< Maliro 5 >

1 Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
Recordare Domine quid acciderit nobis: intuere, et respice opprobrium nostrum.
2 Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
Hereditas nostra versa est ad alienos: domus nostrae ad extraneos.
3 Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
Pupilli facti sumus absque patre, matres nostrae quasi viduae.
4 Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
Aquam nostram pecunia bibimus: ligna nostra pretio comparavimus.
5 Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
Cervicibus nostris minabamur, lassis non dabatur requies.
6 Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
Aegypto dedimus manum, et Assyriis ut saturaremur pane.
7 Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
Patres nostri peccaverunt, et non sunt: et nos iniquitates eorum portavimus.
8 Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
Servi dominati sunt nostri: non fuit qui redimeret de manu eorum.
9 Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
In animabus nostris afferebamus panem nobis, a facie gladii in deserto.
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
Pellis nostra, quasi clibanus exusta est a facie tempestatum famis.
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
Mulieres in Sion humiliaverunt, et virgines in civitatibus Iuda.
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
Principes manu suspensi sunt: facies senum non erubuerunt.
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
Adolescentibus impudice abusi sunt: et pueri in ligno corruerunt.
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
Senes defecerunt de portis: iuvenes de choro psallentium.
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
Defecit gaudium cordis nostri: versus est in luctum chorus noster.
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
Cecidit corona capitis nostri: vae nobis, quia peccavimus.
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
Propterea moestum factum est cor nostrum, ideo contenebrati sunt oculi nostri.
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
Propter montem Sion quia disperiit, vulpes ambulaverunt in eo.
19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
Tu autem Domine in aeternum permanebis, solium tuum in generatione et generationem.
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
Quare in perpetuum oblivisceris nostri? derelinques nos in longitudine dierum?
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
Converte nos Domine ad te, et convertemur: innova dies nostros, sicut a principio.
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.
Sed proiiciens repulisti nos, iratus es contra nos vehementer.

< Maliro 5 >