< Levitiko 11 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose ndi Aaroni kuti,
UThixo wathi kuMosi lo-Aroni,
2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Nyama zomwe mukhoza kudya mwa nyama zonse za dziko lapansi ndi izi:
“Alibokuthi kwabako-Israyeli: ‘Kuzozonke izinyamazana ezisemhlabeni, yilezi elingazidla;
3 Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
lingadla zonke izinyamazana ezilenklagu ezivulekileyo lezentshisayo.
4 “‘Koma pali nyama zina zimene zimabzikula kokha kapena ndi zogawikana zipondero zimene simukuyenera kudya. Nyama zimenezi ndi ngamira, ngakhale imabzikula ilibe zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
Zikhona ezinye ezentshisayo kuphela, zibe khona ezinye ezilenklagu ezivulekileyo kuphela kodwa lingabozidla. Ikamela loba lisentshisa kalilanklagu ezivulekileyo; ngomkhuba kalihlanzekanga kini.
5 Ina ndi mbira, ngakhale imabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
Imbila loba isentshisa kayilanklagu ezivulekileyo; ingcolile kini.
6 Inanso ndi kalulu, ngakhale amabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi wodetsedwa, musadye.
Umvundla, loba usentshisa, kawulanklagu ezivulekileyo; ungcolile kini.
7 Nkhumba simabzikula ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
Lengulube, loba ilenklagu ezivulekileyo ngokupheleleyo, ayentshisi; ingcolile kini.
8 Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa chifukwa ndi yodetsedwa.
Akufanelanga lidle inyama yazo njalo akufanelanga lithinte loba izidumbu zazo; ngoba zingcolile kini.
9 “‘Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi a mʼnyanja ndi a mʼmitsinje mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
Kuzozonke izidalwa ezihlala emanzini asolwandle lasezifuleni, lingadla zonke ezilempiko lamaxolo.
10 Koma zamoyo zonse za mʼnyanja kapena za mʼmitsinje zimene zilibe minga ya pa msana ndi mamba, kaya ndi tizirombo tonse ta mʼmadzi ndi zamoyo zonse zopezeka mʼmenemo ndi zodetsedwa kwa inu.
Kodwa zonke izidalwa ezisolwandle lasezifuleni ezingelampiko lamaxolo, kungelani lokuthi ngezihamba ngamaxuku kumbe phakathi kwazo zonke eziphila emanzini kumele lizenyanye.
11 Pakuti zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu, nyama yake musadye, ndipo zikafa zikhalebe zodetsedwa kwa inu.
Njalo njengoba lizazenyanya, lingabokudla inyama yazo, njalo kumele lizenyanye lezidumbu zazo.
12 Chamoyo chilichonse cha mʼmadzi chimene chilibe minga ya pa msana kapena mamba ndi chodetsedwa kwa inu.
Yonke inyamazana ehlala emanzini engalampiko lamaxolo kumele yenyanyeke kini.
13 “‘Mbalame zimene simukuyenera kudya chifukwa ndi zodetsedwa ndi izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
Lezi yizinyoni okumele lizenyanye njalo lingazidli ngoba zingcolile: ukhozi, ilinqe,
14 nankapakapa, akamtema a mitundu yonse,
uhelwane olubomvu, loba wuphi umhlobo wohelwane,
15 akhungubwi a mitundu yonse,
imihlobo yonke yamawabayi,
16 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo ndi mtundu uliwonse wa akabawi
isikhova esilesicholo, isikhova esitshaya udweba, ingabuzane, loba wuphi umhlobo wokhozi,
17 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
umandukulo, itshayamanzi, isikhova esikhulu,
18 tsekwe, vuwo, dembo,
isikhova esimhlophe, isikhova senkangala, ukhozi oludla inhlanzi,
19 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
ingabuzane, lawuphi umhlobo welanda, imvenduna lomalulwane.
20 “‘Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa.
Zonke izibungu ezilamaphiko ezihamba ngenyawo zazo ezine kumele zibe ngezingcolileyo kini.
21 Komabe mwa zowuluka zokhala ndi miyendo inayi zimene mukhoza kudya ndi zokhazo zimene zili ndi miyendo yolumphira.
Kodwa kulezinye izibungu ezilamaphiko, ezihamba ngezinyawo zazo ezine, lingadla lezo ezilamangqondo, ezeqa ngawo emhlabathini.
22 Pa zimenezo mungathe kudya izi: dzombe la mitundu yonse, atsokonombwe a mitundu yonse, nkhululu za mitundu yonse, ndi ziwala za mitundu yonse.
