< Maliro 5 >

1 Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
Souvenez-vous, Seigneur, de ce qui nous est arrivé; considérez et regardez notre opprobre.
2 Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
Notre héritage est passé à des ennemis, nos maisons à des étrangers.
3 Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
Nous sommes devenus comme des orphelins sans pères, et nos mères comme des veuves.
4 Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
Nous avons bu notre eau à prix d’argent, nous avons acheté chèrement notre bois.
5 Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
Nous étions conduits par des chaînes attachées à nos cous, à ceux qui étaient fatigués on ne donnait pas de repos.
6 Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
Nous avons donné la main à l’Egypte et aux Assyriens, afin de nous rassasier de pain.
7 Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
Nos pères ont péché, et ils ne sont plus; et nous, nous avons porté leurs iniquités.
8 Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
Des esclaves nous ont dominés; il n’y a eu personne qui nous arrachât de leur main.
9 Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
Au péril de nos âmes, nous allions nous chercher du pain à la face du glaive du désert.
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
Notre peau, comme un four, a été brûlée par les ardeurs de la faim.
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
Ils ont humilié des femmes dans Sion, et des vierges dans les cités de Juda,
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
Des princes ont été pendus par la main; on n’a pas révéré la face des vieillards.
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
Ils ont indignement abusé des jeunes hommes; et des enfants ont succombé sous le bois.
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
Des vieillards ont abandonné les portes, et de jeunes hommes, le chœur des joueurs de psaltérion.
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
La joie de notre âme a fait défaut; notre chœur a été changé en deuil.
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
Elle est tombée, la couronne de notre tête; malheur à nous, parce que nous avons péché!
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
À cause de cela, notre cœur est devenu triste; pour cela, nos yeux se sont couverts de ténèbres.
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
À cause de la montagne de Sion, qui a été détruite, les renards s’y sont promenés.
19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
Mais vous, Seigneur, vous demeurerez éternellement; votre trône subsistera dans toutes les générations.
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
Pourquoi nous oublierez-vous à jamais? Pourquoi nous abandonnerez-vous dans la longueur des jours?
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
Convertissez-nous à vous, et nous serons convertis; Seigneur, renouvelez nos jours comme au commencement.
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.
Mais nous rejetant, vous nous avez repoussés; vous êtes extrêmement irrité contre nous.

< Maliro 5 >