< Maliro 5 >

1 Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
Acuérdate, o! Jehová, de lo que nos ha venido: vé, y mira nuestra vergüenza.
2 Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
Nuestra heredad se ha vuelto a extraños, nuestras casas a forasteros.
3 Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
Huérfanos somos sin padre: nuestras madres como viudas.
4 Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
Nuestra agua bebemos por dinero, nuestra leña compramos por precio.
5 Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
Sobre nuestra cerviz padecemos persecución; cansámosnos, y no hay para nosotros descanso.
6 Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
A Egipto dimos la mano, y al Asirio, para hartarnos de pan.
7 Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
Nuestros padres pecaron, y son muertos; y nosotros llevamos sus castigos.
8 Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
Siervos se enseñorearon de nosotros: no hubo quien nos librase de su mano.
9 Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
Con el peligro de nuestras vidas traíamos nuestro pan delante de la espada del desierto.
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
Nuestros cueros se ennegrecieron como un horno a causa del ardor de la hambre.
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
Afligieron a las mujeres en Sión, a las vírgenes en las ciudades de Judá.
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
A los príncipes colgaron con su mano: no reverenciaron los rostros de los viejos.
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
Llevaron los mozos a moler, y los muchachos desfallecieron en la leña.
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
Los ancianos cesaron de la puerta, los mancebos de sus canciones.
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
Cesó el gozo de nuestro corazón, nuestro corro se tornó en luto.
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
Cayó la corona de nuestra cabeza: ¡ay ahora de nosotros! porque pecamos.
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
Por esto fue entristecido nuestro corazón, por esto se entenebrecieron nuestros ojos.
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
Por el monte de Sión que es asolado, zorras andan en él.
19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
Mas tú, Jehová, para siempre permanecerás: tu trono de generación en generación.
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
¿Por qué te olvidarás para siempre de nosotros? ¿dejarnos has por luengos días?
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
Vuélvenos, o! Jehová, a ti, y volvernos hemos: renueva nuestros días como al principio.
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.
Porque desechando nos has desechado: háste airado contra nosotros en gran manera.

< Maliro 5 >