< Levitiko 10 >

1 Ana a Aaroni, Nadabu ndi Abihu, aliyense anatenga chofukizira lubani chake nayikamo makala a moto ndi kuthiramo lubani. Iwo anapereka pamaso pa Yehova moto wachilendo, moto umene Yehova sanawalamule.
Nadab et Abihu, fils d'Aaron, prirent chacun leur brasier, y mirent du feu, y déposèrent du parfum, et offrirent devant l'Éternel un feu étranger qu'il ne leur avait pas ordonné.
2 Choncho moto unatuluka pamaso pa Yehova ndi kuwapsereza, ndipo anafa pamaso pa Yehova.
Le feu sortit de devant l'Éternel, les dévora, et ils moururent devant l'Éternel.
3 Pamenepo Mose anawuza Aaroni kuti, “Pajatu Yehova ananena kuti, “‘Kwa iwo amene amandiyandikira ndidzaonetsa ulemerero wanga; pamaso pa anthu onse ndidzalemekezedwa.’” Aaroni anakhala chete wosayankhula.
Moïse dit alors à Aaron: « C'est ce dont Yahvé a parlé, en disant, Je me montrerai saint pour ceux qui s'approchent de moi, et devant tout le peuple, je serai glorifié. » Aaron se tut.
4 Mose anayitana Misaeli ndi Elizafani, ana a Uzieli, abambo angʼono a Aaroni, ndipo anawawuza kuti, “Bwerani kuno mudzachotse abale anuwa pa malo wopatulika ndi kuwatulutsira kunja kwa msasa.”
Moïse appela Mischaël et Elzaphan, fils d'Uzziel, oncle d'Aaron, et leur dit: « Approchez, portez hors du camp vos frères qui sont devant le sanctuaire. »
5 Choncho anabwera atavala minjiro yawo ndipo anawatenga ndi kuwatulutsa kunja kwa msasawo monga momwe Mose analamulira.
Ils s'approchèrent donc et les transportèrent dans leurs tuniques hors du camp, comme Moïse l'avait dit.
6 Ndipo Mose anawuza Aaroni ndi ana ake Eliezara ndi Itamara kuti, “Musalileke tsitsi lanu nyankhalala ndipo musangʼambe zovala zanu kuti mungafe, ndi mkwiyo wa Yehova ungagwere anthu onsewa. Koma abale anu okha, kutanthauza fuko lonse la Israeli ndiwo ayenera kulira omwalira aja amene Yehova wawapsereza ndi moto.
Moïse dit à Aaron, à Eléazar et à Ithamar, ses fils: « Ne laissez pas tomber les cheveux de vos têtes et ne déchirez pas vos vêtements, afin que vous ne mouriez pas et qu'il ne s'irrite pas contre toute l'assemblée; mais que vos frères, toute la maison d'Israël, se lamentent sur le feu que Yahvé a allumé.
7 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano, mungafe, chifukwa munadzozedwa ndi mafuta a Yehova kukhala ansembe.” Choncho iwo anachita monga Mose ananenera.
Tu ne sortiras pas de l'entrée de la tente de la Rencontre, de peur de mourir, car l'huile d'onction de l'Éternel est sur toi. » Ils firent selon la parole de Moïse.
8 Pambuyo pake Yehova anayankhula ndi Aaroni nati,
Puis Yahvé dit à Aaron:
9 “Iwe ndi ana ako musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa pamene mukulowa mu tenti ya msonkhano kuti mungafe. Ili ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse.
« Toi et tes fils, vous ne boirez ni vin ni boisson forte chaque fois que vous entrerez dans la Tente de la Rencontre, sinon vous mourrez. Ceci sera une loi pour toujours, de génération en génération.
10 Muzisiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, pakati pa zinthu zodetsedwa ndi zinthu zoyeretsedwa,
Tu feras la distinction entre ce qui est saint et ce qui est commun, entre ce qui est impur et ce qui est pur.
11 ndipo muyenera kuphunzitsa Aisraeli onse malamulo amene Yehova wakupatsani kudzera mwa Mose.”
Tu enseigneras aux enfants d'Israël toutes les lois que l'Éternel leur a dites par Moïse. »
12 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake otsalawo, Eliezara ndi Itamara kuti, “Tengani zopereka zachakudya zopanda yisiti zimene zatsala pa nsembe zopsereza za kwa Yehova ndipo muzidye pafupi ndi guwa pakuti ndi zopatulika kwambiri.
