< Levitiko 10 >
1 Ana a Aaroni, Nadabu ndi Abihu, aliyense anatenga chofukizira lubani chake nayikamo makala a moto ndi kuthiramo lubani. Iwo anapereka pamaso pa Yehova moto wachilendo, moto umene Yehova sanawalamule.
Aaron ca rhoi Nadab neh Abihu loh amah amah baelphaih te a loh rhoi tih hmai soah a tloeng rhoi. Te phoeiah bo-ul te a khueh thil rhoi tih hmai hloeh neh BOEIPA mikhmuh ah a khueh rhoi. Te te amih rhoi taengah a uen dae moenih.
2 Choncho moto unatuluka pamaso pa Yehova ndi kuwapsereza, ndipo anafa pamaso pa Yehova.
Te vaengah BOEIPA hmai lamkah hmai ha thoeng tih amih rhoi te a hlawp dongah BOEIPA mikhmuh ah duek rhoi.
3 Pamenepo Mose anawuza Aaroni kuti, “Pajatu Yehova ananena kuti, “‘Kwa iwo amene amandiyandikira ndidzaonetsa ulemerero wanga; pamaso pa anthu onse ndidzalemekezedwa.’” Aaroni anakhala chete wosayankhula.
Te dongah Moses loh Aaron taengah, “BOEIPA loh, 'Kai neh aka yoei taengah ka ciim uh vetih pilnam boeih kah mikhmuh ah ka thangpom uh ni,’ a ti te a thui coeng he,” a ti nah. Te vaengah Aaron khaw kuemsuem sut.
4 Mose anayitana Misaeli ndi Elizafani, ana a Uzieli, abambo angʼono a Aaroni, ndipo anawawuza kuti, “Bwerani kuno mudzachotse abale anuwa pa malo wopatulika ndi kuwatulutsira kunja kwa msasa.”
Te phoeiah Moses loh Aaron kah a napa noe Uzziel ca rhoi Mishael neh Elizaphan te a khue tih, “Halo rhoi lah. Na manuca rhoi he hmuencim hmai lamloh rhaehhmuen vongvoel la kawt uh,” a ti nah.
5 Choncho anabwera atavala minjiro yawo ndipo anawatenga ndi kuwatulutsa kunja kwa msasawo monga momwe Mose analamulira.
Te dongah Moses kah olpaek vanbangla halo uh tih amih rhoi te a angkidung dongah rhaehhmuen vongvoel la a koh uh.
6 Ndipo Mose anawuza Aaroni ndi ana ake Eliezara ndi Itamara kuti, “Musalileke tsitsi lanu nyankhalala ndipo musangʼambe zovala zanu kuti mungafe, ndi mkwiyo wa Yehova ungagwere anthu onsewa. Koma abale anu okha, kutanthauza fuko lonse la Israeli ndiwo ayenera kulira omwalira aja amene Yehova wawapsereza ndi moto.
Te phoeiah Moses loh Aaron, a ca rhoi Eleazar neh Ithamar taengah, “Na lu te lim uh boeh, na himbai khaw phen uh boeh. Te daengah ni a thintoek ah rhaengpuei pum loh na duek uh pawt eh. Tedae Israel imkhui boeih ah BOEIPA loh hmai neh a hoeh na manuca rhoek te tah rhah uh mai saeh.
7 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano, mungafe, chifukwa munadzozedwa ndi mafuta a Yehova kukhala ansembe.” Choncho iwo anachita monga Mose ananenera.
Te dongah tingtunnah dap thohka lamkah moe uh boeh. Na soah BOEIPA kah koelhnah situi dongah na duek uh ve,” a ti nah. Te dongah Moses kah olthui bangla a saii uh.
8 Pambuyo pake Yehova anayankhula ndi Aaroni nati,
BOEIPA loh Aaron te a voek tih,
9 “Iwe ndi ana ako musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa pamene mukulowa mu tenti ya msonkhano kuti mungafe. Ili ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse.
“Namah neh namah taengkah na ca rhoek loh tingtunnah dap khuila na kun uh vaengah misurtui khaw, yu khaw o boeh. Te daengah ni na cadilcahma ham khaw kumhal khosing vanbangla na duek uh pawt eh.
10 Muzisiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, pakati pa zinthu zodetsedwa ndi zinthu zoyeretsedwa,
Cimcaihnah laklo neh rhongingnah laklo ah, rhalawt laklo neh aka cil laklo ah paekboe ham om,” a ti nah.
11 ndipo muyenera kuphunzitsa Aisraeli onse malamulo amene Yehova wakupatsani kudzera mwa Mose.”
