< Levitiko 12 >
1 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
Yahweh also said to Moses/me,
2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Mkazi akakhala woyembekezera, nabala mwana wa mwamuna, mkaziyo adzakhala wodetsedwa kwa masiku asanu ndi awiri, ngati pa masiku ake akusamba.
“Tell this to the Israeli people: ‘If a woman gives birth to a son, she must be avoided for seven days, like she must be avoided when she is menstruating each month.
3 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, mwanayo achite mdulidwe.
The baby son must be circumcised on the eighth day after he is born.
4 Mkaziyo adikire masiku ena 33 kuti ayeretsedwe ku matenda ake. Asakhudze kanthu kalikonse koyera kapena kulowa mʼmalo wopatulika mpaka masiku a kuyeretsedwa kwake atatha.
Then the woman must wait 33 days to be purified from her bleeding [during childbirth]. She must not touch anything that is sacred or enter the Sacred Tent area until that time is ended.
5 Ngati abala mwana wamkazi, adzakhala wodetsedwa kwa masabata awiri, monga zikhalira pa nthawi yake yosamba. Ndipo mkaziyo adikire masiku ena 66, kuti ayeretsedwe ku matenda akewo.
If a woman gives birth to a daughter, she must be avoided for two weeks, like she must be avoided when she is menstruating each month. Then she must wait 66 days to be purified from the bleeding that occurred [when her baby was born].
6 “‘Masiku ake wodziyeretsa akatha, kaya ndi a mwana wamwamuna kapena a mwana wamkazi, abwere kwa wansembe ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi pa khomo la tenti ya msonkhano kuti ikhale nsembe yopsereza. Abwerenso ndi chiwunda cha nkhunda kapena njiwa kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
‘Then that time for her to be purified is ended, that woman must bring to the priest at the entrance of the Sacred Tent a one-year-old lamb to be completely burned [on the altar], and a dove or a young pigeon [to be sacrificed] to enable her to become acceptable to Yahweh again.
7 Wansembeyo apereke zimenezi pamaso pa Yehova pochita mwambo wopepesera mkaziyo. Ndipo mkaziyo adzakhala woyeretsedwa ku msambo wake. “‘Amenewa ndiwo malamulo a mkazi amene wabala mwana wamwamuna kapena wamkazi.
The priest will offer them to Yahweh in order that she may be forgiven for any sins she has committed. Then she will be purified from her loss of blood [when the baby was born]. ‘Those are the regulations for women who give birth to a son or daughter.
8 Ngati mkaziyo sangathe kupeza mwana wankhosa, abwere ndi njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri: imodzi ikhale ya nsembe yopsereza ndipo inayo ikhale ya nsembe yopepesera machimo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera wa mkaziyo ndipo adzayeretsedwa.’”
If a woman who gives birth to a child cannot afford a lamb, she must bring two doves or two young pigeons. One will be burned completely [on the altar], and one will be an offering to enable her to become acceptable to God again. By doing that, the priest will cause that she will be forgiven for any sins she has committed, and she no longer will need to be avoided.’”