< Maliro 5 >

1 Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
Kumbuka, Ee Bwana, yaliyotupata, tazama, nawe uione aibu yetu.
2 Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
Urithi wetu umegeuziwa kwa wageni, na nyumba zetu kwa wageni.
3 Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
Tumekuwa yatima wasio na baba, mama zetu wamekuwa kama wajane.
4 Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
Ni lazima tununue maji tunayokunywa, kuni zetu zapatikana tu kwa kununua.
5 Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
Wanaotufuatilia wapo kwenye visigino vyetu, tumechoka na hakuna pumziko.
6 Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
Tumejitolea kwa Misri na Ashuru tupate chakula cha kutosha.
7 Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
Baba zetu walitenda dhambi na hawapo tena, na sisi tunachukua adhabu yao.
8 Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
Watumwa wanatutawala na hakuna wa kutuokoa mikononi yao.
9 Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
Tunapata chakula chetu kwa kuhatarisha maisha yetu kwa sababu ya upanga jangwani.
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
Ngozi yetu ina joto kama tanuru, kwa sababu ya fadhaa itokanayo na njaa.
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
Wanawake wametendwa jeuri katika Sayuni, na mabikira katika miji ya Yuda.
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
Wakuu wametungikwa juu kwa mikono yao, wazee hawapewi heshima.
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
Vijana wanataabika kwenye mawe ya kusagia, wavulana wanayumbayumba chini ya mizigo ya kuni.
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
Wazee wameondoka langoni la mji, vijana wameacha kuimba nyimbo zao.
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
Furaha imeondoka mioyoni mwetu, kucheza kwetu kumegeuka maombolezo.
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
Taji imeanguka kutoka kichwani petu. Ole wetu, kwa maana tumetenda dhambi!
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
Kwa sababu hiyo, mioyo yetu inazimia, kwa sababu ya hayo, macho yetu yamefifia,
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
kwa ajili ya Mlima Sayuni, ambao unakaa ukiwa, nao mbweha wanatembea juu yake.
19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
Wewe, Ee Bwana unatawala milele, kiti chako cha enzi chadumu kizazi hadi kizazi.
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
Kwa nini watusahau siku zote? Kwa nini umetuacha kwa muda mrefu?
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
Turudishe kwako mwenyewe, Ee Bwana, ili tupate kurudi. Zifanye mpya siku zetu kama siku za kale,
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.
isipokuwa uwe umetukataa kabisa na umetukasirikia pasipo kipimo.

< Maliro 5 >