< Levitiko 12 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
And the Lord spoke to Moses, saying:
2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Mkazi akakhala woyembekezera, nabala mwana wa mwamuna, mkaziyo adzakhala wodetsedwa kwa masiku asanu ndi awiri, ngati pa masiku ake akusamba.
Speak to the sons of Israel, and you shall say to them: A woman, if she has received the seed to bear a male, shall be unclean for seven days, just as in the days of separation due to menstruation.
3 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, mwanayo achite mdulidwe.
And on the eighth day, the little infant shall be circumcised.
4 Mkaziyo adikire masiku ena 33 kuti ayeretsedwe ku matenda ake. Asakhudze kanthu kalikonse koyera kapena kulowa mʼmalo wopatulika mpaka masiku a kuyeretsedwa kwake atatha.
Yet truly, she herself shall remain for thirty-three days in the blood of her purification. She shall not touch anything holy, nor shall she enter into the Sanctuary, until the days of her purification are completed.
5 Ngati abala mwana wamkazi, adzakhala wodetsedwa kwa masabata awiri, monga zikhalira pa nthawi yake yosamba. Ndipo mkaziyo adikire masiku ena 66, kuti ayeretsedwe ku matenda akewo.
But if she will bear a female, she shall be unclean for two weeks, according to the custom of her monthly flow, and she shall remain in the blood of her purification for sixty-six days.
6 “‘Masiku ake wodziyeretsa akatha, kaya ndi a mwana wamwamuna kapena a mwana wamkazi, abwere kwa wansembe ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi pa khomo la tenti ya msonkhano kuti ikhale nsembe yopsereza. Abwerenso ndi chiwunda cha nkhunda kapena njiwa kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
And when the days of her purification have been completed, for a son or for a daughter, she shall bring to the door of the tabernacle of the testimony, a one-year-old lamb as a holocaust, and a young pigeon or a turtledove for sin, and she shall deliver them to the priest.
7 Wansembeyo apereke zimenezi pamaso pa Yehova pochita mwambo wopepesera mkaziyo. Ndipo mkaziyo adzakhala woyeretsedwa ku msambo wake. “‘Amenewa ndiwo malamulo a mkazi amene wabala mwana wamwamuna kapena wamkazi.
He shall offer them in the sight of the Lord, and he shall pray for her. And so she shall be cleansed from the issue of her blood. This is the law for one who bears a male or a female.
8 Ngati mkaziyo sangathe kupeza mwana wankhosa, abwere ndi njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri: imodzi ikhale ya nsembe yopsereza ndipo inayo ikhale ya nsembe yopepesera machimo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera wa mkaziyo ndipo adzayeretsedwa.’”
And if her hand has not obtained or been able to offer a lamb, she shall take two turtledoves or two young pigeons: one as a holocaust, and the other for sin. And the priest shall pray for her, and so she shall be cleansed.

< Levitiko 12 >