Kuzo lingadla intethe ngemihlobo yazo, lamadiye ngemihlobo yawo.
23 Koma za mapiko zina zonse zokhala ndi miyendo inayi muzitenge kukhala zodetsedwa kwa inu.
Kodwa zonke ezinye izibungu ezilamaphiko lenyawo ezine lizenyanye.
24 “‘Zimenezi zidzakudetsani. Aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
Liyabe liyazingcolisa ngalezi; ngakho loba ngubani othinta izidumbu zazo uzatshona engongcolileyo kuze kuhlwe.
25 Aliyense wonyamula chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
Ozaphakamisa izidumbu zezinyamazana lezi kumele ahlambulule izigqoko zakhe, kanti-ke yena uzaba ngongcolileyo kuze kuhlwe.
26 “‘Nyama iliyonse imene ili ndi ziboda zogawikana koma mapazi ake wosagawikana, kapena imene sibzikula muyiyese yodetsedwa kwa inu ndipo munthu aliyense akakhudza nyama yakufayo, adzakhala wodetsedwa.
Yonke inyamazana elengqina elingehlukananga ngokupheleleyo loba engentshisiyo ingcolile kini, wonke othinta isidumbu sezinyamazana lezi uzabe esengongcolile.
27 Mwa nyama zonse zoyenda ndi miyendo inayi, nyama zonse zokhala ndi zikhadabo kuphazi muzitenge kukhala zodetsedwa ndipo aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
Kuzozonke izinyamazana ezihamba ngenyawo ezine, lezo ezihamba ngezidladla zingcolile kini; kuzakuthi wonke othinta izidumbu zazo abe ngongcolileyo kuze kuhlwe.
28 Aliyense wonyamula nyamazi zitafa ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu.
Loba ngubani ozaphakamisa izidumbu zezinyamazana lezi kumele ahlambulule izigqoko zakhe, njalo uzatshona engongcolileyo kuze kuhlwe. Zingcolile kini.
29 “‘Mwa nyama zokwawa, zimene zili zodetsedwa kwa inu ndi izi: likongwe, mbewa, msambulu za mitundu yonse,
Ezinyamazaneni zonke ezihambahambayo emhlabathini, lezi zingcolile kini: indlegu, igundwane, lemihlobo yonke yemibankwa emikhulu,
30 gondwa, mngʼazi, buluzi, dududu ndi nanzikambe.
untulo, imbulumakhasane, umbankwa, isiqhuza lonwabu.
31 Mwa nyama zonse zoyenda pansi, zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu. Munthu aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
Kuzozonke ezihuquzelayo emhlabathini, lezi zingcolile kini. Loba ngubani ozithinta sezifile uzatshona engongcolileyo kuze kuhlwe.
32 Iliyonse mwa nyama zimenezi ikafa ndi kugwera pa chiwiya chilichonse, kaya chimagwira ntchito yotani, kaya ndi chopangidwa ndi mtengo, kaya ndi cha nsalu, kaya ndi cha chikopa kapena chiguduli chiwiyacho chidzakhala chodetsedwa. Muchiviyike mʼmadzi chiwiyacho komabe chidzakhala chodetsedwa mpaka madzulo, ndipo kenaka chidzakhala choyeretsedwa.
Nxa kungafa eyinye yazo iwele phezu kolutho, lololutho, loba lusetshenziswani luzabe selungolungcolileyo, loba lwenziwe ngesigodo, ngelembu, ngesikhumba loba ngesaka. Lufakeni emanzini; luzabe lungcolile kuze kuhlwe, lapho-ke luzabe seluhlambulukile.
33 Tsono nyama ina iliyonse mwa zimenezi ikagwera mʼmbiya ya dothi, ndiye kuti chilichonse cha mʼmbiyamo chidzakhala chodetsedwa, ndipo muyenera kuswa mbiyayo.
Nxa esinye sazo singawela embizeni yomdaka, konke okusembizeni kuyabe sekungcolile, sekumele ubulale imbiza.
34 Chakudya chilichonse chimene mungadye chikakhala kuti chathiridwa mʼmbiyamo, ndiye kuti chakudyacho chidzakhala chodetsedwa, ndipo madzi akumwa wochokera mʼmbiya zotere ndi wodetsedwa.
Konke ukudla obekungadliwa okuchaphakelwe ngamanzi aleyo mbiza kungcolile, njalo lobekunganathwa kuvela kuleyo mbiza kungcolile.
