< Levitiko 11 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose ndi Aaroni kuti,
And Jehovah spoke to Moses and to Aaron, saying to them,
2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Nyama zomwe mukhoza kudya mwa nyama zonse za dziko lapansi ndi izi:
Speak unto the children of Israel, saying, These are the animals which ye shall eat of all the beasts which are on the earth.
3 Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
Whatever hath cloven hoofs, and feet quite split open, and cheweth the cud, among the beasts — that shall ye eat.
4 “‘Koma pali nyama zina zimene zimabzikula kokha kapena ndi zogawikana zipondero zimene simukuyenera kudya. Nyama zimenezi ndi ngamira, ngakhale imabzikula ilibe zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
Only these shall ye not eat of those that chew the cud, or of those with cloven hoofs: the camel, for it cheweth the cud, but hath not cloven hoofs — it shall be unclean unto you;
5 Ina ndi mbira, ngakhale imabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
and the rock-badger, for it cheweth the cud, but hath not cloven hoofs — it shall be unclean unto you;
6 Inanso ndi kalulu, ngakhale amabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi wodetsedwa, musadye.
and the hare, for it cheweth the cud, but hath not cloven hoofs — it shall be unclean unto you;
7 Nkhumba simabzikula ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
and the swine, for it hath cloven hoofs, and feet quite split open, but it cheweth not the cud — it shall be unclean unto you.
8 Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa chifukwa ndi yodetsedwa.
Of their flesh shall ye not eat, and their carcase shall ye not touch: they shall be unclean unto you.
9 “‘Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi a mʼnyanja ndi a mʼmitsinje mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
These shall ye eat of all that are in the waters: whatever hath fins and scales in waters, in seas and in rivers, these shall ye eat;
10 Koma zamoyo zonse za mʼnyanja kapena za mʼmitsinje zimene zilibe minga ya pa msana ndi mamba, kaya ndi tizirombo tonse ta mʼmadzi ndi zamoyo zonse zopezeka mʼmenemo ndi zodetsedwa kwa inu.
but all that have not fins and scales in seas and in rivers, of all that swarm in the waters, and of every living soul which is in the waters — they shall be an abomination unto you.
11 Pakuti zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu, nyama yake musadye, ndipo zikafa zikhalebe zodetsedwa kwa inu.
They shall be even an abomination unto you: of their flesh shall ye not eat, and their carcase ye shall have in abomination.
12 Chamoyo chilichonse cha mʼmadzi chimene chilibe minga ya pa msana kapena mamba ndi chodetsedwa kwa inu.
Whatever in the waters hath no fins and scales, that shall be an abomination unto you.
13 “‘Mbalame zimene simukuyenera kudya chifukwa ndi zodetsedwa ndi izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
And these shall ye have in abomination of the fowls; they shall not be eaten; an abomination shall they be: the eagle, and the ossifrage, and the sea-eagle,
14 nankapakapa, akamtema a mitundu yonse,
and the falcon, and the kite, after its kind;
15 akhungubwi a mitundu yonse,
every raven after its kind;
16 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo ndi mtundu uliwonse wa akabawi
and the female ostrich and the male ostrich, and the sea-gull, and the hawk, after its kind;
17 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
and the owl, and the gannet, and the ibis,
18 tsekwe, vuwo, dembo,
and the swan, and the pelican, and the carrion vulture,
19 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
and the stork; the heron after its kind, and the hoopoe, and the bat.
20 “‘Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa.
Every winged crawling thing that goeth upon all four shall be an abomination unto you.
21 Komabe mwa zowuluka zokhala ndi miyendo inayi zimene mukhoza kudya ndi zokhazo zimene zili ndi miyendo yolumphira.
Yet these shall ye eat of every winged crawling thing that goeth upon all four: those which have legs above their feet with which to leap upon the earth.
22 Pa zimenezo mungathe kudya izi: dzombe la mitundu yonse, atsokonombwe a mitundu yonse, nkhululu za mitundu yonse, ndi ziwala za mitundu yonse.
These shall ye eat of them: the arbeh after its kind, and the solam after its kind, and the hargol after its kind, and the hargab after its kind.
23 Koma za mapiko zina zonse zokhala ndi miyendo inayi muzitenge kukhala zodetsedwa kwa inu.
But every winged crawling thing that hath four feet shall be an abomination unto you.
24 “‘Zimenezi zidzakudetsani. Aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
And by these ye shall make yourselves unclean; whoever toucheth their carcase shall be unclean until the even.
25 Aliyense wonyamula chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
And whoever carrieth [ought] of their carcase shall wash his garments, and be unclean until the even.
26 “‘Nyama iliyonse imene ili ndi ziboda zogawikana koma mapazi ake wosagawikana, kapena imene sibzikula muyiyese yodetsedwa kwa inu ndipo munthu aliyense akakhudza nyama yakufayo, adzakhala wodetsedwa.
Every beast that hath cloven hoofs, but not feet quite split open, nor cheweth the cud, shall be unclean unto you: every one that toucheth them shall be unclean.
27 Mwa nyama zonse zoyenda ndi miyendo inayi, nyama zonse zokhala ndi zikhadabo kuphazi muzitenge kukhala zodetsedwa ndipo aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
And whatever goeth on its paws, among all manner of beasts that go upon all four, those are unclean unto you: whoever toucheth their carcase shall be unclean until the even.
28 Aliyense wonyamula nyamazi zitafa ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu.
And he that carrieth their carcase shall wash his garments, and be unclean until the even: they shall be unclean unto you.