Moïse parla à Aaron, à Éléazar et à Ithamar, ses fils qui étaient restés: Prenez l'offrande qui reste des sacrifices consumés par le feu devant l'Éternel, et mangez-la sans levure à côté de l'autel, car elle est très sainte.
13 Muzidye pa malo wopatulika chifukwa zimenezi ndi gawo lako ndi la ana ako pa zopereka zopsereza kwa Yehova. Izitu ndi zimene Yehova anandilamulira.
Vous la mangerez dans un lieu saint, car c'est votre part et la part de vos fils des sacrifices consumés par le feu devant l'Éternel; c'est ce que je vous ordonne.
14 Koma iwe pamodzi ndi ana ako aamuna ndi aakazi muzidya chidale chimene chinaweyulidwa ndi ntchafu zimene zinaperekedwa nsembe. Muzidye pamalo woyeretsedwa. Zimenezi zaperekedwa kwa iwe ndi ana ako monga gawo lanu pa zopereka zachiyanjano zimene apereka Aisraeli.
Vous mangerez la poitrine ondulée et la cuisse levée dans un lieu pur, toi, tes fils et tes filles avec toi, car elles sont données comme votre part et la part de vos fils, dans les sacrifices d'actions de grâces des enfants d'Israël.
15 Ntchafu imene inaperekedwayo ndi chidale chomwe chinaweyulidwacho abwere nazo pamodzi ndi nsembe ya mafuta ya Yehova yotentha pa moto, ndipo uziweyule kuti zikhale zopereka zoweyula pamaso pa Yehova. Zimenezi zizikhala zako ndi ana ako nthawi zonse monga walamulira Yehova.”
Ils apporteront la cuisse levée et la poitrine agitée, avec les offrandes consumées par le feu de la graisse, pour l'agiter en sacrifice par élévation devant l'Éternel. Ce sera votre part, et celle de vos fils avec vous, comme une part pour toujours, comme Yahvé l'a ordonné. »
16 Pambuyo pake Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yopepesera machimo koma anapeza kuti anayitentha kale. Apa Mose anakalipira Eliezara ndi Itamara, ana a Aaroni otsala aja nati,
Moïse s'enquit du bouc du sacrifice pour le péché, et voici qu'il était brûlé. Moïse se mit en colère contre Éléazar et Ithamar, les fils d'Aaron qui restaient, et dit:
17 “Chifukwa chiyani simunadyere pamalo wopatulika nsembe yopepesera machimo ija? Kodi imene ija siyopatulika? Kodi Yehova sanapereke nyamayo kwa inu kuti muchotse machimo a mpingo wonse powachitira mwambo wa nsembe yopepesera machimo pamaso pa Yehova?
« Pourquoi n'avez-vous pas mangé le sacrifice pour le péché dans le lieu du sanctuaire, puisqu'il est très saint et qu'il vous a été donné de porter l'iniquité de l'assemblée, afin de faire l'expiation pour elle devant Yahvé?
18 Pakuti magazi ake sanalowe nawo ku Malo Wopatulika, mukanadya nyama ya mbuziyo pa malo wopatulikawo monga Yehova analamulira.”
Voici, son sang n'a pas été apporté dans l'intérieur du sanctuaire. Vous auriez certainement dû le manger dans le sanctuaire, comme je l'ai ordonné. »
19 Aaroni anamuyankha Mose kuti, “Lero anthu apereka nsembe yawo yopepesera machimo ndiponso nsembe yawo yopsereza pamaso pa Yehova komabe zinthu zoterezi zandichitikira. Kodi Yehova akanakondwa ndikanadya nsembe yopepesera machimo lero?”
Aaron dit à Moïse: « Voici, ils ont offert aujourd'hui leur sacrifice pour le péché et leur holocauste devant l'Éternel, et il m'est arrivé des choses comme celles-là. Si j'avais mangé aujourd'hui le sacrifice pour le péché, cela aurait-il été agréable aux yeux de Yahvé? ».
20 Pamene Mose anamva zimenezi, anakhutira.
Lorsque Moïse entendit cela, cela lui plut.

< Levitiko 10 >