< Maliro 5 >
1 Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
Gedenke [Das fünfte Lied besteht aus zweizeiligen Strophen, welche bloß ihrer Zahl nach den Buchstaben des Alphabets entsprechen, ] Jehova, dessen, was uns geschehen! schaue her und sieh unsere Schmach!
2 Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
Unser Erbteil ist Fremden zugefallen, unsere Häuser Ausländern.
3 Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
Wir sind Waisen, ohne Vater; unsere Mütter sind wie Witwen.
4 Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
Unser Wasser trinken wir um Geld, unser Holz bekommen wir gegen Zahlung.
5 Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
Unsere Verfolger sind uns auf dem Nacken; wir ermatten, man läßt uns keine Ruhe.
6 Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
Ägypten reichen wir die Hand [d. h. unterwerfen wir uns, ] und Assyrien, um mit Brot gesättigt zu werden.
7 Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
Unsere Väter haben gesündigt, sie sind nicht mehr; wir, wir tragen ihre Missetaten.
8 Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
Knechte herrschen über uns; da ist niemand, der uns aus ihrer Hand reiße.
9 Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
Wir holen unser Brot mit Gefahr unseres Lebens, wegen des Schwertes der Wüste.
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
Vor den Gluten des Hungers brennt unsere Haut wie ein Ofen.
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
Sie haben Weiber geschwächt in Zion, Jungfrauen in den Städten Judas.
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
Fürsten sind durch ihre Hand aufgehängt, das Angesicht der Alten wird nicht geehrt.
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
Jünglinge tragen die Handmühle, und Knaben straucheln unter dem Holze.
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
Die Alten bleiben fern [Eig. feiern] vom Tore, die Jünglinge von ihrem Saitenspiel.
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
Die Freude unseres Herzens hat aufgehört, in Trauer ist unser Reigen verwandelt.
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
Gefallen ist die Krone unseres Hauptes. Wehe uns! denn wir haben gesündigt.
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
Darum ist unser Herz siech geworden, um dieser Dinge willen sind unsere Augen verdunkelt:
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
Wegen des Berges Zion, der verwüstet ist; Füchse streifen auf ihm umher.
19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
Du, Jehova, thronst in Ewigkeit; dein Thron ist von Geschlecht zu Geschlecht.
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
Warum willst du uns für immer vergessen, uns verlassen auf immerdar [W. auf Länge der Tage?]
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
Jehova, bringe uns zu dir zurück, daß wir umkehren; erneuere unsere Tage wie vor alters!
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.
Oder solltest du uns gänzlich verworfen haben, gar zu sehr auf uns zürnen?