< Maliro 5 >
1 Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
Souviens-toi, ô Éternel, de ce qui nous est arrivé! Regarde et vois notre opprobre!
2 Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
Notre héritage a passé à des étrangers, nos maisons à des inconnus.
3 Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
Nous sommes devenus des orphelins sans père, et nos mères sont comme des veuves.
4 Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
Nous buvons notre eau à prix d'argent; c'est contre paiement que nous vient notre bois.
5 Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
Le joug sur le cou, nous souffrons la persécution; nous sommes épuisés, nous n'avons point de repos.
6 Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
Nous avons tendu la main vers l'Égypte et vers l'Assyrie, pour nous rassasier de pain.
7 Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
Nos pères ont péché, ils ne sont plus; et nous, nous portons la peine de leur iniquité.
8 Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
Des esclaves dominent sur nous, et personne ne nous délivre de leurs mains.
9 Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
Nous cherchons notre pain au péril de notre vie, à cause de l'épée du désert.
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
Notre peau est brûlée comme un four, par l'ardeur véhémente de la faim.
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
Ils ont déshonoré les femmes dans Sion, et les vierges dans les villes de Juda.
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
Des chefs ont été pendus par leur main; la personne des anciens n'a point été respectée.
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
Les jeunes gens ont porté la meule, et les enfants ont chancelé sous le bois.
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
Les vieillards ne se trouvent plus aux portes; les jeunes gens ont abandonné leurs lyres.
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
La joie de notre cœur a cessé; nos danses sont changées en deuil.
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
La couronne de notre tête est tombée. Malheur à nous! parce que nous avons péché!
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
C'est pour cela que notre cœur est malade; c'est pour ces choses que nos yeux sont obscurcis;
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
C'est à cause de la montagne de Sion, qui est désolée, tellement que les renards s'y promènent.
19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
Mais toi, Éternel! tu demeures éternellement, et ton trône subsiste d'âge en âge!
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
Pourquoi nous oublierais-tu à jamais, pourquoi nous abandonnerais-tu si longtemps?
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
Convertis-nous à toi, Éternel, et nous serons convertis! Renouvelle nos jours comme ils étaient autrefois!
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.
Nous aurais-tu entièrement rejetés? Serais-tu courroucé contre nous à l'excès?