< Maliro 5 >

1 Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
ای یهوه آنچه بر ما واقع شد به یاد آور وملاحظه فرموده، عار ما را ببین.۱
2 Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
میراث ما از آن غریبان و خانه های ما از آن اجنبیان گردیده است.۲
3 Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
ما یتیم و بی‌پدر شده‌ایم و مادران ما مثل بیوه‌ها گردیده‌اند.۳
4 Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
آب خود را به نقره می‌نوشیم و هیزم ما به مافروخته می‌شود.۴
5 Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
تعاقب کنندگان ما به گردن ما رسیده‌اند وخسته شده، راحت نداریم.۵
6 Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
با اهل مصر و آشور دست دادیم تا از نان سیرشویم.۶
7 Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
پدران ما گناه ورزیده، نابود شده‌اند و مامتحمل عصیان ایشان گردیده‌ایم.۷
8 Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
غلامان بر ما حکمرانی می‌کنند و کسی نیست که از دست ایشان رهایی دهد.۸
9 Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
از ترس شمشیر اهل بیابان، نان خود را بخطرجان خویش می‌یابیم.۹
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
پوست ما به‌سبب سموم قحط مثل تنورسوخته شده است.۱۰
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
زنان را در صهیون بی‌عصمت کردند ودوشیزگان را در شهرهای یهودا.۱۱
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
سروران از دست ایشان به دار کشیده شده و به مشایخ اعتنا ننمودند.۱۲
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
جوانان سنگهای آسیا را برمی دارند وکودکان زیر بار هیزم می‌افتند.۱۳
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
مشایخ از دروازه‌ها نابود شدند و جوانان ازنغمه سرایی خویش.۱۴
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
شادی دل ما نیست شد و رقص ما به ماتم مبدل گردید.۱۵
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
تاج از سر ما افتاد، وای بر ما زیرا که گناه کردیم.۱۶
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
از این جهت دل ما بیتاب شده است و به‌سبب این چیزها چشمان ما تار گردیده است.۱۷
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
یعنی به‌خاطر کوه صهیون که ویران شد وروباهان در آن گردش می‌کنند.۱۸
19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
اما تو‌ای یهوه تا ابدالاباد جلوس می‌فرمایی و کرسی تو تا جمیع دهرها خواهدبود.۱۹
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
پس برای چه ما را تا به ابد فراموش کرده وما را مدت مدیدی ترک نموده‌ای.۲۰
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
‌ای یهوه ما را بسوی خود برگردان وبازگشت خواهیم کرد و ایام ما را مثل زمان سلف تازه کن.۲۱
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.
و الا ما را بالکل رد نموده‌ای و بر مابی نهایت غضبناک شده‌ای.۲۲

< Maliro 5 >