< Maliro 1 >

1 Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha, umene kale unali wodzaza ndi anthu! Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu! Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye. Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi, tsopano wasanduka kapolo.
Balae tih pilnam aka ping khopuei te amah bueng kho a sak. Namtom taengah a cungkuem te nuhmai bangla om tih, paeng taengkah boeinu saldong la poeh.
2 Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse, misozi ili pa masaya pake. Mwa abwenzi ake onse, palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza. Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu; onse akhala adani ake.
Khoyin ah rhap, rhap tih a mikphi loh a kam dongla long. Anih aka lungnah boeih khuiah khaw anih ham aka hloep om pawh. A hui boeih te anih taengah hnukpoh uh tih, anih ham thunkha la om uh.
3 Yuda watengedwa ku ukapolo, kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa. Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina; ndipo alibe malo opumulira. Onse omuthamangitsa iye amupitirira, ndipo alibe kwina kothawira.
Judah te phacipphabaem neh thohtatnah cungkuem lamloh a poelyoe uh. Anih te namtom taengah om tih ngolbuel pataeng a dang moenih. Anih aka hloem boeih loh anih te longcaek ah a kae uh.
4 Misewu yopita ku Ziyoni ikulira, chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake. Zipata zake zonse zili pululu, ansembe akubuwula. Anamwali ake akulira, ndipo ali mʼmasautso woopsa.
Rhahdoe cangpoem ah khaw Zion longpuei kah khoning ah ha pawk uh pawh. A vongka khaw boeih pong coeng. A khosoih khaw huei uh coeng. A oila rhoek khaw pae uh tih amah te phaep uh.
5 Adani ake asanduka mabwana ake; odana naye akupeza bwino. Yehova wamubweretsera mavuto chifukwa cha machimo ake ambiri. Ana ake atengedwa ukapolo pamaso pa mdani.
A rhal te a lu la a om pah tih a thunkha khaw dingsuek uh. A boekoek a yet dongah BOEIPA loh a pae sak tih a ca rhoek te a rhal hmai ah tamna la cet uh.
6 Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni wachokeratu. Akalonga ake ali ngati mbawala zosowa msipu; alibe mphamvu zothawira owathamangitsa.
A tanu khui lamloh Zion nu tah a rhuepomnah cungkuem khaw a coe pah coeng. A mangpa rhoek te rhangrhaeh bangla om uh tih luemnah hmu uh pawh. Te dongah aka hloem kah mikhmuh ah thadueng om kolla yong uh.
7 Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake, Yerusalemu amakumbukira chuma chonse chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake. Anthu ake atagwidwa ndi adani ake, panalibe aliyense womuthandiza. Adani ake ankamuyangʼana ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.
Jerusalem loh a phacipphabaem neh a airhoeng hnin ah tah hlamat kum kah khuehtawn cungkuem neh a om uh te a poek. A pilnam loh rhal kut dongah cungku tih anih te aka bom om pawh. Rhal loh anih a hmuh vaengah a rhawpnah te a nueih thiluh.
8 Yerusalemu wachimwa kwambiri ndipo potero wakhala wodetsedwa. Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza, chifukwa aona umaliseche wake. Iye mwini akubuwula ndipo akubisa nkhope yake.
Jerusalem a tholh te tholhnah coeng ni. Te dongah anih a thangpom khaw longhnawt la boeih poeh coeng. Anih kah a yah aka hmuh ham khaw haam uh. Amah khaw huei tih a hnuk la mael.
9 Uve wake umaonekera pa zovala zake; iye sanaganizire za tsogolo lake. Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu; ndipo analibe womutonthoza. “Inu Yehova, taonani masautso anga, pakuti mdani wapambana.”
A hnihmoi kah a tihnai neh a hmailong khaw poek pawh. Anih aka hloep a om van pawt ah khobaerhambae la suntla uh. BOEIPA aw kai kah phacipphabaem dongah thunkha rhoek a pantai khaw hmuh lah saw.
10 Adani amulanda chuma chake chonse; iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika, amene Inu Mulungu munawaletsa kulowa mu msonkhano wanu.
A ngailaemnah cungkuem soah rhal loh a kut a duen. Namah kah hlangping taengah kun pawt ham na uen lalah a rhokso ah namtom a kun te a hmuh.
11 Anthu ake onse akubuwula pamene akufunafuna chakudya; asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya kuti akhale ndi moyo. “Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani, chifukwa ine ndanyozeka.”
A pilnam te boeih huei uh. Buh a tlap uh tih a khuehtawn a paek uh. A hinglu hlawt ham ni a ngailaemnah khaw caak la a thung. BOEIPA so lamtah a hnom ham ka om he paelki lah.
