< Levitiko 12 >
1 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
I PAN przemówił do Mojżesza:
2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Mkazi akakhala woyembekezera, nabala mwana wa mwamuna, mkaziyo adzakhala wodetsedwa kwa masiku asanu ndi awiri, ngati pa masiku ake akusamba.
Powiedz synom Izraela: Jeśli kobieta pocznie i urodzi chłopca, będzie nieczysta przez siedem dni; jak w dniach jej odłączenia z powodu swej miesięcznej słabości, będzie nieczysta.
3 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, mwanayo achite mdulidwe.
A ósmego dnia zostanie obrzezany jego napletek.
4 Mkaziyo adikire masiku ena 33 kuti ayeretsedwe ku matenda ake. Asakhudze kanthu kalikonse koyera kapena kulowa mʼmalo wopatulika mpaka masiku a kuyeretsedwa kwake atatha.
Potem [ona] pozostanie przez trzydzieści trzy dni we krwi swego oczyszczenia; nie dotknie żadnej świętej rzeczy ani nie wejdzie do świątyni, aż wypełnią się dni jej oczyszczenia.
5 Ngati abala mwana wamkazi, adzakhala wodetsedwa kwa masabata awiri, monga zikhalira pa nthawi yake yosamba. Ndipo mkaziyo adikire masiku ena 66, kuti ayeretsedwe ku matenda akewo.
A jeśli urodzi dziewczynkę, będzie nieczysta przez dwa tygodnie, jak podczas jej odłączenia. Potem pozostanie przez sześćdziesiąt sześć dni we krwi [swego] oczyszczenia.
6 “‘Masiku ake wodziyeretsa akatha, kaya ndi a mwana wamwamuna kapena a mwana wamkazi, abwere kwa wansembe ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi pa khomo la tenti ya msonkhano kuti ikhale nsembe yopsereza. Abwerenso ndi chiwunda cha nkhunda kapena njiwa kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
A gdy wypełnią się dni [jej] oczyszczenia po synu lub po córce, przyniesie do kapłana przed wejście do Namiotu Zgromadzenia rocznego baranka na całopalenie i młodego gołębia lub synogarlicę na ofiarę za grzech;
7 Wansembeyo apereke zimenezi pamaso pa Yehova pochita mwambo wopepesera mkaziyo. Ndipo mkaziyo adzakhala woyeretsedwa ku msambo wake. “‘Amenewa ndiwo malamulo a mkazi amene wabala mwana wamwamuna kapena wamkazi.
Ten złoży to w ofierze przed PANEM i dokona za nią przebłagania; i tak będzie oczyszczona od upływu swojej krwi. Takie jest prawo dla tej, która urodziła chłopca lub dziewczynkę.
8 Ngati mkaziyo sangathe kupeza mwana wankhosa, abwere ndi njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri: imodzi ikhale ya nsembe yopsereza ndipo inayo ikhale ya nsembe yopepesera machimo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera wa mkaziyo ndipo adzayeretsedwa.’”
A jeśli nie może [przynieść] baranka, to przyniesie dwie synogarlice lub dwa młode gołębie: jednego na całopalenie, a drugiego na ofiarę za grzech. I kapłan dokona za nią przebłagania i będzie czysta.