Israel ca rhoek thuinuet ham oltlueh cungkuem te khaw BOEIPA loh amih ham Moses kut ah a thui pah.
12 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake otsalawo, Eliezara ndi Itamara kuti, “Tengani zopereka zachakudya zopanda yisiti zimene zatsala pa nsembe zopsereza za kwa Yehova ndipo muzidye pafupi ndi guwa pakuti ndi zopatulika kwambiri.
Te dongah Moses loh Aaron, Eleazar neh Ithamar koca aka sueng rhoek te, “BOEIPA hmaihlutnah dong lamkah khocang aka coih te lo uh. Tedae te tah a cim kah a cim dongah hmueihtuk taengah vaidamding la ca uh.
13 Muzidye pa malo wopatulika chifukwa zimenezi ndi gawo lako ndi la ana ako pa zopereka zopsereza kwa Yehova. Izitu ndi zimene Yehova anandilamulira.
Kai ng'uen van coeng dongah BOEIPA hmaihlutnah khui lamkah khocang te namah kah buhvae neh namah koca rhoek kah buhvae la hmuen cim ah ca uh.
14 Koma iwe pamodzi ndi ana ako aamuna ndi aakazi muzidya chidale chimene chinaweyulidwa ndi ntchafu zimene zinaperekedwa nsembe. Muzidye pamalo woyeretsedwa. Zimenezi zaperekedwa kwa iwe ndi ana ako monga gawo lanu pa zopereka zachiyanjano zimene apereka Aisraeli.
Tedae Israel ca rhoek kah rhoepnah hmueih khuiah thueng hmueih kah a rhang neh khosaa kah a laeng tah namah kah maehvae neh, na ca rhoek kah maehvae coeng ni. Na capa rhoek, na canu rhoek neh namah kah hmuen saelh ah ca uh.
15 Ntchafu imene inaperekedwayo ndi chidale chomwe chinaweyulidwacho abwere nazo pamodzi ndi nsembe ya mafuta ya Yehova yotentha pa moto, ndipo uziweyule kuti zikhale zopereka zoweyula pamaso pa Yehova. Zimenezi zizikhala zako ndi ana ako nthawi zonse monga walamulira Yehova.”
Khosaa kah a laeng neh thueng hmueih kah a rhang khaw maehtha hmaihlutnah khaw BOEIPA mikhmuh kah thueng hmueih la thueng ham khuen uh. BOEIPA kah a uen vanbangla namah ham neh na ca rhoek ham kumhal ah maehvae la om saeh,” a ti nah.
16 Pambuyo pake Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yopepesera machimo koma anapeza kuti anayitentha kale. Apa Mose anakalipira Eliezara ndi Itamara, ana a Aaroni otsala aja nati,
Te phoeiah boirhaem maae te Moses loh a tlap a tlap hatah vawl ana hai pauh. Te dongah Aaron koca rhoek khuiah aka sueng Eleazar neh Ithamar taengah a thintoek tih,
17 “Chifukwa chiyani simunadyere pamalo wopatulika nsembe yopepesera machimo ija? Kodi imene ija siyopatulika? Kodi Yehova sanapereke nyamayo kwa inu kuti muchotse machimo a mpingo wonse powachitira mwambo wa nsembe yopepesera machimo pamaso pa Yehova?
“A cim kah a cim boirhaem he balae tih hmuencim hmuen ah na caak uh pawh He khaw rhaengpuei kathaesainah aka phuei tih BOEIPA mikhmuh ah amih kah tholh aka dawth hamla nangmih taengah m'paek dae.
18 Pakuti magazi ake sanalowe nawo ku Malo Wopatulika, mukanadya nyama ya mbuziyo pa malo wopatulikawo monga Yehova analamulira.”
A thii te hmuencim la a khuen moenih ko he. Kang uen bangla hmuencim ah ca khaw ca uh yap mai saw,” a ti nah.
19 Aaroni anamuyankha Mose kuti, “Lero anthu apereka nsembe yawo yopepesera machimo ndiponso nsembe yawo yopsereza pamaso pa Yehova komabe zinthu zoterezi zandichitikira. Kodi Yehova akanakondwa ndikanadya nsembe yopepesera machimo lero?”
Te vaengah Aaron loh Moses taengah, “Tihnin ah a boirhaem neh hmueihhlutnah te khaw BOEIPA mikhmuh ah a nawn uh coeng dae tahae kah bangla kai taengah thoeng coeng he. Tihnin ah boirhaem he ka ca koinih BOEIPA mikhmuh ah then aya?,” a ti nah.
20 Pamene Mose anamva zimenezi, anakhutira.
Tedae Moses loh a yaak vaengah a mikhmuh ah a thuem sak.