< Levitiko 12 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
Pǝrwǝrdigar Musaƣa sɵz ⱪilip mundaⱪ dedi: —
2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Mkazi akakhala woyembekezera, nabala mwana wa mwamuna, mkaziyo adzakhala wodetsedwa kwa masiku asanu ndi awiri, ngati pa masiku ake akusamba.
Israillarƣa sɵz ⱪilip mundaⱪ degin: — «Ayal kixi ⱨamilidar bolup oƣul tuƣsa, adǝt kɵrüp aƣriⱪ bolƣan künliridikidǝk yǝttǝ küngiqǝ napak sanalsun.
3 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, mwanayo achite mdulidwe.
Sǝkkizinqi küni oƣli bolsa hǝtnǝ ⱪilinsun.
4 Mkaziyo adikire masiku ena 33 kuti ayeretsedwe ku matenda ake. Asakhudze kanthu kalikonse koyera kapena kulowa mʼmalo wopatulika mpaka masiku a kuyeretsedwa kwake atatha.
Ayal bolsa xuningdin keyin ottuz üq küngiqǝ «ⱪan paklinix»ta tursun; paklinix künliri tamam bolmiƣuqǝ ⱨeqbir muⱪǝddǝs nǝrsigǝ tǝgmisun, muⱪǝddǝs jayƣimu kirmisun.
5 Ngati abala mwana wamkazi, adzakhala wodetsedwa kwa masabata awiri, monga zikhalira pa nthawi yake yosamba. Ndipo mkaziyo adikire masiku ena 66, kuti ayeretsedwe ku matenda akewo.
Əgǝr u ⱪiz tuƣsa undaⱪta adǝt künliridikidǝk ikki ⱨǝptigiqǝ napak turup, andin atmix altǝ küngiqǝ «ⱪan paklinix»ta tursun.
6 “‘Masiku ake wodziyeretsa akatha, kaya ndi a mwana wamwamuna kapena a mwana wamkazi, abwere kwa wansembe ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi pa khomo la tenti ya msonkhano kuti ikhale nsembe yopsereza. Abwerenso ndi chiwunda cha nkhunda kapena njiwa kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
Mǝyli oƣul yaki ⱪiz tuƣsun, ⱪan paklinix künliri tamam bolƣandin keyin u ayal kɵydürmǝ ⱪurbanliⱪ üqün bir yaxⱪa kirgǝn ⱪozini, gunaⱨ ⱪurbanliⱪi üqün bir baqka yaki pahtǝkni elip jamaǝt qedirining kirix aƣziƣa, kaⱨinning ⱪexiƣa kǝltürsun.
7 Wansembeyo apereke zimenezi pamaso pa Yehova pochita mwambo wopepesera mkaziyo. Ndipo mkaziyo adzakhala woyeretsedwa ku msambo wake. “‘Amenewa ndiwo malamulo a mkazi amene wabala mwana wamwamuna kapena wamkazi.
Kaⱨin uni Pǝrwǝrdigarning aldida sunup, xu ayal üqün kafarǝt kǝltüridu; xuning bilǝn u hunidin pak bolidu. Oƣul yaki ⱪiz tuƣⱪan ayal toƣrisidiki ⱪanun-bǝlgilimǝ mana xudur.
8 Ngati mkaziyo sangathe kupeza mwana wankhosa, abwere ndi njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri: imodzi ikhale ya nsembe yopsereza ndipo inayo ikhale ya nsembe yopepesera machimo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera wa mkaziyo ndipo adzayeretsedwa.’”
Əgǝr uning ⱪoziƣa ⱪurbi yǝtmisǝ, u ikki pahtǝk yaki ikki baqka kǝltürsun; ularning biri kɵydürmǝ ⱪurbanliⱪ üqün, yǝnǝ biri gunaⱨ ⱪurbanliⱪi üqün bolidu; xu yol bilǝn kaⱨin uning üqün kafarǝt kǝltüridu; u ayal pak bolidu.

< Levitiko 12 >