< Maliro 1 >

1 Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha, umene kale unali wodzaza ndi anthu! Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu! Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye. Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi, tsopano wasanduka kapolo.
Hvorledes sidder hun saa enlig, den Stad, som havde meget Folk, den er bleven som en Enke! den, som var saa stor iblandt Hedningerne, en Fyrstinde iblandt Landskaberne, er bleven skatskyldig.
2 Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse, misozi ili pa masaya pake. Mwa abwenzi ake onse, palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza. Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu; onse akhala adani ake.
Hun græder svart om Natten, og hendes Taarer løbe over hendes Kinder; der er ingen, som trøster hende af alle dem, som elskede hende, alle hendes Venner ere troløse imod hende, de ere blevne hendes Fjender.
3 Yuda watengedwa ku ukapolo, kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa. Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina; ndipo alibe malo opumulira. Onse omuthamangitsa iye amupitirira, ndipo alibe kwina kothawira.
Juda er vandret ud for Elendigheds og for svar Trældoms Skyld; hun bor iblandt Hedningerne, hun finder ikke Ro; alle hendes Forfølgere naa hende midt i Trængslerne.
4 Misewu yopita ku Ziyoni ikulira, chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake. Zipata zake zonse zili pululu, ansembe akubuwula. Anamwali ake akulira, ndipo ali mʼmasautso woopsa.
Zions Veje sørge, fordi ingen kommer til Festforsamling, alle dens Porte ere øde, dens Præster sukke, dens Jomfruer ere bedrøvede, og for deri selv er det bittert.
5 Adani ake asanduka mabwana ake; odana naye akupeza bwino. Yehova wamubweretsera mavuto chifukwa cha machimo ake ambiri. Ana ake atengedwa ukapolo pamaso pa mdani.
Hendes Modstandere ere voksede hende over Hovedet, hendes Fjender ere trygge; thi Herren har bedrøvet hende for hendes mange Overtrædelsers Skyld; hendes spæde Børn ere dragne i Fangenskab for Modstanderens Ansigt.
6 Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni wachokeratu. Akalonga ake ali ngati mbawala zosowa msipu; alibe mphamvu zothawira owathamangitsa.
Og fra Zions Datter er al hendes Prydelse gaaet bort; hendes Fyrster ere blevne ligesom Hjorte, der ikke finde Føde, og de gik kraftesløse for Forfølgerens Ansigt.
7 Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake, Yerusalemu amakumbukira chuma chonse chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake. Anthu ake atagwidwa ndi adani ake, panalibe aliyense womuthandiza. Adani ake ankamuyangʼana ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.
Jerusalem ihukommer i sin Elendigheds og sin Landflygtigheds Dage alle sine Herligheder, som den havde i gamle Dage, idet dens Folk nu er faldet i Fjendens Haand, og der er ingen, som hjælper den; Fjenderne saa den, de spottede over, at den ikke er mere;
8 Yerusalemu wachimwa kwambiri ndipo potero wakhala wodetsedwa. Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza, chifukwa aona umaliseche wake. Iye mwini akubuwula ndipo akubisa nkhope yake.
Jerusalem har syndet svarlig, derfor er den bleven til Væmmelse; alle, som ærede den, ringeagte den, thi de saa dens Nøgenhed; selv sukker den og vender sig bort.
9 Uve wake umaonekera pa zovala zake; iye sanaganizire za tsogolo lake. Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu; ndipo analibe womutonthoza. “Inu Yehova, taonani masautso anga, pakuti mdani wapambana.”
Hendes Slæb er besmittet, hun tænkte ikke paa sin Fremtid, og hun er nedstyrtet paa vidunderlig Maade, der er ingen, som trøster hende. Herre! se min Elendighed, thi Fjenden har gjort sig stor.
10 Adani amulanda chuma chake chonse; iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika, amene Inu Mulungu munawaletsa kulowa mu msonkhano wanu.
Fjender udstrakte deres Haand efter alle hendes Herligheder; thi hun saa, at Hedninger kom ind i hendes Helligdom, om hvilke du havde befalet, at de ikke skulde komme i din Menighed.
11 Anthu ake onse akubuwula pamene akufunafuna chakudya; asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya kuti akhale ndi moyo. “Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani, chifukwa ine ndanyozeka.”
Hele hendes Folk sukker og søger efter Brød, de give deres Herligheder hen for Mad til at vederkvæge deres Sjæl; se, Herre! og sku, at jeg er bleven ringe.
