< Levitiko 1 >

1 Yehova anayitana Mose mu tenti ya msonkhano. Iye anati,
And Jehovah called to Moses and spoke to him out of the tent of meeting, saying,
2 “Aliyense wa inu ngati abwera ndi nsembe kwa Yehova kuchokera pa ziweto zake, choperekacho chikhale ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi.
Speak unto the children of Israel and say unto them, When any man of you presenteth an offering to Jehovah, ye shall present your offering of the cattle, of the herd and of the flock.
3 “‘Ngati munthu apereka nsembe yopsereza ya ngʼombe, ikhale yayimuna yopanda chilema. Aziyipereka pa khomo la tenti ya msonkhano, kuti Yehova alandire.
If his offering be a burnt-offering of the herd, he shall present it a male without blemish: at the entrance of the tent of meeting shall he present it, for his acceptance before Jehovah.
4 Munthuyo asanjike dzanja lake pa mutu pa nsembe yopserezayo, ndipo idzalandiridwa kuti ikhale yopepesera machimo ake.
And he shall lay his hand on the head of the burnt-offering; and it shall be accepted for him to make atonement for him.
5 Pambuyo pake aphe ngʼombeyo pamaso pa Yehova, ndipo ansembe, ana a Aaroni, atenge magazi ake ndi kuwawaza mbali zonse za guwa lansembe limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
And he shall slaughter the bullock before Jehovah; and Aaron's sons, the priests, shall present the blood and sprinkle the blood round about on the altar that is at the entrance of the tent of meeting.
6 Munthuyo asende nsembe yopserezayo ndi kuyidula nthulinthuli.
And he shall flay the burnt-offering, and cut it up into its pieces.
7 Ndipo ana a Aaroni, wansembe uja asonkhe moto pa guwa ndi kuyalapo nkhuni pa motopo.
And the sons of Aaron the priest shall put fire on the altar, and lay wood in order on the fire;
8 Kenaka ana a Aaroni, wansembe uja, ayike nthuli za nyamayo, mutu wake pamodzi ndi mafuta omwe pa nkhuni zimene zili paguwapo.
and Aaron's sons, the priests, shall lay the pieces, the head, and the fat, in order on the wood that is on the fire which is on the altar;
9 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe awotche nyama yonse paguwapo. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chowotcha pa moto, cha fungo lokomera Yehova.
but its inwards and its legs shall he wash in water; and the priest shall burn all on the altar, a burnt-offering, an offering by fire to Jehovah of a sweet odour.
10 “‘Koma ngati chopereka cha nsembe yopserezayo ndi nkhosa kapena mbuzi kuchokera pa ziweto zake, munthuyo apereke yayimuna yopanda chilema.
And if his offering be of the flock, of the sheep or of the goats, for a burnt-offering, he shall present it a male without blemish.
11 Ayiphere kumpoto kwa guwa, pamaso pa Yehova, ndipo ana a Aaroni amene ndi ansembe, awaze magazi ake mbali zonse za guwalo.
And he shall slaughter it on the side of the altar northward before Jehovah; and Aaron's sons, the priests, shall sprinkle its blood on the altar round about.
12 Kenaka ayidule nyamayo nthulinthuli, ndipo wansembe ayike nthulizo pa guwa, atengenso mutu ndi mafuta omwe, ndipo ayike zonsezi pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa.
And he shall cut it into its pieces, and its head, and its fat; and the priest shall lay them in order on the wood that is on the fire which is on the altar;
13 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe abwere nazo zonse ndi kuzitentha pa guwa. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chotentha pa moto, fungo lokomera Yehova.
but the inwards and the legs shall he wash with water; and the priest shall present [it] all, and burn [it] on the altar: it is a burnt-offering, an offering by fire to Jehovah of a sweet odour.
14 “‘Koma ngati chopereka kwa Yehova ndi nsembe yopsereza ya mbalame, ndiye ikhale njiwa kapena mawunda.
And if his offering to Jehovah be a burnt-offering of fowls, then he shall present his offering of turtle-doves, or of young pigeons.
15 Wansembe abwere nayo ku guwa, ayidule mutu moyipotola ndi kutentha mutuwo pa guwa. Magazi ake awathire pansi kuti ayenderere pambali pa guwa.
And the priest shall bring it near to the altar and pinch off its head and burn it on the altar; and its blood shall be pressed out at the side of the altar.
16 Iye achotse chithokomiro pamodzi ndi nthenga zake zomwe ndi kuzitaya ku malo wotayirako phulusa, kummawa kwa guwalo.
And he shall remove its crop with its feathers, and cast it beside the altar on the east, into the place of the ashes;
17 Kenaka ayingʼambe pakati, koma asachotse mapiko. Ndipo wansembe ayiwotche pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa. Imeneyi ndi nsembe yopsereza, yowotcha pa moto ndiponso ya fungo lokomera Yehova.
and he shall split it open at its wings, [but] shall not divide [it] asunder; and the priest shall burn it on the altar on the wood that is on the fire: it is a burnt-offering, an offering by fire to Jehovah of a sweet odour.

< Levitiko 1 >