< Maliro 5 >

1 Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
Gedenke, HERR, was uns widerfahren ist! Schau her und siehe unsere Schmach!
2 Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
Unser Erbe ist den Fremden zugefallen, unsere Häuser den Ausländern.
3 Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
Wir sind Waisen geworden, vaterlos, unsere Mütter zu Witwen.
4 Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
Unser Wasser trinken wir um Geld, unser Holz kommt uns gegen Bezahlung zu.
5 Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
Unsere Verfolger sind uns beständig auf dem Hals; werden wir müde, so gönnt man uns keine Ruhe.
6 Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
Wir haben Ägypten die Hand gereicht und Assur, um genug Brot zu erhalten.
7 Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
Unsere Väter, die gesündigt haben, sind nicht mehr; wir müssen ihre Schuld tragen.
8 Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
Knechte herrschen über uns; niemand befreit uns aus ihrer Hand!
9 Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
Wir schaffen unsere Nahrung unter Lebensgefahr herbei, weil uns in der Wüste das Schwert bedroht.
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
Unsere Haut ist schwarz wie ein Ofen, so versengt uns der Hunger.
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
Frauen wurden in Zion vergewaltigt, Jungfrauen in den Städten Judas.
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
Fürsten wurden durch ihre Hand gehängt, die Person der Alten hat man nicht geachtet.
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
Jünglinge müssen Mühlsteine tragen und Knaben straucheln unter Bürden von Holz.
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
Die Ältesten bleiben weg vom Tor, und die Jünglinge lassen ihr Saitenspiel.
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
Die Freude unsres Herzens ist dahin, unser Reigen hat sich in Klage verwandelt.
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
Die Krone ist uns vom Haupte gefallen; wehe uns, daß wir gesündigt haben!
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
Darob ist unser Herz krank geworden, darum sind unsere Augen trübe:
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
weil der Berg Zion verwüstet ist; Füchse tummeln sich daselbst.
19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
Du aber, o HERR, bleibst ewiglich, dein Thron besteht für und für!
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
Warum willst du uns für immer vergessen, uns verlassen auf Lebenszeit?
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
Bringe uns zu dir zurück, o HERR, so kehren wir um; laß es wieder werden wie vor alters!
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.
Oder hast du uns gänzlich verworfen, bist du allzusehr über uns erzürnt?

< Maliro 5 >