12 “Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa? Yangʼanani ndipo muone. Kodi pali mavuto ofanana ndi amene andigwerawa, amene Ambuye anandibweretsera pa tsiku la ukali wake?
Longpuei kah aka khum boeih ke paelki uh lamtah so uh lah, kai kah nganboh bangla nganboh aka khueh nangmih ah a om moenih. Te te a thintoek thinsa hnin ah BOEIPA loh kai soah a poelyoe tih m'pae sak.
13 “Anatumiza moto kuchokera kumwamba, unalowa mpaka mʼmafupa anga. Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga ndipo anandibweza. Anandisiya wopanda chilichonse, wolefuka tsiku lonse.
Hmuensang lamkah ka rhuh khuilah hmai han tueih. Ka kho ham lawk a tung tih a man sak dongah kai he a hnuk la m'mael sak. Hnin at puet ah kai he pumthim hainak neh aka pong la n'khueh.
14 “Wazindikira machimo anga onse ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi. Machimowa afika pakhosi panga, ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu. Iye wandipereka kwa anthu amene sindingalimbane nawo.
Ka boekoek hnamkun te a kut neh a hlin tih ka rhawn dongla a pawk vaengah rhap a cuet. Ka thadueng a tangdawt sak tih kai aka thoh thai pawt kah kut dongah Boeipa loh kai n'khueh.
15 “Ambuye wakana anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane: wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane, kuti litekedze anyamata anga; mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza anamwali a Yuda.
Ka boei cungkuem khaw ka kotak ah tah Boeipa loh a suntlae coeng. Ka tongpang rhoek neet ham kai he tingtunnah ng'hueh thil. Judah nu oila te ka Boeipa loh misur rhom ah a nook.
16 “Chifukwa cha zimenezi ndikulira ndipo maso anga adzaza ndi misozi. Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze, palibe aliyense wondilimbitsa mtima. Ana anga ali okhaokha chifukwa mdani watigonjetsa.
Te dongah kai kamah mik khaw rhap tih ka mik lamkah tui a suntla. Kai aka hloep tih hinglu aka mael sak khaw kai lamloh lakhla coeng. Ka ca rhoek aka om khaw thunkha loh a et tih pong uh.
17 “Ziyoni wakweza manja ake, koma palibe aliyense womutonthoza. Yehova walamula kuti abale ake a Yakobo akhale adani ake; Yerusalemu wasanduka chinthu chodetsedwa pakati pawo.
Zion loh a kut te a phuel dae anih te hloep pawh. A kaepvai kah a rhal te BOEIPA loh Jakob ham a uen coeng dongah Jerusalem khaw amih lakli ah pumom la poeh.
18 “Yehova ndi wolungama, koma ndine ndinawukira malamulo ake. Imvani inu anthu a mitundu yonse; onani masautso anga. Anyamata ndi anamwali anga agwidwa ukapolo.
BOEIPA amah tah dueng dae a ol te ka koek oeh. Pilnam aw, pilnam boeih aw hnatun uh laeh. Ka oila neh ka tongpang rhoek loh tamna la a caeh kah ka nganboh he hmu uh lah.
19 “Ndinayitana abwenzi anga koma anandinyenga. Ansembe ndi akuluakulu anga anafa mu mzinda pamene ankafunafuna chakudya kuti akhale ndi moyo.
Amih te ka lungnah la ka khue dae kai m'phok uh. Khopuei kah ka khosoih rhoek neh patong rhoek loh amamih caak a tlap uh pangthuem ah pal uh tih a hinglu te a mael puei uh.
20 “Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira! Ndikuzunzika mʼkati mwanga, ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa chifukwa ndakhala osamvera. Mʼmisewu anthu akuphedwa, ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.
BOEIPA aw kai taengkah puencak he hmu lah. Ka ko tah noong tih ka khui ah ka lungbuei a maelh. A koek khaw ka koek oeh coeng dongah imkhui kah dueknah bangla kawtpoeng ah cunghang loh a cakol sak.
21 “Anthu amva kubuwula kwanga, koma palibe wonditonthoza. Adani anga onse amva masautso anga; iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita. Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija kuti iwonso adzakhale ngati ine.
Ka huei te a yaak uh dae kai he n'hloep moenih. Ka thunkha boeih loh ka yoethae he a yaak uh vaengah ngaingaih uh. Namah ham na saii tih na khue khohnin na pha vaengah kai bangla om uh bitni.
22 “Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu; muwalange ngati mmene mwandilangira ine chifukwa cha machimo anga onse. Ndikubuwula kwambiri ndipo mtima wanga walefuka.”
Amih kah boethae cungkuem te na mikhmuh ah phoe saeh. Kai taengah na poelyoe bangla amih te poelyoe van. Ka boekoek cungkuem dongah ka hueinah khaw yet tih ka lungbuei hal coeng.

< Maliro 1 >