12 “Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa? Yangʼanani ndipo muone. Kodi pali mavuto ofanana ndi amene andigwerawa, amene Ambuye anandibweretsera pa tsiku la ukali wake?
Det rører ikke eder, alle I, som gaa forbi ad Vejen. Skuer og ser, om der er en Smerte som min Smerte, der mig er vederfaren; thi Herren har bedrøvet mig paa sin brændende Vredes Dag.
13 “Anatumiza moto kuchokera kumwamba, unalowa mpaka mʼmafupa anga. Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga ndipo anandibweza. Anandisiya wopanda chilichonse, wolefuka tsiku lonse.
Han sendte en Ild fra det høje i mine Ben, og den herskede der; han udspændte et Garn for mine Fødder, kastede mig tilbage, han gjorde mig øde og svag den ganske Dag.
14 “Wazindikira machimo anga onse ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi. Machimowa afika pakhosi panga, ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu. Iye wandipereka kwa anthu amene sindingalimbane nawo.
Mine Overtrædelsers Aag er knyttet ved hans Haand, de sammenslynge sig, de ere gaaede op over min Hals, han lod min Kraft bukke under; Herren har givet mig i deres Hænder, for hvilke jeg ikke kan rejse mig.
15 “Ambuye wakana anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane: wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane, kuti litekedze anyamata anga; mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza anamwali a Yuda.
Herren forkastede alle mine vældige i min Midte, han sammenkaldte en Forsamling imod mig til at knuse mit unge Mandskab; Herren traadte Vinpersen for Jomfruen, Judas Datter.
16 “Chifukwa cha zimenezi ndikulira ndipo maso anga adzaza ndi misozi. Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze, palibe aliyense wondilimbitsa mtima. Ana anga ali okhaokha chifukwa mdani watigonjetsa.
Over disse Ting græder jeg, mit Øje, mit Øje strømmer med Vand; thi Trøsteren, som skulde, vederkvæge nyn Sjæl, er langt fra mig; mine Børn ere ødelagte, thi Fjenden fik Overhaand.
17 “Ziyoni wakweza manja ake, koma palibe aliyense womutonthoza. Yehova walamula kuti abale ake a Yakobo akhale adani ake; Yerusalemu wasanduka chinthu chodetsedwa pakati pawo.
Zion udstrækker sine Hænder, der er ingen, som trøster hende; Herren har givet Befaling imod Jakob til hans Fjender trindt omkring ham; Jerusalem er bleven til Væmmelse imellem dem.
18 “Yehova ndi wolungama, koma ndine ndinawukira malamulo ake. Imvani inu anthu a mitundu yonse; onani masautso anga. Anyamata ndi anamwali anga agwidwa ukapolo.
Herren, han er retfærdig; thi jeg var genstridig imod hans Mund; hører dog, alle Folk! og ser min Smerte, mine Jomfruer og mine unge Karle ere vandrede i Fangenskab.
19 “Ndinayitana abwenzi anga koma anandinyenga. Ansembe ndi akuluakulu anga anafa mu mzinda pamene ankafunafuna chakudya kuti akhale ndi moyo.
Jeg raabte paa mine Elskere, de bedroge mig; mine Præster og mine Ældste opgave Aanden i Staden; thi de søgte sig Brød, at de kunde vederkvæge deres Sjæl.
20 “Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira! Ndikuzunzika mʼkati mwanga, ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa chifukwa ndakhala osamvera. Mʼmisewu anthu akuphedwa, ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.
Se til, Herre! thi jeg har Angest, mine Indvolde ere oprørte, mit Hjerte har vendt sig inden i mig; thi jeg har været meget genstridig; udenfor har Sværdet gjort mig barnløs, i Huset har det været ret som Døden.
21 “Anthu amva kubuwula kwanga, koma palibe wonditonthoza. Adani anga onse amva masautso anga; iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita. Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija kuti iwonso adzakhale ngati ine.
De hørte, at jeg sukkede, jeg havde dog ingen Trøster; alle mine Fjender hørte min Ulykke, de glædede sig; thi du har gjort det; men du lader en Dag komme, som du kalder frem, da skulle de være ligesom jeg.
22 “Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu; muwalange ngati mmene mwandilangira ine chifukwa cha machimo anga onse. Ndikubuwula kwambiri ndipo mtima wanga walefuka.”
Lad al deres Ondskab komme for dit Ansigt, og handl med dem, som du handlede med mig for alle mine Overtrædelsers Skyld; thi mine Sukke ere mange, og mit Hjerte er afmægtigt.

< Maliro 1 >