< Levitiko 10 >

1 Ana a Aaroni, Nadabu ndi Abihu, aliyense anatenga chofukizira lubani chake nayikamo makala a moto ndi kuthiramo lubani. Iwo anapereka pamaso pa Yehova moto wachilendo, moto umene Yehova sanawalamule.
and to take: take son: child Aaron Nadab and Abihu man: anyone censer his and to give: put in/on/with them fire and to set: put upon her incense and to present: bring to/for face: before LORD fire be a stranger which not to command [obj] them
2 Choncho moto unatuluka pamaso pa Yehova ndi kuwapsereza, ndipo anafa pamaso pa Yehova.
and to come out: issue fire from to/for face: before LORD and to eat [obj] them and to die to/for face: before LORD
3 Pamenepo Mose anawuza Aaroni kuti, “Pajatu Yehova ananena kuti, “‘Kwa iwo amene amandiyandikira ndidzaonetsa ulemerero wanga; pamaso pa anthu onse ndidzalemekezedwa.’” Aaroni anakhala chete wosayankhula.
and to say Moses to(wards) Aaron he/she/it which to speak: speak LORD to/for to say in/on/with near my to consecrate: consecate and upon face: before all [the] people to honor: honour and to silence: silent Aaron
4 Mose anayitana Misaeli ndi Elizafani, ana a Uzieli, abambo angʼono a Aaroni, ndipo anawawuza kuti, “Bwerani kuno mudzachotse abale anuwa pa malo wopatulika ndi kuwatulutsira kunja kwa msasa.”
and to call: call to Moses to(wards) Mishael and to(wards) Elizaphan son: child Uzziel beloved: male relative Aaron and to say to(wards) them to present: come to lift: bear [obj] brother: male-sibling your from with face: before [the] holiness to(wards) from outside to/for camp
5 Choncho anabwera atavala minjiro yawo ndipo anawatenga ndi kuwatulutsa kunja kwa msasawo monga momwe Mose analamulira.
and to present: come and to lift: bear them in/on/with tunic their to(wards) from outside to/for camp like/as as which to speak: speak Moses
6 Ndipo Mose anawuza Aaroni ndi ana ake Eliezara ndi Itamara kuti, “Musalileke tsitsi lanu nyankhalala ndipo musangʼambe zovala zanu kuti mungafe, ndi mkwiyo wa Yehova ungagwere anthu onsewa. Koma abale anu okha, kutanthauza fuko lonse la Israeli ndiwo ayenera kulira omwalira aja amene Yehova wawapsereza ndi moto.
and to say Moses to(wards) Aaron and to/for Eleazar and to/for Ithamar son: child his head your not to neglect and garment your not to tear and not to die and upon all [the] congregation be angry and brother: male-sibling your all house: household Israel to weep [obj] [the] fire which to burn LORD
7 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano, mungafe, chifukwa munadzozedwa ndi mafuta a Yehova kukhala ansembe.” Choncho iwo anachita monga Mose ananenera.
and from entrance tent meeting not to come out: come lest to die for oil anointing LORD upon you and to make: do like/as word Moses
8 Pambuyo pake Yehova anayankhula ndi Aaroni nati,
and to speak: speak LORD to(wards) Aaron to/for to say
9 “Iwe ndi ana ako musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa pamene mukulowa mu tenti ya msonkhano kuti mungafe. Ili ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse.
wine and strong drink not to drink you(m. s.) and son: child your with you in/on/with to come (in): come you to(wards) tent meeting and not to die statute forever: enduring to/for generation your
10 Muzisiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, pakati pa zinthu zodetsedwa ndi zinthu zoyeretsedwa,
and to/for to separate between [the] holiness and between [the] common and between [the] unclean and between [the] pure
11 ndipo muyenera kuphunzitsa Aisraeli onse malamulo amene Yehova wakupatsani kudzera mwa Mose.”
and to/for to show [obj] son: descendant/people Israel [obj] all [the] statute: decree which to speak: speak LORD to(wards) them in/on/with hand: by Moses
12 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake otsalawo, Eliezara ndi Itamara kuti, “Tengani zopereka zachakudya zopanda yisiti zimene zatsala pa nsembe zopsereza za kwa Yehova ndipo muzidye pafupi ndi guwa pakuti ndi zopatulika kwambiri.
