< Maliro 3 >

1 Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
ALEPH. Ego vir videns paupertatem meam in virga indignationis eius.
2 Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
ALEPH. Me minavit, et adduxit in tenebras, et non in lucem.
3 zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
ALEPH. Tantum in me vertit, et convertit manum suam tota die.
4 Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
BETH. Vetustam fecit pellem meam, et carnem meam, contrivit ossa mea.
5 Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
BETH. Aedificavit in gyro meo, et circumdedit me felle, et labore.
6 Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
BETH. In tenebrosis collocavit me, quasi mortuos sempiternos.
7 Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
GHIMEL. Circumaedificavit adversum me, ut non egrediar: aggravavit compedem meum.
8 Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
GHIMEL. Sed et cum clamavero, et rogavero, exclusit orationem meam.
9 Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
GHIMEL. Conclusit vias meas lapidibus quadris, semitas meas subvertit.
10 Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
DALETH. Ursus insidians factus est mihi: leo in absconditis.
11 Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
DALETH. Semitas meas subvertit, et confregit me: posuit me desolatam.
12 Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
DALETH. Tetendit arcum suum, et posuit me quasi signum ad sagittam.
13 Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
HE. Misit in renibus meis filias pharetrae suae.
14 Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
HE. Factus sum in derisum omni populo meo, canticum eorum tota die.
15 Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
HE. Replevit me amaritudinibus, inebriavit me absynthio.
16 Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
VAU. Et fregit ad numerum dentes meos, cibavit me cinere.
17 Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
VAU. Et repulsa est a pace anima mea, oblitus sum bonorum.
18 Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
VAU. Et dixi: Periit finis meus, et spes mea a Domino.
19 Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
ZAIN. Recordare paupertatis, et transgressionis meae, absinthii, et fellis.
20 Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
ZAIN. Memoria memor ero, et tabescet in me anima mea.
21 Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
ZAIN. Haec recolens in corde meo, ideo sperabo.
22 Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
HETH. Misericordiae Domini quia non sumus consumpti: quia non defecerunt miserationes eius.
23 Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
HETH. Novi diluculo, multa est fides tua.
24 Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
HETH. Pars mea Dominus, dixit anima mea: propterea expectabo eum.
25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
TETH. Bonus est Dominus sperantibus in eum, animae quaerenti illum.
26 nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
TETH. Bonum est praestolari cum silentio salutare Dei.
27 Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
TETH. Bonum est viro, cum portaverit iugum ab adolescentia sua.
28 Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
IOD. Sedebit solitarius, et tacebit: quia levavit se super se.
29 Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
IOD. Ponet in pulvere os suum, si forte sit spes.
30 Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
IOD. Dabit percutienti se maxillam, saturabitur opprobriis.
31 Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
CAPH. Quia non repellet in sempiternum Dominus.
32 Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
CAPH. Quia si abiecit, miserebitur secundum multitudinem misericordiarum suarum.
33 Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
CAPH. Non enim humiliavit ex corde suo, et abiecit filios hominum,
34 Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
LAMED. Ut conteret sub pedibus suis omnes vinctos terrae,
35 kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
LAMED. Ut declinaret iudicium viri in conspectu vultus Altissimi.
36 kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
LAMED. Ut perverteret hominem in iudicio suo, Dominus ignoravit.
37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
MEM. Quis est iste, qui dixit ut fieret, Domino non iubente?
38 Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
MEM. Ex ore Altissimi non egredientur nec mala nec bona?
39 Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
MEM. Quid murmuravit homo vivens, vir pro peccatis suis?
40 Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
NUN. Scrutemur vias nostras, et quaeramus, et revertamur ad Dominum.
41 Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
NUN. Levemus corda nostra cum manibus ad Dominum in caelos.
42 “Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
NUN. Nos inique egimus, et ad iracundiam provocavimus: idcirco tu inexorabilis es.
43 “Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
SAMECH. Operuisti in furore, et percussisti nos: occidisti, nec pepercisti.
44 Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
SAMECH. Opposuisti nubem tibi, ne transeat oratio.
45 Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
SAMECH. Eradicationem, et abiectionem posuisti me in medio populorum.
46 “Adani anthu atitsekulira pakamwa.
PHE. Aperuerunt super nos os suum omnes inimici.
47 Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
PHE. Formido, et laqueus facta est nobis vaticinatio, et contritio.
48 Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
PHE. Divisiones aquarum deduxit oculus meus, in contritione filiae populi mei.
49 Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
AIN. Oculus meus afflictus est, nec tacuit, eo quod non esset requies,
50 mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
AIN. Donec respiceret et videret Dominus de caelis.
51 Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
AIN. Oculus meus depraedatus est animam meam in cunctis filiabus urbis meae.
52 Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
SADE. Venatione ceperunt me quasi avem inimici mei gratis.
53 Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
SADE. Lapsa est in lacum vita mea, et posuerunt lapidem super me.
54 madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
SADE. Inundaverunt aquae super caput meum: dixi: Perii.
55 Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
COPH. Invocavi nomen tuum Domine de lacu novissimo.
56 Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
COPH. Vocem meam audisti: ne avertas aurem tuam a singultu meo, et clamoribus.
57 Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
COPH. Appropinquasti in die, quando invocavi te: dixisti: Ne timeas.
58 Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
RES. Iudicasti Domine causam animae meae, redemptor vitae meae.
59 Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
RES. Vidisti Domine iniquitatem illorum adversum me: iudica iudicium meum.
60 Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
RES. Vidisti omnem furorem, universas cogitationes eorum adversum me.
61 Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
SIN. Audisti opprobrium eorum Domine, omnes cogitationes eorum adversum me:
62 manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
SIN. Labia insurgentium mihi; et meditationes eorum adversum me tota die.
63 Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
SIN. Sessionem eorum, et resurrectionem eorum vide, ego sum psalmus eorum.
64 Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
THAU. Redes eis vicem Domine iuxta opera manuum suarum.
65 Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
THAU. Dabis eis scutum cordis laborem tuum.
66 Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.
THAU. Persequeris in furore, et conteres eos sub caelis Domine.

< Maliro 3 >