka muchichapenso kawiri ndipo chidzakhala choyeretsedwa.”
And the garment, either the warp, or the woof, or whatever thing of skin it be, which thou shall wash, if the disease has departed from them, then it shall be washed the second time, and shall be clean.
59 Amenewa ndiwo malamulo a nguwi yokhala pa chovala chaubweya kapena pa chovala chathonje, kapenanso pa chinthu chilichonse chopangidwa ndi chikopa kuti muzitha kulekanitsa choyeretsedwa ndi chodetsedwa.
This is the law of a leprous disease in a garment of woolen or linen, either in the warp, or the woof, or anything of skin, to pronounce it clean, or to pronounce it unclean.