< Levitiko 10 >

1 Ana a Aaroni, Nadabu ndi Abihu, aliyense anatenga chofukizira lubani chake nayikamo makala a moto ndi kuthiramo lubani. Iwo anapereka pamaso pa Yehova moto wachilendo, moto umene Yehova sanawalamule.
Men Arons Sønner Nadab og Abihu tog hver sin Pande, kom Ild i dem og lagde Røgelse derpaa og frembar for HERRENS Aasyn fremmed Ild, som han ikke havde paalagt dem.
2 Choncho moto unatuluka pamaso pa Yehova ndi kuwapsereza, ndipo anafa pamaso pa Yehova.
Da for Ild ud fra HERRENS Aasyn og fortærede dem, saa de døde for HERRENS Aasyn.
3 Pamenepo Mose anawuza Aaroni kuti, “Pajatu Yehova ananena kuti, “‘Kwa iwo amene amandiyandikira ndidzaonetsa ulemerero wanga; pamaso pa anthu onse ndidzalemekezedwa.’” Aaroni anakhala chete wosayankhula.
Moses sagde da til Aron: »Det er det, HERREN talede om, da han sagde: Jeg viser min Hellighed paa dem, der staar mig nær, og min Herlighed for alt Folkets Øjne!« Og Aron tav.
4 Mose anayitana Misaeli ndi Elizafani, ana a Uzieli, abambo angʼono a Aaroni, ndipo anawawuza kuti, “Bwerani kuno mudzachotse abale anuwa pa malo wopatulika ndi kuwatulutsira kunja kwa msasa.”
Da kaldte Moses Misjael og Elzafan, Arons Farbroder, Uzziels Sønner, til sig og sagde til dem: »Kom og bær eders Frænder bort fra Helligdommen uden for Lejren!«
5 Choncho anabwera atavala minjiro yawo ndipo anawatenga ndi kuwatulutsa kunja kwa msasawo monga momwe Mose analamulira.
Og de kom og bar dem uden for Lejren i deres Kjortler, som Moses havde sagt.
6 Ndipo Mose anawuza Aaroni ndi ana ake Eliezara ndi Itamara kuti, “Musalileke tsitsi lanu nyankhalala ndipo musangʼambe zovala zanu kuti mungafe, ndi mkwiyo wa Yehova ungagwere anthu onsewa. Koma abale anu okha, kutanthauza fuko lonse la Israeli ndiwo ayenera kulira omwalira aja amene Yehova wawapsereza ndi moto.
Men Moses sagde til Aron og hans Sønner Eleazar og Itamar: »I maa hverken lade eders Haar vokse frit eller sønderrive eders Klæder, ellers skal I dø og Vrede komme over hele Menigheden; lad eders Brødre, hele Israels Hus, begræde den Brand, HERREN har antændt;
7 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano, mungafe, chifukwa munadzozedwa ndi mafuta a Yehova kukhala ansembe.” Choncho iwo anachita monga Mose ananenera.
og vig ikke fra Aabenbaringsteltets Indgang, ellers skal I dø, thi HERRENS Salveolie er paa eder!« Og de gjorde som Moses sagde.
8 Pambuyo pake Yehova anayankhula ndi Aaroni nati,
Og HERREN talede til Aron og sagde:
9 “Iwe ndi ana ako musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa pamene mukulowa mu tenti ya msonkhano kuti mungafe. Ili ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse.
Vin og stærk Drik maa hverken du eller dine Sønner drikke, naar I gaaet ind i Aabenbaringsteltet, for at I ikke skal dø. Det skal være eder en evig gyldig Anordning fra Slægt til Slægt,
10 Muzisiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, pakati pa zinthu zodetsedwa ndi zinthu zoyeretsedwa,
for at I kan gøre Skel mellem det hellige og det, der ikke er helligt, og mellem det urene og det rene,
11 ndipo muyenera kuphunzitsa Aisraeli onse malamulo amene Yehova wakupatsani kudzera mwa Mose.”
og for at I kan vejlede Israeliterne i alle de Love, HERREN har kundgjort dem ved Moses.
