< Maliro 5 >
1 Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
耶和華啊,求你記念我們所遭遇的事, 觀看我們所受的凌辱。
2 Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
我們的產業歸與外邦人; 我們的房屋歸與外路人。
3 Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
我們是無父的孤兒; 我們的母親好像寡婦。
4 Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
我們出錢才得水喝; 我們的柴是人賣給我們的。
5 Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
追趕我們的,到了我們的頸項上; 我們疲乏不得歇息。
6 Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
我們投降埃及人和亞述人, 為要得糧吃飽。
7 Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
我們列祖犯罪,而今不在了; 我們擔當他們的罪孽。
8 Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
奴僕轄制我們, 無人救我們脫離他們的手。
9 Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
因為曠野的刀劍, 我們冒着險才得糧食。
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
因飢餓燥熱, 我們的皮膚就黑如爐。
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
敵人在錫安玷污婦人, 在猶大的城邑玷污處女。
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
他們吊起首領的手, 也不尊敬老人的面。
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
少年人扛磨石, 孩童背木柴,都絆跌了。
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
老年人在城門口斷絕; 少年人不再作樂。
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
我們心中的快樂止息, 跳舞變為悲哀。
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
冠冕從我們的頭上落下; 我們犯罪了,我們有禍了!
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
這些事我們心裏發昏, 我們的眼睛昏花。
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
錫安山荒涼, 野狗行在其上。
19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
耶和華啊,你存到永遠; 你的寶座存到萬代。
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
你為何永遠忘記我們? 為何許久離棄我們?
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
耶和華啊,求你使我們向你回轉, 我們便得回轉。 求你復新我們的日子,像古時一樣。
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.
你竟全然棄絕我們, 向我們大發烈怒?