< Maliro 4 >

1 Haa! Golide wathimbirira, golide wosalala wasinthikiratu! Amwazamwaza miyala yokongola ya kumalo opatulika pamphambano ponse pa mzinda.
How the gold has become dim, the most pure gold changed! The stones of the sanctuary are poured out at the head of every street.
2 Haa! Ana a Ziyoni amtengowapatali amene kale anali ngati golide, tsopano ali ngati miphika ya dothi, ntchito ya owumba mbiya!
The precious sons of Zion, comparable to fine gold, how they are esteemed as earthen pitchers, the work of the hands of the potter!
3 Ngakhale nkhandwe zimapereka bere kuyamwitsa ana ake, koma anthu anga asanduka ankhanza ngati nthiwatiwa mʼchipululu.
Even the jackals draw out the breast; they give suck to their young ones. The daughter of my people has become cruel, like the ostriches in the wilderness.
4 Lilime la mwana lakangamira kukhosi chifukwa cha ludzu, ana akupempha chakudya, koma palibe amene akuwapatsa.
The tongue of the sucking child clings to the roof of his mouth for thirst. The young sons ask bread, and no man breaks it to them.
5 Iwo amene kale ankadya zonona akupemphetsa mʼmisewu ya mu mzinda. Iwo amene kale ankavala zokongola tsopano akugona pa phulusa.
Those who fed luxuriously are desolate in the streets. Those who were brought up in scarlet embrace dunghills.
6 Kuyipa kwa anthu anga kunali kwakukulu kuposa anthu a ku Sodomu, amene anawonongedwa mʼkamphindi kochepa popanda owathandiza.
For the iniquity of the daughter of my people is greater than the sin of Sodom, that was overthrown as in a moment, and no hands were laid upon her.
7 Akalonga ake anali owala koposa chisanu chowundana ndi oyera kuposa mkaka. Matupi awo anali ofiira kuposa miyala ya rubi, maonekedwe awo ngati miyala ya safiro.
Her ranking men were purer than snow. They were whiter than milk. They were more ruddy in body than rubies. Their polishing was as of sapphire.
8 Koma tsopano maonekedwe awo ndi akuda kuposa mwaye; palibe angawazindikire mʼmisewu ya mu mzinda. Khungu lawo lachita makwinyamakwinya pa mafupa awo; lawuma gwaa ngati nkhuni.
Their visage is blacker than a coal. They are not known in the streets. Their skin clings to their bones. It is withered. It has become like a stick.
9 Amene anaphedwa ndi lupanga aliko bwino kuposa amene anafa ndi njala; chifukwa chosowa chakudya cha mʼmunda iwowa ankafowoka ndi njala mpaka kufa.
Those who are slain with the sword are better than those who are slain with hunger, for these pine away, stricken through, for want of the fruits of the field.
10 Amayi achifundo afika pophika ana awo enieni, ndiwo anali chakudya chawo pamene anthu anga anali kuwonongeka.
The hands of the pitiful women have boiled their own children. They were their food in the destruction of the daughter of my people.
11 Yehova wakwaniritsa ukali wake; wagwetsa pansi mkwiyo wake woopsa. Ndipo wayatsa moto mʼZiyoni kuti uwononge maziko ake.
Jehovah has accomplished his wrath. He has poured out his fierce anger, and he has kindled a fire in Zion, which has devoured the foundations thereof.
12 Mafumu a pa dziko lapansi sanakhulupirire, kapena wina aliyense wokhala pa dziko lonse, kuti adani kapena ankhondo akhoza kulowa pa zipata za Yerusalemu.
The kings of the earth did not believe, nor all the inhabitants of the world, that the adversary and the enemy would enter into the gates of Jerusalem.
13 Koma izi zinachitika chifukwa cha kuchimwa kwa aneneri ake ndi mphulupulu za ansembe ake, amene ankapha anthu osalakwa pakati pawo.
It is because of the sins of her prophets, and the iniquities of her priests, who have shed the blood of the just in the midst of her.
14 Tsopano akungoyendayenda mʼmisewu ya mu mzinda ngati anthu osaona. Iwo ndi odetsedwa kwambiri ndi magazi palibe yemwe angayerekeze nʼkukhudza komwe chovala chawo.
They wander as blind men in the streets. They are polluted with blood, so that men cannot touch their garments.
15 Anthu akuwafuwulira kuti, “Chokani! Inu anthu odetsedwa!” “Chokani! Chokani! Musatikhudze ife!” Akamathawa ndi kumangoyendayenda, pakati pa anthu a mitundu yonse amati, “Asakhalenso ndi ife.”
Depart ye, they cried to them. Unclean! Depart, depart, do not touch! When they fled away and wandered, men said among the nations, They shall no more sojourn here.
16 Yehova mwini wake wawabalalitsa; Iye sakuwalabadiranso. Ansembe sakulandira ulemu, akuluakulu sakuwachitira chifundo.
The anger of Jehovah has scattered them. He will no more regard them. They did not respect the persons of the priests. They did not favor the elders.
17 Ndiponso maso athu atopa nʼkuyangʼana, chithandizo chosabwera nʼkomwe, kuchokera pa nsanja zathu tinadikirira mtundu wa anthu umene sukanatipulumutsa.
Our eyes do yet fail in looking for our vain help. In our watching we have watched for a nation that could not save.
18 Anthu ankalondola mapazi athu, choncho sitikanayenda mʼmisewu yathu mu mzinda. Chimaliziro chathu chinali pafupi, masiku athu anali owerengeka, chifukwa chimaliziro chathu chinali chitafika.
They hunt our steps, so that we cannot go in our streets. Our end is near, our days are fulfilled, for our end has come.
19 Otilondola akuthamanga kwambiri kuposa ziwombankhanga mu mlengalenga; anatithamangitsa mpaka ku mapiri ndi kutibisalira mʼchipululu.
Our pursuers were swifter than the eagles of the heavens. They chased us upon the mountains. They laid wait for us in the wilderness.
20 Wodzozedwa wa Yehova, mpweya wathu wotipatsa moyo, anakodwa mʼmisampha yawo. Tinaganiza kuti tidzakhala pansi pa mthunzi wake pakati pa mitundu ya anthu.
The breath of our nostrils, the anointed of Jehovah, was taken in their pits, of whom we said, Under his shadow we shall live among the nations.
21 Kondwera ndi kusangalala, mwana wamkazi wa Edomu. Iwe amene umakhala mʼdziko la Uzi. Koma iwenso chikho chidzakupeza; udzaledzera mpaka kukhala maliseche.
Rejoice and be glad, O daughter of Edom, who dwells in the land of Uz. Yet the cup shall pass through to thee also. Thou shall be drunken, and shall make thyself naked.
22 Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, chilango chako chidzatha; Iye sadzatalikitsa nthawi yako ya ukapolo. Koma Yehova adzalanga machimo ako, iwe mwana wamkazi wa Edomu, ndi kuyika poyera mphulupulu zako.
The punishment of thine iniquity is accomplished, O daughter of Zion. He will no more carry thee away into captivity. He will visit thine iniquity, O daughter of Edom. He will uncover thy sins.

< Maliro 4 >