and to speak: speak Moses to(wards) Aaron and to(wards) Eleazar and to(wards) Ithamar son: child his [the] to remain to take: take [obj] [the] offering [the] to remain from food offering LORD and to eat her unleavened bread beside [the] altar for holiness holiness he/she/it
13 Muzidye pa malo wopatulika chifukwa zimenezi ndi gawo lako ndi la ana ako pa zopereka zopsereza kwa Yehova. Izitu ndi zimene Yehova anandilamulira.
and to eat [obj] her in/on/with place holy for statute: portion your and statute: portion son: child your he/she/it from food offering LORD for so to command
14 Koma iwe pamodzi ndi ana ako aamuna ndi aakazi muzidya chidale chimene chinaweyulidwa ndi ntchafu zimene zinaperekedwa nsembe. Muzidye pamalo woyeretsedwa. Zimenezi zaperekedwa kwa iwe ndi ana ako monga gawo lanu pa zopereka zachiyanjano zimene apereka Aisraeli.
and [obj] breast [the] wave offering and [obj] leg [the] contribution to eat in/on/with place pure you(m. s.) and son: child your and daughter your with you for statute: portion your and statute: portion son: child your to give: give from sacrifice peace offering son: descendant/people Israel
15 Ntchafu imene inaperekedwayo ndi chidale chomwe chinaweyulidwacho abwere nazo pamodzi ndi nsembe ya mafuta ya Yehova yotentha pa moto, ndipo uziweyule kuti zikhale zopereka zoweyula pamaso pa Yehova. Zimenezi zizikhala zako ndi ana ako nthawi zonse monga walamulira Yehova.”
leg [the] contribution and breast [the] wave offering upon food offering [the] fat to come (in): bring to/for to wave wave offering to/for face: before LORD and to be to/for you and to/for son: child your with you to/for statute: portion forever: enduring like/as as which to command LORD
16 Pambuyo pake Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yopepesera machimo koma anapeza kuti anayitentha kale. Apa Mose anakalipira Eliezara ndi Itamara, ana a Aaroni otsala aja nati,
and [obj] he-goat [the] sin: sin offering to seek to seek Moses and behold to burn and be angry upon Eleazar and upon Ithamar son: child Aaron [the] to remain to/for to say
17 “Chifukwa chiyani simunadyere pamalo wopatulika nsembe yopepesera machimo ija? Kodi imene ija siyopatulika? Kodi Yehova sanapereke nyamayo kwa inu kuti muchotse machimo a mpingo wonse powachitira mwambo wa nsembe yopepesera machimo pamaso pa Yehova?
why? not to eat [obj] [the] sin: sin offering in/on/with place [the] holiness for holiness holiness he/she/it and [obj] her to give: give to/for you to/for to lift: guilt [obj] iniquity: crime [the] congregation to/for to atone upon them to/for face: before LORD
18 Pakuti magazi ake sanalowe nawo ku Malo Wopatulika, mukanadya nyama ya mbuziyo pa malo wopatulikawo monga Yehova analamulira.”
look! not to come (in): bring [obj] blood her to(wards) [the] holiness within to eat to eat [obj] her in/on/with holiness like/as as which to command
19 Aaroni anamuyankha Mose kuti, “Lero anthu apereka nsembe yawo yopepesera machimo ndiponso nsembe yawo yopsereza pamaso pa Yehova komabe zinthu zoterezi zandichitikira. Kodi Yehova akanakondwa ndikanadya nsembe yopepesera machimo lero?”
and to speak: speak Aaron to(wards) Moses look! [the] day to present: bring [obj] sin their and [obj] burnt offering their to/for face: before LORD and to encounter: chanced [obj] me like/as these and to eat sin: sin offering [the] day be good in/on/with eye: appearance LORD
20 Pamene Mose anamva zimenezi, anakhutira.
and to hear: hear Moses and be good in/on/with eye: appearance his

< Levitiko 10 >