35 Chiwalo chilichonse cha nyama yakufa chikagwera pa chinthu chilichonse kaya pa uvuni, kapena pa mʼphika, ndiye kuti zinthuzo zidzakhala zodetsedwa, ndipo ziphwanyidwe popeza ndi zodetsedwa.
Loba yini ewelwe yizidumbu zezinanakazana lezi iba ngengcolileyo; iziko loba imbiza yokupheka sekumele kubhidlizwe. Kuyabe sekungcolile, njalo kumele likuthathe njengokungcolileyo.
36 Koma kasupe kapena chitsime chamadzi chidzakhala choyeretsedwa ngakhale kuti chilichonse chokhudza nyama yakufayo chidzakhala chodetsedwa. Zimenezi muzitenge kukhala zodetsedwa.
Kanti-ke, umthombo loba umgqomo wokukha amanzi uhlala uhlambulukile, kodwa loba ngubani othinta izidumbu lezi ungcolile.
37 Chiwalo chilichonse cha nyama yakufayo chikagwera pa mbewu zimene akuti adzale, mbewu zimenezo zidzakhalabe zabwino.
Nxa isidumbu sezinyamazana lezi singawela loba kuyiphi inhlanyelo esilungele ukuhlanyelwa, izahlala ihlambulukile.
38 Koma mbewuzo zikakhala zonyowa ndi madzi, ndipo chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo chikagwera pa mbewuzo, mbewuzo zikhale zodetsedwa kwa inu.
Kodwa nxa amanzi esethelwe enhlanyelweni, isidumbu sakhona besesiwela phezu kwayo, isingcolile kini.
39 “‘Ngati nyama imene mumaloledwa kudya yafa yokha, ndiye kuti aliyense wokhudza nyama yakufayo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
Nxa inyamazana elivunyelwe ukuyidla ingazifela, lowo othinta isidumbu sayo uzakuba ngongcolileyo kuze kuhlwe.
40 Aliyense amene adyako nyama yakufayo achape zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Aliyense amene wanyamula nyama yakufayo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
Loba ngubani ozakudla inyama yalesisidumbu kumele ahlambulule izigqoko zakhe, uzakuba ngongcolileyo kuze kuhlwe. Loba ngubani ozaphakamisa lesisidumbu, kumele ahlambulule izigqoko zakhe, uzakuba ngongcolileyo kuze kuhlwe.
41 “‘Chinthu chilichonse chokwawa pansi ndi chonyansa, simuyenera kudya.
Loba yisiphi isinanakazana esihuquzelayo emhlabathini siyenyanyeka, kasingadliwa.
42 Musadye chilichonse chokwawa pansi, choyenda chamimba kapena choyenda ndi miyendo inayi kapenanso yambiri popeza ndi chodetsedwa.
Akufanelanga lidle izinanakazana zonke ezihambahambayo emhlabathini, loba ngezihuquzela ngezisu loba ngezihamba ngazozonke zone loba ngezilenyawo ezinengi; ziyenyanyeka.
43 Musadzisandutse nokha odetsedwa ndi chokwawa chilichonse. Musadziyipitse nazo, kuti mukhale odetsedwa.
Lingazingcolisi ngezinanakazana lezi, lingazingcolisi ngenxa yazo njalo lingayekeli zilingcolisa.
44 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, choncho dziyeretseni kuti mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera. Musadzisandutse odetsedwa ndi chokwawa chilichonse.
NginguThixo uNkulunkulu wenu, zihlambululeni libengcwele, ngoba mina ngingcwele. Lingazingcolisi ngezinanakazana ezihuquzelayo emhlabathini.
45 Ine ndine Yehova amene ndinakutulutsani ku Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Tsono mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera.
NginguThixo owalikhupha eGibhithe ukuze ngibe nguNkulunkulu wenu; kungakho wobani ngcwele, ngoba mina ngingcwele.
46 “‘Amenewa ndi malamulo onena za nyama, mbalame, chamoyo chilichonse choyenda mʼmadzi ndiponso chamoyo chilichonse chokwawa.
Le yiyo imithetho emayelana lezinyamazana, izinyoni, yonke into ephilayo entsheza emanzini lezinanakazana ezihuquzela emhlabathini.
47 Muzisiyanitsa pakati pa chodetsedwa ndi choyeretsedwa, komanso pakati pa zomwe mutha kudya ndi zomwe simuyenera kudya.’”
Kumele lehlukanise phakathi kwezingcolileyo lezihlambulukileyo, lehlukanise phakathi kwezidalwa eziphilayo ezingadliwa kanye lokungamelanga zidliwe.’”

< Levitiko 11 >