< Levitiko 12 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
and to speak: speak LORD to(wards) Moses to/for to say
2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Mkazi akakhala woyembekezera, nabala mwana wa mwamuna, mkaziyo adzakhala wodetsedwa kwa masiku asanu ndi awiri, ngati pa masiku ake akusamba.
to speak: speak to(wards) son: descendant/people Israel to/for to say woman for to sow and to beget male and to defile seven day like/as day impurity be sick she to defile
3 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, mwanayo achite mdulidwe.
and in/on/with day [the] eighth to circumcise flesh foreskin his
4 Mkaziyo adikire masiku ena 33 kuti ayeretsedwe ku matenda ake. Asakhudze kanthu kalikonse koyera kapena kulowa mʼmalo wopatulika mpaka masiku a kuyeretsedwa kwake atatha.
and thirty day and three day to dwell in/on/with blood purity in/on/with all holiness not to touch and to(wards) [the] sanctuary not to come (in): come till to fill day purity her
5 Ngati abala mwana wamkazi, adzakhala wodetsedwa kwa masabata awiri, monga zikhalira pa nthawi yake yosamba. Ndipo mkaziyo adikire masiku ena 66, kuti ayeretsedwe ku matenda akewo.
and if female to beget and to defile week like/as impurity her and sixty day and six day to dwell upon blood purity
6 “‘Masiku ake wodziyeretsa akatha, kaya ndi a mwana wamwamuna kapena a mwana wamkazi, abwere kwa wansembe ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi pa khomo la tenti ya msonkhano kuti ikhale nsembe yopsereza. Abwerenso ndi chiwunda cha nkhunda kapena njiwa kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
and in/on/with to fill day purity her to/for son: child or to/for daughter to come (in): bring lamb son: aged year his to/for burnt offering and son: aged dove or turtledove to/for sin: sin offering to(wards) entrance tent meeting to(wards) [the] priest
7 Wansembeyo apereke zimenezi pamaso pa Yehova pochita mwambo wopepesera mkaziyo. Ndipo mkaziyo adzakhala woyeretsedwa ku msambo wake. “‘Amenewa ndiwo malamulo a mkazi amene wabala mwana wamwamuna kapena wamkazi.
and to present: bring him to/for face: before LORD and to atone upon her and be pure from fountain blood her this instruction [the] to beget to/for male or to/for female
8 Ngati mkaziyo sangathe kupeza mwana wankhosa, abwere ndi njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri: imodzi ikhale ya nsembe yopsereza ndipo inayo ikhale ya nsembe yopepesera machimo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera wa mkaziyo ndipo adzayeretsedwa.’”
and if not to find hand her sufficiency sheep and to take: take two turtledove or two son: young animal dove one to/for burnt offering and one to/for sin: sin offering and to atone upon her [the] priest and be pure

< Levitiko 12 >