< Levitiko 1 >

1 Yehova anayitana Mose mu tenti ya msonkhano. Iye anati,
Then the Lord called Moses and spoke to him from the tabernacle of the testimony, saying:
2 “Aliyense wa inu ngati abwera ndi nsembe kwa Yehova kuchokera pa ziweto zake, choperekacho chikhale ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi.
Speak to the sons of Israel, and you shall say to them: The man among you who will offer to the Lord a sacrifice from the cattle, that is, an offering of victims of oxen or sheep:
3 “‘Ngati munthu apereka nsembe yopsereza ya ngʼombe, ikhale yayimuna yopanda chilema. Aziyipereka pa khomo la tenti ya msonkhano, kuti Yehova alandire.
if his offering will be a holocaust, as well as from the herd, he shall offer an immaculate male at the door of the tabernacle of the testimony, to make himself pleasing to the Lord.
4 Munthuyo asanjike dzanja lake pa mutu pa nsembe yopserezayo, ndipo idzalandiridwa kuti ikhale yopepesera machimo ake.
And he shall place his hand on the head of the sacrifice, and so it shall be acceptable and effective, in its expiation.
5 Pambuyo pake aphe ngʼombeyo pamaso pa Yehova, ndipo ansembe, ana a Aaroni, atenge magazi ake ndi kuwawaza mbali zonse za guwa lansembe limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
And he shall immolate the calf in the sight of the Lord. And the priests, the sons of Aaron, shall offer its blood, pouring it all around the altar, which is before the door of the tabernacle.
6 Munthuyo asende nsembe yopserezayo ndi kuyidula nthulinthuli.
And having pulled away the skin of the victim, they shall cut up the joints into pieces,
7 Ndipo ana a Aaroni, wansembe uja asonkhe moto pa guwa ndi kuyalapo nkhuni pa motopo.
and they shall toss fire under the altar, having arranged beforehand a stack of wood.
8 Kenaka ana a Aaroni, wansembe uja, ayike nthuli za nyamayo, mutu wake pamodzi ndi mafuta omwe pa nkhuni zimene zili paguwapo.
And they shall lay the parts which are cut up in order upon it: namely, the head, and all the things that adjoin to the liver,
9 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe awotche nyama yonse paguwapo. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chowotcha pa moto, cha fungo lokomera Yehova.
the intestines and feet having been washed with water. And the priest shall burn them on the altar as a holocaust and as a sweet odor to the Lord.
10 “‘Koma ngati chopereka cha nsembe yopserezayo ndi nkhosa kapena mbuzi kuchokera pa ziweto zake, munthuyo apereke yayimuna yopanda chilema.
But if the offering is from the flocks, a holocaust either of sheep or goats, he shall offer a male without blemish.
11 Ayiphere kumpoto kwa guwa, pamaso pa Yehova, ndipo ana a Aaroni amene ndi ansembe, awaze magazi ake mbali zonse za guwalo.
And he shall immolate it at the side of the altar which looks out toward the north, in the sight of the Lord. Yet truly, the sons of Aaron shall pour its blood upon the altar all around.
12 Kenaka ayidule nyamayo nthulinthuli, ndipo wansembe ayike nthulizo pa guwa, atengenso mutu ndi mafuta omwe, ndipo ayike zonsezi pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa.
And they shall divide the limbs, the head, and everything that adjoins to the liver. And they shall place them on the wood, under which the fire is to be thrown.
13 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe abwere nazo zonse ndi kuzitentha pa guwa. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chotentha pa moto, fungo lokomera Yehova.
Yet truly, the intestines and the feet they shall wash with water. And the priest, having offered everything, shall burn it upon the altar as a holocaust and as a most sweet odor to the Lord.
14 “‘Koma ngati chopereka kwa Yehova ndi nsembe yopsereza ya mbalame, ndiye ikhale njiwa kapena mawunda.
But if the oblation of a holocaust to the Lord is of birds, either of turtledoves, or young pigeons,
15 Wansembe abwere nayo ku guwa, ayidule mutu moyipotola ndi kutentha mutuwo pa guwa. Magazi ake awathire pansi kuti ayenderere pambali pa guwa.
the priest shall offer it at the altar: and twisting back the neck with the head, and also rupturing the place of the wound, he shall make the blood run down over the edge of the altar.
16 Iye achotse chithokomiro pamodzi ndi nthenga zake zomwe ndi kuzitaya ku malo wotayirako phulusa, kummawa kwa guwalo.
Yet truly, the craw of the throat and the feathers he shall cast near the altar at the eastern section, in the place where the ashes are usually poured out.
17 Kenaka ayingʼambe pakati, koma asachotse mapiko. Ndipo wansembe ayiwotche pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa. Imeneyi ndi nsembe yopsereza, yowotcha pa moto ndiponso ya fungo lokomera Yehova.
And he shall break its wing joints, but he shall neither cut, nor divide it with metal, and he shall burn it upon the altar, placing fire under the wood. It is a holocaust and an oblation of a most sweet odor to the Lord.

< Levitiko 1 >