< Maliro 5 >

1 Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
上主,求你眷念我們的遭遇,垂顧憐視我們受的恥辱。
2 Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
我們的產業,轉入外人手中;我們的房舍,歸屬了異邦人。
3 Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
我們自己變成了無父的孤兒,我們的母親好像寡婦一樣。
4 Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
我們自己的水,必須用錢買來喝;我們自己的木柴,需要用款換來。
5 Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
重軛加在我們的頸項上,受人折磨迫害;我們困憊疲乏,不得安息。
6 Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
我們向埃及伸手,向亞述乞食充餓。
7 Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
我們的祖先犯了罪,已不存在;我們卻要承擔他們的罪債;
8 Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
原是奴隸的人,竟然統治我們,但沒有人解救我們,脫離他們的手。
9 Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
我們面臨曠野刀劍的威脅,該冒性命的危險,纔能得到食糧。
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
我們的皮膚因飢餓而發炎,發熱有如火爐。
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
婦女們在熙雍被人強姦,處女們在猶大遭人奸污。
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
王臣被人縛手吊起,長老的儀容受人凌辱,
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
青年人應該服役推磨,幼童倒在柴捆之下。
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
長老們不再安坐城門口,青年們不再奏樂高歌。
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
我們心中已毫無樂趣,我們的歌舞反而變成悲愁。
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
我們頭上的花冠已經墮地。我們犯罪的人,確是有禍的!
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
我們的心神所以徬徨,我們的眼睛所以模糊;
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
因為熙雍山已經荒蕪,狐狸成群出沒其間。
19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
上主,至於你,你永遠常存,你的寶座萬世不替。
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
為什麼你常忘記我們﹖為什麼你常拋棄我們﹖
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
上主,求你叫我們歸向你,我們必定回心轉意;求你重整我們的時代,如同往昔一樣。
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.
你豈能完全擯棄我們,豈能向我們憤怒到底﹖

< Maliro 5 >