< Maliro 4 >
1 Haa! Golide wathimbirira, golide wosalala wasinthikiratu! Amwazamwaza miyala yokongola ya kumalo opatulika pamphambano ponse pa mzinda.
Altın nasıl donuklaştı, Saf altın nasıl değişti! Kutsal taşlar sokak başlarına dağılmış.
2 Haa! Ana a Ziyoni amtengowapatali amene kale anali ngati golide, tsopano ali ngati miphika ya dothi, ntchito ya owumba mbiya!
Değerleri saf altınla ölçülen Siyon çocukları Nasıl çömlekçi işi, toprak testi yerine sayılır oldu!
3 Ngakhale nkhandwe zimapereka bere kuyamwitsa ana ake, koma anthu anga asanduka ankhanza ngati nthiwatiwa mʼchipululu.
Çakallar bile meme verip yavrularını emzirir, Ama halkım çöldeki devekuşları kadar acımasız oldu.
4 Lilime la mwana lakangamira kukhosi chifukwa cha ludzu, ana akupempha chakudya, koma palibe amene akuwapatsa.
Susuzluktan emzikteki bebeklerin dili damağına yapışıyor, Çocuklar ekmek istiyor, veren yok.
5 Iwo amene kale ankadya zonona akupemphetsa mʼmisewu ya mu mzinda. Iwo amene kale ankavala zokongola tsopano akugona pa phulusa.
Onlar ki, yemeğin en iyisini yerlerdi, Sokaklarda perişan oldular; Onlar ki, al giysiler içinde büyüdüler, Çöp yığınlarını kapışır oldular.
6 Kuyipa kwa anthu anga kunali kwakukulu kuposa anthu a ku Sodomu, amene anawonongedwa mʼkamphindi kochepa popanda owathandiza.
Halkımın suçu el değmeden, bir anda yıkılan Sodom'un günahından daha büyüktür.
7 Akalonga ake anali owala koposa chisanu chowundana ndi oyera kuposa mkaka. Matupi awo anali ofiira kuposa miyala ya rubi, maonekedwe awo ngati miyala ya safiro.
Beyleri kardan temiz, sütten aktılar, Bedence mercandan kızıl, laciverttaşı kadar biçimliydiler.
8 Koma tsopano maonekedwe awo ndi akuda kuposa mwaye; palibe angawazindikire mʼmisewu ya mu mzinda. Khungu lawo lachita makwinyamakwinya pa mafupa awo; lawuma gwaa ngati nkhuni.
Şimdiyse görünüşleri kömürden kara, Sokaklarda tanınmaz oldular. Bir deri bir kemiğe döndüler, odun gibi kurudular.
9 Amene anaphedwa ndi lupanga aliko bwino kuposa amene anafa ndi njala; chifukwa chosowa chakudya cha mʼmunda iwowa ankafowoka ndi njala mpaka kufa.
Kılıçla öldürülenler kıtlıktan ölenlerden mutludur, Çünkü kıtlıktan ölenler tarla ürününün yokluğundan yıpranarak erimekteler.
10 Amayi achifundo afika pophika ana awo enieni, ndiwo anali chakudya chawo pamene anthu anga anali kuwonongeka.
Merhametli kadınlar çocuklarını elleriyle pişirdiler, Halkım kırılırken yiyecek oldu bu kendilerine.
11 Yehova wakwaniritsa ukali wake; wagwetsa pansi mkwiyo wake woopsa. Ndipo wayatsa moto mʼZiyoni kuti uwononge maziko ake.
RAB öfkesini boşalttı, kızgın öfkesini döktü, Temellerini yiyip bitiren ateşi Siyon'un içinde tutuşturdu.
12 Mafumu a pa dziko lapansi sanakhulupirire, kapena wina aliyense wokhala pa dziko lonse, kuti adani kapena ankhondo akhoza kulowa pa zipata za Yerusalemu.
Dünyadaki kralların ve insanların hiçbiri Yeruşalim kapılarından hasımların, düşmanların gireceğine inanmazdı.
