< Maliro 5 >

1 Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
Rozpomeň se, Hospodine, co se nám děje; popatř a viz pohanění naše.
2 Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
Dědictví naše obráceno jest k cizím, domové naši k cizozemcům.
3 Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
Sirotci jsme a bez otce, matky naše jsou jako vdovy.
4 Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
Vody své za peníze pijeme, dříví naše za záplatu přichází.
5 Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
Na hrdle svém protivenství snášíme, pracujeme, nedopouští se nám odpočinouti.
6 Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
Egyptským podáváme ruky i Assyrským, abychom nasyceni byli chlebem.
7 Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
Otcové naši hřešili, není jich, my pak trestáni po nich neseme.
8 Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
Služebníci panují nad námi; není žádného, kdo by vytrhl z ruky jejich.
9 Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
S opovážením se života svého hledáme chleba svého, pro strach meče i na poušti.
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
Kůže naše jako pec zčernaly od náramného hladu.
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
Ženám na Sionu i pannám v městech Judských násilé činí.
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
Knížata rukou jejich zvěšena jsou, osoby starých nemají v poctivosti.
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
Mládence k žernovu berou, a pacholata pod dřívím klesají.
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
Starci sedati v branách přestali a mládenci od zpěvů svých.
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
Přestala radost srdce našeho, obrátilo se v kvílení plésání naše.
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
Spadla koruna s hlavy naší; běda nám již, že jsme hřešili.
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
Protoť jest mdlé srdce naše, pro tyť věci zatměly se oči naše,
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
Pro horu Sion, že zpuštěna jest; lišky chodí po ní.
19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
Ty Hospodine, na věky zůstáváš, a stolice tvá od národu do pronárodu.
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
Proč se zapomínáš na věky na nás, a opouštíš nás za tak dlouhé časy?
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
Obrať nás, ó Hospodine, k sobě, a obráceni budeme; obnov dny naše, jakž byly za starodávna.
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.
Nebo zdali všelijak zavržeš nás, a hněvati se budeš na nás velice?

< Maliro 5 >