< Maliro 3 >

1 Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
Ngiyindodaebone inhlupheko ngentonga yolaka lwayo.
2 Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
Ingikhokhele yangihambisa emnyameni kodwa hatshi ekukhanyeni.
3 zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
Isibili iphenduke yamelana lami; iphendule isandla sayo imelene lami usuku lonke.
4 Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
Igugisile inyama yami lesikhumba sami; yephulile amathambo ami.
5 Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
Yakhile imelene lami, yangihanqa ngenyongo lobunzima.
6 Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
Ingihlalise endaweni ezimnyama, njengabafa endulo.
7 Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
Ingibiyele ukuze ngingaphumi, yenza iketane lami lethusi laba nzima.
8 Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
Njalo nxa ngikhala ngimemeza, ivalela phandle umkhuleko wami.
9 Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
Ibiyele indlela yami ngamatshe abaziweyo, yenza izindlela zami zagoba.
10 Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
Yaba kimi njengebhere elicathemeyo, isilwane ezindaweni zensitha.
11 Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
Iphambule izindlela zami, yangidabudabula, yangenza unxiwa.
12 Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
Igobisile idandili layo, yangimisa njengento yokunenjwa ngomtshoko.
13 Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
Yenze amadodana esamba semitshoko yayo angena ezinsweni zami.
14 Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
Ngaba yinhlekisa kibo bonke abantu bakithi, ingoma yabo usuku lonke.
15 Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
Ingisuthise ngezinto ezibabayo, yanginathisa umhlonyane.
16 Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
Njalo ichoboze amazinyo ami ngokhethe, yangigiga emlotheni.
17 Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
Njalo wena walahla umphefumulo wami khatshana lokuthula; ngikhohlwe okuhle.
18 Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
Ngakho ngithi: Kubhubhile amandla ami lethemba lami eNkosini.
19 Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
Khumbula inhlupheko yami lokuzulazula kwami, umhlonyane lenyongo.
20 Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
Umphefumulo wami uhlala ukukhumbula, njalo ukhotheme phakathi kwami.
21 Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
Lokhu ngiyakubuyisela enhliziyweni yami, ngakho-ke ngiyathemba.
22 Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
Kuyizihawu zeNkosi ukuthi kasiqedwanga, ngoba izisa zakhe kazipheli;
23 Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
zintsha ikuseni yonke; lukhulu uthembeko lwayo.
24 Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
INkosi iyisabelo sami, kutsho umphefumulo wami; ngakho-ke ngizathemba kiyo.
25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
INkosi ilungile kwabayilindelayo, kumphefumulo oyidingayo.
26 nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
Kuhle ukuthi umuntu athembe, njalo ngokuthula kusindiso lweNkosi.
27 Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
Kuhle emuntwini ukuthi athwale ijogwe ebutsheni bakhe.
28 Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
Kahlale yedwa, athule, ngoba isimethese lona.
29 Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
Kabeke umlomo wakhe othulini; mhlawumbe kungaba khona ithemba.
30 Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
Kanikele isihlathi sakhe komtshayayo; asuthe inhlamba.
31 Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
Ngoba iNkosi kayiyikulahla kuze kube phakade.
32 Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
Ngoba lanxa idabukisile, kanti izakuba lesihawu ngobunengi bezisa zayo.
33 Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
Ngoba kayihluphi ngenhliziyo yayo idabukise abantwana babantu;
34 Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
ukuchoboza ngaphansi kwenyawo zayo zonke izibotshwa zomhlaba;
35 kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
ukuphambukisa ilungelo lomuntu phambi kobuso boPhezukonke;
36 kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
ukuphambanisa umuntu kudaba lwakhe, iNkosi kayikuboni yini?
37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
Ngubani ongakukhuluma, njalo kwenzeke, nxa iNkosi ingakulayanga?
38 Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
Kakuphumi ububi lokuhle emlonyeni woPhezukonke yini?
39 Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
Ngakho usolelani umuntu ophilayo, umuntu ngezono zakhe?
40 Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
Asihlole silinge izindlela zethu, sibuyele eNkosini.
41 Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
Asiphakamisele inhliziyo lezandla zethu kuNkulunkulu emazulwini.
42 “Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
Thina siphambukile, saba lenkani; wena kawuthethelelanga.
43 “Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
Wembese ngolaka, waxotshana lathi, wabulala, kawuhawukelanga.
44 Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
Uzembese ngeyezi, ukuze kungedluli umkhuleko.
45 Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
Usenze saba yimfucuza lezibi phakathi kwezizwe.
46 “Adani anthu atitsekulira pakamwa.
Zonke izitha zethu zivule umlomo wazo zimelene lathi.
47 Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
Ukwesaba lomgodi kukhona phambi kwethu, incithakalo lokwephuka.
48 Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
Ilihlo lami lehlisa imifula yamanzi ngokuchitheka kwendodakazi yabantu bami.
49 Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
Ilihlo lami liyajuluka, kaliyekeli, kungelakuma,
50 mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
ize ikhangele phansi ibone iNkosi isezulwini.
51 Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
Ilihlo lami lenza umphefumulo wami ube buhlungu ngenxa yawo wonke amadodakazi omuzi wakithi.
52 Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
Izitha zami zingizingele kabuhlungu njengenyoni, kungelasizatho.
53 Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
Bayiqumile impilo yami emgodini, baphosa ilitshe phezu kwami.
54 madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
Amanzi ageleza phezu kwekhanda lami; ngathi: Ngiqunyiwe.
55 Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
Ngabiza ibizo lakho, Nkosi, ngisemgodini phansi;
56 Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
wezwa ilizwi lami; ungafihli indlebe yakho ekuphefumuleni kwami, ekukhaleleni kwami usizo.
57 Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
Wasondela ngosuku lapho ngikubiza, wathi: Ungesabi.
58 Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
Nkosi, uzimele izindaba zomphefumulo wami, wahlenga impilo yami.
59 Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
Nkosi, ubonile ukoniwa kwami; yahlulela udaba lwami.
60 Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
Ubonile yonke impindiselo yabo, wonke amacebo abo amelene lami.
61 Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
Uzwile inhlamba yabo, Nkosi, wonke amacebo abo amelene lami,
62 manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
indebe zabangivukelayo, lokuzindla kwabo kumelene lami lonke usuku.
63 Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
Khangela ukuhlala kwabo, lokusukuma kwabo; ngiyingoma yabo.
64 Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
Buyisela kibo impindiselo, Nkosi, njengokomsebenzi wezandla zabo.
65 Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
Banike ubulukhuni benhliziyo, isiqalekiso sakho kibo.
66 Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.
Xotshana labo ngolaka, ubabhubhise bangabi ngaphansi kwamazulu eNkosi.

< Maliro 3 >