< Maliro 4 >

1 Haa! Golide wathimbirira, golide wosalala wasinthikiratu! Amwazamwaza miyala yokongola ya kumalo opatulika pamphambano ponse pa mzinda.
Как почерня златото! Измени се най-чистото злато! Камъните на светилището са пръснати край всичките улици,
2 Haa! Ana a Ziyoni amtengowapatali amene kale anali ngati golide, tsopano ali ngati miphika ya dothi, ntchito ya owumba mbiya!
Драгоценните синове на Сион, равноценни с чисто злато, Как се считат за глинени съдове, дело на грънчарска ръка!
3 Ngakhale nkhandwe zimapereka bere kuyamwitsa ana ake, koma anthu anga asanduka ankhanza ngati nthiwatiwa mʼchipululu.
Даже чакалите подават съсци и кърмят малките си; А дъщерята на людете ми се ожесточи като камилоптиците в пустинята;
4 Lilime la mwana lakangamira kukhosi chifukwa cha ludzu, ana akupempha chakudya, koma palibe amene akuwapatsa.
Защото езикът на бозайничето се залепя на небцето му от жажда; Децата искат хляб, но няма кой да им отчупи.
5 Iwo amene kale ankadya zonona akupemphetsa mʼmisewu ya mu mzinda. Iwo amene kale ankavala zokongola tsopano akugona pa phulusa.
Ония, които ядяха отбрани ястия, лежат небрежни в улиците; Възпитаните в мораво прегръщат бунището.
6 Kuyipa kwa anthu anga kunali kwakukulu kuposa anthu a ku Sodomu, amene anawonongedwa mʼkamphindi kochepa popanda owathandiza.
Защото наказанието за беззаконието на дъщерята на людете ми стана по-голямо от наказанието за греха на Содом, Който биде съсипан в един миг, без да са го барали човешки ръце.
7 Akalonga ake anali owala koposa chisanu chowundana ndi oyera kuposa mkaka. Matupi awo anali ofiira kuposa miyala ya rubi, maonekedwe awo ngati miyala ya safiro.
Благородните й бяха по-чисти от сняг, по-бели от мляко, Снагата им по-червена от рубини, блестяха като сапфир;
8 Koma tsopano maonekedwe awo ndi akuda kuposa mwaye; palibe angawazindikire mʼmisewu ya mu mzinda. Khungu lawo lachita makwinyamakwinya pa mafupa awo; lawuma gwaa ngati nkhuni.
А сега лицето им е по-черно от сажди; не се познават по улиците! Кожата им залепна за костите им, изсъхна, стана като дърво.
9 Amene anaphedwa ndi lupanga aliko bwino kuposa amene anafa ndi njala; chifukwa chosowa chakudya cha mʼmunda iwowa ankafowoka ndi njala mpaka kufa.
По-щастливи бяха убитите от меч, нежели умъртвените от глад; Защото тия чезнат, прободени, от липса на полските произведения.
10 Amayi achifundo afika pophika ana awo enieni, ndiwo anali chakudya chawo pamene anthu anga anali kuwonongeka.
Ръцете на милозливите жени свариха чадата им; Те им станаха храна при разорението на дъщерята на людете ми,
11 Yehova wakwaniritsa ukali wake; wagwetsa pansi mkwiyo wake woopsa. Ndipo wayatsa moto mʼZiyoni kuti uwononge maziko ake.
Господ извърши възнамереното от Него в яростта Му, изля пламенния Си гняв, Запали огън в Сион, който изпояде основите му.
12 Mafumu a pa dziko lapansi sanakhulupirire, kapena wina aliyense wokhala pa dziko lonse, kuti adani kapena ankhondo akhoza kulowa pa zipata za Yerusalemu.
Земните царе не вярваха, нито живущите по целия свят, Че щеше да влезе противник и неприятел в ерусалимските порти.
13 Koma izi zinachitika chifukwa cha kuchimwa kwa aneneri ake ndi mphulupulu za ansembe ake, amene ankapha anthu osalakwa pakati pawo.
А това стана поради греховете на пророците му и поради беззаконията на свещениците му, Които проливаха кръвта на праведните всред него.
14 Tsopano akungoyendayenda mʼmisewu ya mu mzinda ngati anthu osaona. Iwo ndi odetsedwa kwambiri ndi magazi palibe yemwe angayerekeze nʼkukhudza komwe chovala chawo.
Те се скитаха като слепи по улиците, оскверниха се с кръв, Тъй щото човеците не можаха да се допират до дрехите им.
15 Anthu akuwafuwulira kuti, “Chokani! Inu anthu odetsedwa!” “Chokani! Chokani! Musatikhudze ife!” Akamathawa ndi kumangoyendayenda, pakati pa anthu a mitundu yonse amati, “Asakhalenso ndi ife.”
Отстъпете, вие нечисти, викаха към тях; отстъпете, отстъпете, не се допирайте до нас; А когато те бягаха и се скитаха, говореше се между народите: Няма да пришелствуват вече с нас.
16 Yehova mwini wake wawabalalitsa; Iye sakuwalabadiranso. Ansembe sakulandira ulemu, akuluakulu sakuwachitira chifundo.
Гневът на Господа ги разпръсна; Той не ще вече да гледа на тях; Свещеническо лице не почетоха, за старци не се смилиха.
17 Ndiponso maso athu atopa nʼkuyangʼana, chithandizo chosabwera nʼkomwe, kuchokera pa nsanja zathu tinadikirira mtundu wa anthu umene sukanatipulumutsa.
И до сега очите ни се изнуряват от чакане суетната за нас помощ; Ожидахме народ, който не можеше да спасява.
18 Anthu ankalondola mapazi athu, choncho sitikanayenda mʼmisewu yathu mu mzinda. Chimaliziro chathu chinali pafupi, masiku athu anali owerengeka, chifukwa chimaliziro chathu chinali chitafika.
Причакват стъпките ни, така че да не можем да ходим по улиците си; Приближи се краят ни; дните ни се изпълниха; да! краят ни дойде.
19 Otilondola akuthamanga kwambiri kuposa ziwombankhanga mu mlengalenga; anatithamangitsa mpaka ku mapiri ndi kutibisalira mʼchipululu.
Ония, които ни гонеха, станаха по-леки от небесните орли; Гониха ни по планините, причакваха ни в пустинята.
20 Wodzozedwa wa Yehova, mpweya wathu wotipatsa moyo, anakodwa mʼmisampha yawo. Tinaganiza kuti tidzakhala pansi pa mthunzi wake pakati pa mitundu ya anthu.
Помазаникът Господен, дишането на ноздрите ни, Тоя, под чиято сянка казвахме, че ще живеем между народите, се хвана в техните ями.
21 Kondwera ndi kusangalala, mwana wamkazi wa Edomu. Iwe amene umakhala mʼdziko la Uzi. Koma iwenso chikho chidzakupeza; udzaledzera mpaka kukhala maliseche.
Радвай се и весели се, дъщерьо едомска, която живееш в земята Уз! Обаче и до тебе ще дойде чашата; ще се опиеш, и ще се заголиш.
22 Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, chilango chako chidzatha; Iye sadzatalikitsa nthawi yako ya ukapolo. Koma Yehova adzalanga machimo ako, iwe mwana wamkazi wa Edomu, ndi kuyika poyera mphulupulu zako.
Свърши се наказанието за беззаконието ти, дъщерьо Сионова; Той няма вече да те закара в плен; Но ще накаже твоето беззаконие, дъщерьо едомска, ще открие съгрешенията ти.

< Maliro 4 >