< Levitiko 10 >

1 Ana a Aaroni, Nadabu ndi Abihu, aliyense anatenga chofukizira lubani chake nayikamo makala a moto ndi kuthiramo lubani. Iwo anapereka pamaso pa Yehova moto wachilendo, moto umene Yehova sanawalamule.
А синови Аронови, Надав и Авијуд, узевши сваки своју кадионицу метнуше огањ у њих и на огањ метнуше кад, и принесоше пред Господом огањ туђ, а то им не беше заповедио.
2 Choncho moto unatuluka pamaso pa Yehova ndi kuwapsereza, ndipo anafa pamaso pa Yehova.
Тада дође огањ од Господа и удари их, те погибоше пред Господом.
3 Pamenepo Mose anawuza Aaroni kuti, “Pajatu Yehova ananena kuti, “‘Kwa iwo amene amandiyandikira ndidzaonetsa ulemerero wanga; pamaso pa anthu onse ndidzalemekezedwa.’” Aaroni anakhala chete wosayankhula.
Тада рече Мојсије Арону: То је што је казао Господ говорећи: У онима који приступају к мени бићу свет и пред целим народом прославићу се. А Арон оћуте.
4 Mose anayitana Misaeli ndi Elizafani, ana a Uzieli, abambo angʼono a Aaroni, ndipo anawawuza kuti, “Bwerani kuno mudzachotse abale anuwa pa malo wopatulika ndi kuwatulutsira kunja kwa msasa.”
А Мојсије позва Мисаила и Елисафана синове Озила стрица Ароновог, и рече им: Ходите и изнесите браћу своју испред светиње напоље из логора.
5 Choncho anabwera atavala minjiro yawo ndipo anawatenga ndi kuwatulutsa kunja kwa msasawo monga momwe Mose analamulira.
И приступише и изнесоше их у кошуљама њиховим напоље из логора, као што рече Мојсије.
6 Ndipo Mose anawuza Aaroni ndi ana ake Eliezara ndi Itamara kuti, “Musalileke tsitsi lanu nyankhalala ndipo musangʼambe zovala zanu kuti mungafe, ndi mkwiyo wa Yehova ungagwere anthu onsewa. Koma abale anu okha, kutanthauza fuko lonse la Israeli ndiwo ayenera kulira omwalira aja amene Yehova wawapsereza ndi moto.
Тада рече Мојсије Арону и Елеазару и Итамару, синовима његовим: Немојте откривати глава својих, ни хаљина својих раздирати, да не изгинете и да се Господ не разгневи на сав збор; него браћа ваша, сав род Израиљев, нека плаче ради пожара који учини Господ.
7 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano, mungafe, chifukwa munadzozedwa ndi mafuta a Yehova kukhala ansembe.” Choncho iwo anachita monga Mose ananenera.
И с врата шатора од састанка немојте излазити, да не изгинете, јер је на вама уље помазања Господњег. И учинише по речи Мојсијевој.
8 Pambuyo pake Yehova anayankhula ndi Aaroni nati,
И Господ рече Арону говорећи:
9 “Iwe ndi ana ako musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa pamene mukulowa mu tenti ya msonkhano kuti mungafe. Ili ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse.
Вино и силовито пиће немој пити ти ни синови твоји с тобом, кад улазите у шатор од састанка да не изгинете. То нека вам је уредба вечна од колена на колено.
10 Muzisiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, pakati pa zinthu zodetsedwa ndi zinthu zoyeretsedwa,
Да бисте могли распознавати шта је свето шта ли није, и шта је чисто шта ли нечисто.
11 ndipo muyenera kuphunzitsa Aisraeli onse malamulo amene Yehova wakupatsani kudzera mwa Mose.”
И да бисте учили синове Израиљеве свим уредбама које им је казао Господ преко Мојсија.
12 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake otsalawo, Eliezara ndi Itamara kuti, “Tengani zopereka zachakudya zopanda yisiti zimene zatsala pa nsembe zopsereza za kwa Yehova ndipo muzidye pafupi ndi guwa pakuti ndi zopatulika kwambiri.
А Мојсије рече Арону и Елеазару и Итамару синовима његовим који осташе: Узимајте дар што остане од огњених жртава Господњих, и једите с хлебом пресним код олтара, јер је светиња над светињама.
13 Muzidye pa malo wopatulika chifukwa zimenezi ndi gawo lako ndi la ana ako pa zopereka zopsereza kwa Yehova. Izitu ndi zimene Yehova anandilamulira.
Зато ћете га јести на светом месту, јер је део твој и део синова твојих од огњених жртава Господњих; јер ми је тако заповеђено.
14 Koma iwe pamodzi ndi ana ako aamuna ndi aakazi muzidya chidale chimene chinaweyulidwa ndi ntchafu zimene zinaperekedwa nsembe. Muzidye pamalo woyeretsedwa. Zimenezi zaperekedwa kwa iwe ndi ana ako monga gawo lanu pa zopereka zachiyanjano zimene apereka Aisraeli.
А груди од жртве обртане и плеће од жртве подизане једите на чистом месту, ти и синови твоји и кћери твоје с тобом; јер је тај део дан теби и синовима твојим од захвалних жртава синова Израиљевих.
15 Ntchafu imene inaperekedwayo ndi chidale chomwe chinaweyulidwacho abwere nazo pamodzi ndi nsembe ya mafuta ya Yehova yotentha pa moto, ndipo uziweyule kuti zikhale zopereka zoweyula pamaso pa Yehova. Zimenezi zizikhala zako ndi ana ako nthawi zonse monga walamulira Yehova.”
Плеће од жртве подизане и груди од жртве обртане доносиће се са салом што се сажиже, да се обрне тамо и амо пред Господом, и биће твоје и синова твојих с тобом законом вечним, као што је заповедио Господ.
16 Pambuyo pake Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yopepesera machimo koma anapeza kuti anayitentha kale. Apa Mose anakalipira Eliezara ndi Itamara, ana a Aaroni otsala aja nati,
И Мојсије потражи јаре за грех; али гле, беше изгорело; зато се разгневи на Елеазара и на Итамара синове Аронове који осташе, и рече:
17 “Chifukwa chiyani simunadyere pamalo wopatulika nsembe yopepesera machimo ija? Kodi imene ija siyopatulika? Kodi Yehova sanapereke nyamayo kwa inu kuti muchotse machimo a mpingo wonse powachitira mwambo wa nsembe yopepesera machimo pamaso pa Yehova?
Зашто не једосте жртве за грех на светом месту? Светиња је над светињама, и даде вам је Господ да носите грех свега збора, да би се очистили од греха пред Господом.
18 Pakuti magazi ake sanalowe nawo ku Malo Wopatulika, mukanadya nyama ya mbuziyo pa malo wopatulikawo monga Yehova analamulira.”
А ето крв њена није унесена у светињу; ваљаше вам је јести на светом месту, као што сам заповедио.
19 Aaroni anamuyankha Mose kuti, “Lero anthu apereka nsembe yawo yopepesera machimo ndiponso nsembe yawo yopsereza pamaso pa Yehova komabe zinthu zoterezi zandichitikira. Kodi Yehova akanakondwa ndikanadya nsembe yopepesera machimo lero?”
Тада рече Арон Мојсију: Ето, данас принесоше жртву своју за грех и жртву своју паљеницу пред Господом, и то ми се догоди. А да сам данас јео жртве за грех, би ли било по вољи Господу?
20 Pamene Mose anamva zimenezi, anakhutira.
Кад чу то Мојсије, приста на то.

< Levitiko 10 >