< Levitiko 1 >

1 Yehova anayitana Mose mu tenti ya msonkhano. Iye anati,
And the Lord called Moses again and spoke to him out of the tabernacle of witness, saying, Speak to the children of Israel, and you shall say to them,
2 “Aliyense wa inu ngati abwera ndi nsembe kwa Yehova kuchokera pa ziweto zake, choperekacho chikhale ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi.
If [any] man of you shall bring gifts to the Lord, you shall bring your gifts of the cattle and of the oxen and of the sheep.
3 “‘Ngati munthu apereka nsembe yopsereza ya ngʼombe, ikhale yayimuna yopanda chilema. Aziyipereka pa khomo la tenti ya msonkhano, kuti Yehova alandire.
If his gift be a whole burnt offering, he shall bring an unblemished male of the herd to the door of the tabernacle of witness, he shall bring it as acceptable before the Lord.
4 Munthuyo asanjike dzanja lake pa mutu pa nsembe yopserezayo, ndipo idzalandiridwa kuti ikhale yopepesera machimo ake.
And he shall lay his hand on the head of the burnt offering as a thing acceptable for him, to make atonement for him.
5 Pambuyo pake aphe ngʼombeyo pamaso pa Yehova, ndipo ansembe, ana a Aaroni, atenge magazi ake ndi kuwawaza mbali zonse za guwa lansembe limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
And they shall kill the calf before the Lord; and the sons of Aaron the priests shall bring the blood, and they shall pour the blood round about on the altar, which [is] at the doors of the tabernacle of witness.
6 Munthuyo asende nsembe yopserezayo ndi kuyidula nthulinthuli.
And having flayed the whole burnt offering, they shall divide it by its limbs.
7 Ndipo ana a Aaroni, wansembe uja asonkhe moto pa guwa ndi kuyalapo nkhuni pa motopo.
And the sons of Aaron the priests shall put fire on the altar, and shall pile wood on the fire.
8 Kenaka ana a Aaroni, wansembe uja, ayike nthuli za nyamayo, mutu wake pamodzi ndi mafuta omwe pa nkhuni zimene zili paguwapo.
And the sons of Aaron the priests shall pile up the divided parts, and the head, and the fat on the wood on the fire, [the wood] which is on the altar.
9 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe awotche nyama yonse paguwapo. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chowotcha pa moto, cha fungo lokomera Yehova.
And the entrails and the feet they shall wash in water, and the priests shall put all on the altar: it is a burnt offering, a sacrifice, a smell of sweet savor to the Lord.
10 “‘Koma ngati chopereka cha nsembe yopserezayo ndi nkhosa kapena mbuzi kuchokera pa ziweto zake, munthuyo apereke yayimuna yopanda chilema.
And if his gift [be] of the sheep to the Lord, or of the lambs, or of the kids for whole burnt offerings, he shall bring it a male without blemish.
11 Ayiphere kumpoto kwa guwa, pamaso pa Yehova, ndipo ana a Aaroni amene ndi ansembe, awaze magazi ake mbali zonse za guwalo.
And he shall lay his hand on its head; and they shall kill it by the side of the altar, toward the north before the Lord, and the sons of Aaron the priests shall pour its blood on the altar round about.
12 Kenaka ayidule nyamayo nthulinthuli, ndipo wansembe ayike nthulizo pa guwa, atengenso mutu ndi mafuta omwe, ndipo ayike zonsezi pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa.
And they shall divide it by its limbs, and its head and its fat, and the priests shall pile them up on the wood which is on the fire, on the altar.
13 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe abwere nazo zonse ndi kuzitentha pa guwa. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chotentha pa moto, fungo lokomera Yehova.
And they shall wash the entrails and the feet with water, and the priest shall bring all the [parts] and put them on the altar: it is a burnt offering, a sacrifice, a smell of sweet savor to the Lord.
14 “‘Koma ngati chopereka kwa Yehova ndi nsembe yopsereza ya mbalame, ndiye ikhale njiwa kapena mawunda.
And if he bring his gift, a burnt offering to the Lord, of birds, then shall he bring his gift of doves or pigeons.
15 Wansembe abwere nayo ku guwa, ayidule mutu moyipotola ndi kutentha mutuwo pa guwa. Magazi ake awathire pansi kuti ayenderere pambali pa guwa.
And the priest shall bring it to the altar, and shall wring off its head; and the priest shall put it on the altar, and shall wring out the blood at the bottom of the altar.
16 Iye achotse chithokomiro pamodzi ndi nthenga zake zomwe ndi kuzitaya ku malo wotayirako phulusa, kummawa kwa guwalo.
And he shall take away the crop with the feathers, and shall cast it forth by the altar toward the east to the place of the ashes.
17 Kenaka ayingʼambe pakati, koma asachotse mapiko. Ndipo wansembe ayiwotche pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa. Imeneyi ndi nsembe yopsereza, yowotcha pa moto ndiponso ya fungo lokomera Yehova.
And he shall break it off from the wings and shall not separate it, and the priest shall put it on the altar on the wood which is on the fire: it is a burnt offering, a sacrifice, a sweet smelling savor to the Lord.

< Levitiko 1 >