< Levitiko 1 >

1 Yehova anayitana Mose mu tenti ya msonkhano. Iye anati,
And the Lord called unto Moses, and spoke unto him out of the tabernacle of the congregation, saying,
2 “Aliyense wa inu ngati abwera ndi nsembe kwa Yehova kuchokera pa ziweto zake, choperekacho chikhale ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi.
Speak unto the children of Israel, and say unto them, If any one of you wish to bring an offering unto the Lord: of the cattle, either of the herds, or of the flocks, shall ye bring your offering.
3 “‘Ngati munthu apereka nsembe yopsereza ya ngʼombe, ikhale yayimuna yopanda chilema. Aziyipereka pa khomo la tenti ya msonkhano, kuti Yehova alandire.
If his offering be a burnt-sacrifice of the herds, then shall he offer a male without blemish: unto the door of the tabernacle of the congregation shall he bring it, that it may be favorably received for him before the Lord.
4 Munthuyo asanjike dzanja lake pa mutu pa nsembe yopserezayo, ndipo idzalandiridwa kuti ikhale yopepesera machimo ake.
And he shall lay his hand upon the head of the burnt-offering; and it shall be accepted for him to make atonement for him.
5 Pambuyo pake aphe ngʼombeyo pamaso pa Yehova, ndipo ansembe, ana a Aaroni, atenge magazi ake ndi kuwawaza mbali zonse za guwa lansembe limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
And he shall kill the young steer before the Lord: and the sons of Aaron the priests shall bring near the blood, and they shall sprinkle the blood round about upon the altar that is by the door of the tabernacle of the congregation.
6 Munthuyo asende nsembe yopserezayo ndi kuyidula nthulinthuli.
And he shall flay the burnt-offering, and cut it into its pieces.
7 Ndipo ana a Aaroni, wansembe uja asonkhe moto pa guwa ndi kuyalapo nkhuni pa motopo.
And the sons of Aaron the priest shall put fire upon the altar, and lay the wood in order upon the fire;
8 Kenaka ana a Aaroni, wansembe uja, ayike nthuli za nyamayo, mutu wake pamodzi ndi mafuta omwe pa nkhuni zimene zili paguwapo.
And the sons of Aaron the priests shall lay in order the parts, the head, and the fat, upon the wood that is on the fire which is upon the altar;
9 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe awotche nyama yonse paguwapo. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chowotcha pa moto, cha fungo lokomera Yehova.
But its inwards and its legs shall he wash in water; and the priest shall burn the whole on the altar, as a burnt-sacrifice, an offering made by fire, of a sweet savor unto the Lord.
10 “‘Koma ngati chopereka cha nsembe yopserezayo ndi nkhosa kapena mbuzi kuchokera pa ziweto zake, munthuyo apereke yayimuna yopanda chilema.
And if his offering be of the flocks, of the sheep, or of the goats, for a burnt-sacrifice: then shall he offer a male without blemish as the same.
11 Ayiphere kumpoto kwa guwa, pamaso pa Yehova, ndipo ana a Aaroni amene ndi ansembe, awaze magazi ake mbali zonse za guwalo.
And he shall kill it on the side of the altar, northward, before the Lord; and the sons of Aaron the priests shall sprinkle its blood upon the altar round about.
12 Kenaka ayidule nyamayo nthulinthuli, ndipo wansembe ayike nthulizo pa guwa, atengenso mutu ndi mafuta omwe, ndipo ayike zonsezi pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa.
And he shall cut it into its pieces, with its head and its fat; and the priest shall lay them in order on the wood that is on the fire which is upon the altar;
13 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe abwere nazo zonse ndi kuzitentha pa guwa. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chotentha pa moto, fungo lokomera Yehova.
But the inwards and the legs shall he wash with water; and the priest shall bring near the whole, and burn it upon the altar; it is a burnt-sacrifice, an offering made by fire, of a sweet savor unto the Lord.
14 “‘Koma ngati chopereka kwa Yehova ndi nsembe yopsereza ya mbalame, ndiye ikhale njiwa kapena mawunda.
And if of fowls be the burnt-sacrifice for his offering to the Lord: then shall he bring his offering of turtle-doves, or of young pigeons.
15 Wansembe abwere nayo ku guwa, ayidule mutu moyipotola ndi kutentha mutuwo pa guwa. Magazi ake awathire pansi kuti ayenderere pambali pa guwa.
And the priest shall bring it near unto the altar, and pinch off its head, and burn it on the altar; and the blood thereof shall be wrung out on the wall of the altar.
16 Iye achotse chithokomiro pamodzi ndi nthenga zake zomwe ndi kuzitaya ku malo wotayirako phulusa, kummawa kwa guwalo.
And he shall remove its crop with its feathers, and cast it beside the altar on the east part, at the place of the ashes.
17 Kenaka ayingʼambe pakati, koma asachotse mapiko. Ndipo wansembe ayiwotche pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa. Imeneyi ndi nsembe yopsereza, yowotcha pa moto ndiponso ya fungo lokomera Yehova.
And he shall cleave it by its wings, but shall not divide it asunder; and the priest shall burn it upon the altar, upon the wood that is on the fire: it is a burnt-sacrifice, an offering made by fire, of a sweet savor unto the Lord.

< Levitiko 1 >