< Maliro 5 >

1 Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
Remember, O Lord, what has happened to us: behold, and look on our reproach.
2 Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
Our inheritance has been turned away to aliens, our houses to strangers:
3 Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
we are become orphans, we have no father, our mothers are as widows.
4 Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
We have drunk our water for money; our wood is sold to us [for a burden] on our neck:
5 Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
we have been persecuted, we have laboured, we have had no rest.
6 Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
Egypt gave the hand [to us], Assur to their own satisfaction.
7 Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
Our fathers sinned, [and] are not: we have borne their iniquities.
8 Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
Servants have ruled over us: there is none to ransom [us] out of their hand.
9 Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
We shall bring in our bread with [danger of] our lives, because of the sword of the wilderness.
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
Our skin is blackened like an oven; they are convulsed, because of the storms of famine.
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
They humbled the women in Sion, the virgins in the cities of Juda.
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
Princes were hanged up by their hands: the elders were not honored.
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
The chosen men lifted up [the voice in] weeping, and the youths fainted under the wood.
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
And the elders ceased from the gate, the chosen men ceased from their music.
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
The joy of our heart has ceased; our dance is turned into mourning.
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
The crown has fallen [from] our head: yes, woe to us! for we have sinned.
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
For this has grief come; our heart is sorrowful: for this our eyes are darkened.
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
Over the mountain of Sion, because it is made desolate, foxes have walked therein.
19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
But you, O Lord, shall dwell for ever; your throne [shall endure] to generation and generation.
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
Therefore will you utterly forget us, and abandon us a long time?
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
Turn us, O Lord, to you, and we shall be turned; and renew our days as before.
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.
For you have indeed rejected us; you have been very angry against us.

< Maliro 5 >