< Maliro 5 >
1 Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
RICORDATI, Signore, di quello che ci è avvenuto; Riguarda, e vedi li nostro vituperio.
2 Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
La nostra eredità [è] stata trasportata agli stranieri, [E] le nostre case a' forestieri.
3 Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
Noi siam divenuti orfani, senza padre; [E] le nostre madri come donne vedove.
4 Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
Noi abbiam bevuta la nostra acqua per danari, Le nostre legne ci sono state vendute a prezzo.
5 Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
Noi abbiam sofferta persecuzione sopra il nostro collo; Noi ci siamo affannati, e non abbiamo avuto alcun riposo.
6 Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
Noi abbiam porta la mano agli Egizi, [Ed] agli Assiri, per saziarci di pane.
7 Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
I nostri padri hanno peccato, e non sono [più]; Noi abbiam portate le loro iniquità.
8 Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
De' servi ci hanno signoreggiati; Non [vi è stato] alcuno che [ci] abbia riscossi di man loro.
9 Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
Noi abbiamo addotta la nostra vittuaglia A rischio della nostra vita, per la spada del deserto.
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
La nostra pelle è divenuta bruna come un forno, Per l'arsure della fame.
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
Le donne sono state sforzate in Sion, E le vergini nelle città di Giuda.
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
I principi sono stati impiccati per man di coloro; Non si è avuta riverenza alle facce de' vecchi.
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
I giovani hanno portata la macinatura, E i fanciulli son caduti per le legne.
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
I vecchi hanno abbandonato le porte, E i giovani i loro suoni.
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
La gioia del nostro cuore è cessata, I nostri balli sono stati cangiati in duolo.
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
La corona del nostro capo è caduta; Guai ora a noi! perciocchè abbiam peccato.
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
Per questo il cuor nostro è languido; Per queste cose gli occhi nostri sono scurati.
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
Egli è perchè il monte di Sion è deserto, [Sì che] le volpi vi passeggiano.
19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
Tu, Signore, dimori in eterno; Il tuo trono [è stabile] per ogni età.
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
Perchè ci dimenticheresti in perpetuo? [Perchè] ci abbandoneresti per lungo tempo?
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
O Signore, convertici a te, e noi sarem convertiti: Rinnova i nostri giorni, come [erano] anticamente.
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.
Perciocchè, ci hai tu del tutto riprovati? Sei tu adirato contro a noi fino all'estremo?