< Levitiko 10 >

1 Ana a Aaroni, Nadabu ndi Abihu, aliyense anatenga chofukizira lubani chake nayikamo makala a moto ndi kuthiramo lubani. Iwo anapereka pamaso pa Yehova moto wachilendo, moto umene Yehova sanawalamule.
And the sons of Aaron, Nadab and Abihu, each take his censer, and put fire in them, and put incense on it, and bring strange fire near before YHWH, which He has not commanded them;
2 Choncho moto unatuluka pamaso pa Yehova ndi kuwapsereza, ndipo anafa pamaso pa Yehova.
and fire goes out from before YHWH and consumes them, and they die before YHWH.
3 Pamenepo Mose anawuza Aaroni kuti, “Pajatu Yehova ananena kuti, “‘Kwa iwo amene amandiyandikira ndidzaonetsa ulemerero wanga; pamaso pa anthu onse ndidzalemekezedwa.’” Aaroni anakhala chete wosayankhula.
And Moses says to Aaron, “It [is] that which YHWH has spoken, saying, By those drawing near to Me I am sanctified, and in the face of all the people I am honored”; and Aaron is silent.
4 Mose anayitana Misaeli ndi Elizafani, ana a Uzieli, abambo angʼono a Aaroni, ndipo anawawuza kuti, “Bwerani kuno mudzachotse abale anuwa pa malo wopatulika ndi kuwatulutsira kunja kwa msasa.”
And Moses calls to Mishael and to Elzaphan, sons of Uzziel, uncle of Aaron, and says to them, “Come near, carry your brothers from the front of the holy place to the outside of the camp”;
5 Choncho anabwera atavala minjiro yawo ndipo anawatenga ndi kuwatulutsa kunja kwa msasawo monga momwe Mose analamulira.
and they come near, and carry them in their coats to the outside of the camp, as Moses has spoken.
6 Ndipo Mose anawuza Aaroni ndi ana ake Eliezara ndi Itamara kuti, “Musalileke tsitsi lanu nyankhalala ndipo musangʼambe zovala zanu kuti mungafe, ndi mkwiyo wa Yehova ungagwere anthu onsewa. Koma abale anu okha, kutanthauza fuko lonse la Israeli ndiwo ayenera kulira omwalira aja amene Yehova wawapsereza ndi moto.
And Moses says to Aaron and his sons, to Eleazar and to Ithamar, “You do not uncover your heads, and you do not tear your garments, that you do not die, and He is angry on all the congregation; as for your brothers, the whole house of Israel, they lament the burning which YHWH has kindled;
7 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano, mungafe, chifukwa munadzozedwa ndi mafuta a Yehova kukhala ansembe.” Choncho iwo anachita monga Mose ananenera.
and you do not go out from the opening of the Tent of Meeting, lest you die, for the anointing oil of YHWH [is] on you”; and they do according to the word of Moses.
8 Pambuyo pake Yehova anayankhula ndi Aaroni nati,
And YHWH speaks to Aaron, saying,
9 “Iwe ndi ana ako musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa pamene mukulowa mu tenti ya msonkhano kuti mungafe. Ili ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse.
“You do not drink wine and strong drink, you and your sons with you, in your going into the Tent of Meeting, and you do not die—a continuous statute throughout your generations,
10 Muzisiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, pakati pa zinthu zodetsedwa ndi zinthu zoyeretsedwa,
so as to make a separation between the holy and the common, and between the unclean and the pure;
11 ndipo muyenera kuphunzitsa Aisraeli onse malamulo amene Yehova wakupatsani kudzera mwa Mose.”
and to teach the sons of Israel all the statutes which YHWH has spoken to them by the hand of Moses.”
12 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake otsalawo, Eliezara ndi Itamara kuti, “Tengani zopereka zachakudya zopanda yisiti zimene zatsala pa nsembe zopsereza za kwa Yehova ndipo muzidye pafupi ndi guwa pakuti ndi zopatulika kwambiri.
And Moses speaks to Aaron and his sons, to Eleazar and to Ithamar, who are left, “Take the present that is left from the fire-offerings of YHWH, and eat it unleavened near the altar, for it [is] most holy,
13 Muzidye pa malo wopatulika chifukwa zimenezi ndi gawo lako ndi la ana ako pa zopereka zopsereza kwa Yehova. Izitu ndi zimene Yehova anandilamulira.
and you have eaten it in the holy place, for it [is] your portion, and the portion of your sons, from the fire-offerings of YHWH; for so I have been commanded.
14 Koma iwe pamodzi ndi ana ako aamuna ndi aakazi muzidya chidale chimene chinaweyulidwa ndi ntchafu zimene zinaperekedwa nsembe. Muzidye pamalo woyeretsedwa. Zimenezi zaperekedwa kwa iwe ndi ana ako monga gawo lanu pa zopereka zachiyanjano zimene apereka Aisraeli.
And you eat the breast of the wave-offering and the leg of the raised-offering in a clean place, you, and your sons, and your daughters with you; they have been given for your portion and the portion of your sons, out of the sacrifices of peace-offerings of the sons of Israel;
15 Ntchafu imene inaperekedwayo ndi chidale chomwe chinaweyulidwacho abwere nazo pamodzi ndi nsembe ya mafuta ya Yehova yotentha pa moto, ndipo uziweyule kuti zikhale zopereka zoweyula pamaso pa Yehova. Zimenezi zizikhala zako ndi ana ako nthawi zonse monga walamulira Yehova.”
the leg of the raised-offering, and breast of the wave-offering, besides fire-offerings of the fat, they bring in to wave [as] a wave-offering before YHWH, and it has been to you, and to your sons with you, by a continuous statute, as YHWH has commanded.”
16 Pambuyo pake Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yopepesera machimo koma anapeza kuti anayitentha kale. Apa Mose anakalipira Eliezara ndi Itamara, ana a Aaroni otsala aja nati,
And Moses has diligently sought the goat of the sin-offering, and behold, it is burned, and he is angry against Eleazar and against Ithamar, sons of Aaron, who are left, saying,
17 “Chifukwa chiyani simunadyere pamalo wopatulika nsembe yopepesera machimo ija? Kodi imene ija siyopatulika? Kodi Yehova sanapereke nyamayo kwa inu kuti muchotse machimo a mpingo wonse powachitira mwambo wa nsembe yopepesera machimo pamaso pa Yehova?
“Why have you not eaten the sin-offering in the holy place, for it [is] most holy—and He has given it to you to take away the iniquity of the congregation, to make atonement for them before YHWH?
18 Pakuti magazi ake sanalowe nawo ku Malo Wopatulika, mukanadya nyama ya mbuziyo pa malo wopatulikawo monga Yehova analamulira.”
Behold, its blood has not been brought into the holy place within; eating you eat it in the holy place, as I have commanded.”
19 Aaroni anamuyankha Mose kuti, “Lero anthu apereka nsembe yawo yopepesera machimo ndiponso nsembe yawo yopsereza pamaso pa Yehova komabe zinthu zoterezi zandichitikira. Kodi Yehova akanakondwa ndikanadya nsembe yopepesera machimo lero?”
And Aaron speaks to Moses, “Behold, today they have brought their sin-offering and their burnt-offering near before YHWH; and [things] like these meet me, yet I have eaten a sin-offering today; is it good in the eyes of YHWH?”
20 Pamene Mose anamva zimenezi, anakhutira.
And Moses listens, and it is good in his eyes.

< Levitiko 10 >