29 “‘Mwa nyama zokwawa, zimene zili zodetsedwa kwa inu ndi izi: likongwe, mbewa, msambulu za mitundu yonse,
And these shall be unclean unto you among the crawling things which crawl on the earth: the mole, and the field-mouse, and the lizard, after its kind;
30 gondwa, mngʼazi, buluzi, dududu ndi nanzikambe.
and the groaning lizard, and the great red lizard, and the climbing lizard, and the chomet, and the chameleon.
31 Mwa nyama zonse zoyenda pansi, zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu. Munthu aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
These shall be unclean unto you among all that crawl: whoever toucheth them when they are dead, shall be unclean until the even.
32 Iliyonse mwa nyama zimenezi ikafa ndi kugwera pa chiwiya chilichonse, kaya chimagwira ntchito yotani, kaya ndi chopangidwa ndi mtengo, kaya ndi cha nsalu, kaya ndi cha chikopa kapena chiguduli chiwiyacho chidzakhala chodetsedwa. Muchiviyike mʼmadzi chiwiyacho komabe chidzakhala chodetsedwa mpaka madzulo, ndipo kenaka chidzakhala choyeretsedwa.
And on whatever any of them when they are dead doth fall, it shall be unclean; all vessels of wood, or garment, or skin, or sack, every vessel wherewith work is done — it shall be put into water, and be unclean until the even; then shall it be clean.
33 Tsono nyama ina iliyonse mwa zimenezi ikagwera mʼmbiya ya dothi, ndiye kuti chilichonse cha mʼmbiyamo chidzakhala chodetsedwa, ndipo muyenera kuswa mbiyayo.
And every earthen vessel into which [any] of them falleth — whatever is in it shall be unclean; and ye shall break it.
34 Chakudya chilichonse chimene mungadye chikakhala kuti chathiridwa mʼmbiyamo, ndiye kuti chakudyacho chidzakhala chodetsedwa, ndipo madzi akumwa wochokera mʼmbiya zotere ndi wodetsedwa.
All food that is eaten on which [such] water hath come shall be unclean; and all drink that is drunk shall be unclean, in every [such] vessel.
35 Chiwalo chilichonse cha nyama yakufa chikagwera pa chinthu chilichonse kaya pa uvuni, kapena pa mʼphika, ndiye kuti zinthuzo zidzakhala zodetsedwa, ndipo ziphwanyidwe popeza ndi zodetsedwa.
And everything where upon [any part] of their carcase falleth shall be unclean; oven and hearth shall be broken down: they are unclean, and shall be unclean unto you.
36 Koma kasupe kapena chitsime chamadzi chidzakhala choyeretsedwa ngakhale kuti chilichonse chokhudza nyama yakufayo chidzakhala chodetsedwa. Zimenezi muzitenge kukhala zodetsedwa.
Nevertheless, a spring or a well, a quantity of water, shall be clean. But he that toucheth their carcase shall be unclean.
37 Chiwalo chilichonse cha nyama yakufayo chikagwera pa mbewu zimene akuti adzale, mbewu zimenezo zidzakhalabe zabwino.
And if any part of their carcase fall upon any sowing-seed which is to be sown, it shall be clean;
38 Koma mbewuzo zikakhala zonyowa ndi madzi, ndipo chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo chikagwera pa mbewuzo, mbewuzo zikhale zodetsedwa kwa inu.
but if water have been put on the seed, and any part of their carcase fall thereon, it shall be unclean unto you.
39 “‘Ngati nyama imene mumaloledwa kudya yafa yokha, ndiye kuti aliyense wokhudza nyama yakufayo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
And if any beast which is to you for food die, he that toucheth the carcase thereof shall be unclean until the even.
40 Aliyense amene adyako nyama yakufayo achape zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Aliyense amene wanyamula nyama yakufayo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
And he that eateth of its carcase shall wash his garments, and be unclean until the even: he also that carrieth its carcase shall wash his garments, and be unclean until the even.
41 “‘Chinthu chilichonse chokwawa pansi ndi chonyansa, simuyenera kudya.
And every crawling thing which crawleth on the earth shall be an abomination; it shall not be eaten.
42 Musadye chilichonse chokwawa pansi, choyenda chamimba kapena choyenda ndi miyendo inayi kapenanso yambiri popeza ndi chodetsedwa.
Whatever goeth on the belly, and whatever goeth on all four, and all that have a great many feet, of every manner of crawling thing which crawleth on the earth — these ye shall not eat; for they are an abomination.
43 Musadzisandutse nokha odetsedwa ndi chokwawa chilichonse. Musadziyipitse nazo, kuti mukhale odetsedwa.
Ye shall not make yourselves abominable through any crawling thing which crawleth, neither shall ye make yourselves unclean with them, that ye should be defiled thereby.
44 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, choncho dziyeretseni kuti mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera. Musadzisandutse odetsedwa ndi chokwawa chilichonse.
For I am Jehovah your God; and ye shall hallow yourselves, and ye shall be holy; for I am holy; and ye shall not make yourselves unclean through any manner of crawling thing which creepeth on the earth.
45 Ine ndine Yehova amene ndinakutulutsani ku Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Tsono mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera.
For I am Jehovah who brought you up out of the land of Egypt, to be your God: ye shall therefore be holy, for I am holy.
46 “‘Amenewa ndi malamulo onena za nyama, mbalame, chamoyo chilichonse choyenda mʼmadzi ndiponso chamoyo chilichonse chokwawa.
This is the law of cattle, and of fowl, and of every living soul that moveth in the waters, and of every soul that crawleth on the earth;
47 Muzisiyanitsa pakati pa chodetsedwa ndi choyeretsedwa, komanso pakati pa zomwe mutha kudya ndi zomwe simuyenera kudya.’”
to make a difference between the unclean and the clean, and between the beast that is to be eaten and the beast that is not to be eaten.

< Levitiko 11 >