12 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake otsalawo, Eliezara ndi Itamara kuti, “Tengani zopereka zachakudya zopanda yisiti zimene zatsala pa nsembe zopsereza za kwa Yehova ndipo muzidye pafupi ndi guwa pakuti ndi zopatulika kwambiri.
Og Moses sagde til Aron og hans tilbageblevne Sønner Eleazar og Itamar: »Tag Afgrødeofferet, der er levnet fra HERRENS Ildoffer, og spis det usyret ved Siden af Alteret, thi det er højhelligt;
13 Muzidye pa malo wopatulika chifukwa zimenezi ndi gawo lako ndi la ana ako pa zopereka zopsereza kwa Yehova. Izitu ndi zimene Yehova anandilamulira.
I skal spise det paa et helligt Sted; det er jo din og dine Sønners retmæssige Del af HERRENS Ildofre; thi saaledes er det mig paabudt.
14 Koma iwe pamodzi ndi ana ako aamuna ndi aakazi muzidya chidale chimene chinaweyulidwa ndi ntchafu zimene zinaperekedwa nsembe. Muzidye pamalo woyeretsedwa. Zimenezi zaperekedwa kwa iwe ndi ana ako monga gawo lanu pa zopereka zachiyanjano zimene apereka Aisraeli.
Og Svingningsbrystet og Offerydelseskøllen skal I spise paa et rent Sted, du, dine Sønner og Døtre, thi de er givet dig tillige med dine Sønner som en retmæssig Del af Israeliternes Takofre;
15 Ntchafu imene inaperekedwayo ndi chidale chomwe chinaweyulidwacho abwere nazo pamodzi ndi nsembe ya mafuta ya Yehova yotentha pa moto, ndipo uziweyule kuti zikhale zopereka zoweyula pamaso pa Yehova. Zimenezi zizikhala zako ndi ana ako nthawi zonse monga walamulira Yehova.”
Offerydelseskøllen og Svingningsbrystet skal man frembære sammen med de til Ildofre bestemte Fedtdele, for at Svingningen kan udføres for HERRENS Aasyn, og de skal tilfalde dig og dine Sønner tillige med dig som en evig gyldig Rettighed, saaledes som HERREN har paabudt!«
16 Pambuyo pake Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yopepesera machimo koma anapeza kuti anayitentha kale. Apa Mose anakalipira Eliezara ndi Itamara, ana a Aaroni otsala aja nati,
Og Moses spurgte efter Syndofferbukken, men se, den var opbrændt. Da blev han fortørnet paa Eleazar og Itamar, Arons tilbageblevne Sønner, og sagde:
17 “Chifukwa chiyani simunadyere pamalo wopatulika nsembe yopepesera machimo ija? Kodi imene ija siyopatulika? Kodi Yehova sanapereke nyamayo kwa inu kuti muchotse machimo a mpingo wonse powachitira mwambo wa nsembe yopepesera machimo pamaso pa Yehova?
»Hvorfor har I ikke spist Syndofferet paa det hellige Sted? Det er jo dog højhelligt, og han har givet eder det, for at I skal borttage Menighedens Skyld og saaledes skaffe dem Soning for HERRENS Aasyn.
18 Pakuti magazi ake sanalowe nawo ku Malo Wopatulika, mukanadya nyama ya mbuziyo pa malo wopatulikawo monga Yehova analamulira.”
Se, Blodet deraf er ikke blevet bragt ind i Helligdommens Indre, derfor havde det været eders Pligt at spise det paa det hellige Sted, saaledes som jeg har paabudt!«
19 Aaroni anamuyankha Mose kuti, “Lero anthu apereka nsembe yawo yopepesera machimo ndiponso nsembe yawo yopsereza pamaso pa Yehova komabe zinthu zoterezi zandichitikira. Kodi Yehova akanakondwa ndikanadya nsembe yopepesera machimo lero?”
Men Aron svarede Moses: »Se, de har i Dag frembaaret deres Syndoffer og Brændoffer for HERRENS Aasyn, og en saadan Tilskikkelse har ramt mig! Om jeg i Dag havde spist Syndofferkød, vilde HERREN da have billiget det?«
20 Pamene Mose anamva zimenezi, anakhutira.
Da Moses hørte dette, billigede han det.

< Levitiko 10 >