13 Koma izi zinachitika chifukwa cha kuchimwa kwa aneneri ake ndi mphulupulu za ansembe ake, amene ankapha anthu osalakwa pakati pawo.
Peygamberlerinin günahı, kâhinlerinin suçu yüzündendi bu, Çünkü onlar kentin ortasında doğruların kanını döktüler.
14 Tsopano akungoyendayenda mʼmisewu ya mu mzinda ngati anthu osaona. Iwo ndi odetsedwa kwambiri ndi magazi palibe yemwe angayerekeze nʼkukhudza komwe chovala chawo.
Sokaklarda körler gibi dolaşıyorlar, Kanla kirlendikleri için kimse giysilerine dokunamıyor.
15 Anthu akuwafuwulira kuti, “Chokani! Inu anthu odetsedwa!” “Chokani! Chokani! Musatikhudze ife!” Akamathawa ndi kumangoyendayenda, pakati pa anthu a mitundu yonse amati, “Asakhalenso ndi ife.”
“Çekilin! Kirliler!” diye bağırdılar onlara, “Çekilin! Çekilin! Dokunmayın!” Kaçıp başıboş dolaştıklarında, Öteki uluslar, “Artık burada kalmasınlar” dediler.
16 Yehova mwini wake wawabalalitsa; Iye sakuwalabadiranso. Ansembe sakulandira ulemu, akuluakulu sakuwachitira chifundo.
RAB kendisi dağıttı onları, Artık yüzlerine bakmayacak. Kâhinleri saymadılar, yaşlılara acımadılar.
17 Ndiponso maso athu atopa nʼkuyangʼana, chithandizo chosabwera nʼkomwe, kuchokera pa nsanja zathu tinadikirira mtundu wa anthu umene sukanatipulumutsa.
Boş yere yardım beklemekten gözlerimizin feri sönüyor, Gözetleme kulesinde bizi kurtaramayacak bir ulusu bekledikçe bekledik.
18 Anthu ankalondola mapazi athu, choncho sitikanayenda mʼmisewu yathu mu mzinda. Chimaliziro chathu chinali pafupi, masiku athu anali owerengeka, chifukwa chimaliziro chathu chinali chitafika.
İzlerimizi sürüyorlar, Sokaklarımızda gezemez olduk. Sonumuz yaklaştı, günlerimiz tükendi, Çünkü sonumuz geldi.
19 Otilondola akuthamanga kwambiri kuposa ziwombankhanga mu mlengalenga; anatithamangitsa mpaka ku mapiri ndi kutibisalira mʼchipululu.
Bizi kovalayanlar gökteki kartallardan çevikti, Dağların üstünde kovaladılar bizi, Çölde bize pusu kurdular.
20 Wodzozedwa wa Yehova, mpweya wathu wotipatsa moyo, anakodwa mʼmisampha yawo. Tinaganiza kuti tidzakhala pansi pa mthunzi wake pakati pa mitundu ya anthu.
Yaşam soluğumuz, RAB'bin meshettiği kral onların çukurunda yakalandı; Hani onun için, “Ulusların arasında onun gölgesinde yaşayacağız” dediğimiz.
21 Kondwera ndi kusangalala, mwana wamkazi wa Edomu. Iwe amene umakhala mʼdziko la Uzi. Koma iwenso chikho chidzakupeza; udzaledzera mpaka kukhala maliseche.
Ûs ülkesinde yaşayan Edom kızı, sevin, coş, Ancak kâse sana da gelecek, sarhoş olup soyunacaksın.
22 Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, chilango chako chidzatha; Iye sadzatalikitsa nthawi yako ya ukapolo. Koma Yehova adzalanga machimo ako, iwe mwana wamkazi wa Edomu, ndi kuyika poyera mphulupulu zako.
Ey Siyon kızı, suçunun cezası sona erdi, RAB bir daha seni sürgüne göndermeyecek. Ama, ey Edom kızı, suçun yüzünden seni cezalandırıp günahlarını ortaya çıkaracak.