< Maliro 3 >

1 Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
उसके रोष की छड़ी से दुःख भोगनेवाला पुरुष मैं ही हूँ;
2 Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
वह मुझे ले जाकर उजियाले में नहीं, अंधियारे ही में चलाता है;
3 zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
उसका हाथ दिन भर मेरे ही विरुद्ध उठता रहता है।
4 Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
उसने मेरा माँस और चमड़ा गला दिया है, और मेरी हड्डियों को तोड़ दिया है;
5 Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
उसने मुझे रोकने के लिये किला बनाया, और मुझ को कठिन दुःख और श्रम से घेरा है;
6 Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
उसने मुझे बहुत दिन के मरे हुए लोगों के समान अंधेरे स्थानों में बसा दिया है।
7 Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
मेरे चारों ओर उसने बाड़ा बाँधा है कि मैं निकल नहीं सकता; उसने मुझे भारी साँकल से जकड़ा है;
8 Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
मैं चिल्ला-चिल्ला के दुहाई देता हूँ, तो भी वह मेरी प्रार्थना नहीं सुनता;
9 Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
मेरे मार्गों को उसने गढ़े हुए पत्थरों से रोक रखा है, मेरी डगरों को उसने टेढ़ी कर दिया है।
10 Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
१०वह मेरे लिये घात में बैठे हुए रीछ और घात लगाए हुए सिंह के समान है;
11 Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
११उसने मुझे मेरे मार्गों से भुला दिया, और मुझे फाड़ डाला; उसने मुझ को उजाड़ दिया है।
12 Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
१२उसने धनुष चढ़ाकर मुझे अपने तीर का निशाना बनाया है।
13 Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
१३उसने अपनी तीरों से मेरे हृदय को बेध दिया है;
14 Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
१४सब लोग मुझ पर हँसते हैं और दिन भर मुझ पर ढालकर गीत गाते हैं,
15 Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
१५उसने मुझे कठिन दुःख से भर दिया, और नागदौना पिलाकर तृप्त किया है।
16 Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
१६उसने मेरे दाँतों को कंकड़ से तोड़ डाला, और मुझे राख से ढाँप दिया है;
17 Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
१७और मुझ को मन से उतारकर कुशल से रहित किया है; मैं कल्याण भूल गया हूँ;
18 Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
१८इसलिए मैंने कहा, “मेरा बल नष्ट हुआ, और मेरी आशा जो यहोवा पर थी, वह टूट गई है।”
19 Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
१९मेरा दुःख और मारा-मारा फिरना, मेरा नागदौने और विष का पीना स्मरण कर!
20 Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
२०मैं उन्हीं पर सोचता रहता हूँ, इससे मेरा प्राण ढला जाता है।
21 Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
२१परन्तु मैं यह स्मरण करता हूँ, इसलिए मुझे आशा है:
22 Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
२२हम मिट नहीं गए; यह यहोवा की महाकरुणा का फल है, क्योंकि उसकी दया अमर है।
23 Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
२३प्रति भोर वह नई होती रहती है; तेरी सच्चाई महान है।
24 Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
२४मेरे मन ने कहा, “यहोवा मेरा भाग है, इस कारण मैं उसमें आशा रखूँगा।”
25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
२५जो यहोवा की बाट जोहते और उसके पास जाते हैं, उनके लिये यहोवा भला है।
26 nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
२६यहोवा से उद्धार पाने की आशा रखकर चुपचाप रहना भला है।
27 Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
२७पुरुष के लिये जवानी में जूआ उठाना भला है।
28 Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
२८वह यह जानकर अकेला चुपचाप रहे, कि परमेश्वर ही ने उस पर यह बोझ डाला है;
29 Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
२९वह अपना मुँह धूल में रखे, क्या जाने इसमें कुछ आशा हो;
30 Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
३०वह अपना गाल अपने मारनेवाले की ओर फेरे, और नामधराई सहता रहे।
31 Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
३१क्योंकि प्रभु मन से सर्वदा उतारे नहीं रहता,
32 Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
३२चाहे वह दुःख भी दे, तो भी अपनी करुणा की बहुतायत के कारण वह दया भी करता है;
33 Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
३३क्योंकि वह मनुष्यों को अपने मन से न तो दबाता है और न दुःख देता है।
34 Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
३४पृथ्वी भर के बन्दियों को पाँव के तले दलित करना,
35 kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
३५किसी पुरुष का हक़ परमप्रधान के सामने मारना,
36 kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
३६और किसी मनुष्य का मुकद्दमा बिगाड़ना, इन तीन कामों को यहोवा देख नहीं सकता।
37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
३७यदि यहोवा ने आज्ञा न दी हो, तब कौन है कि वचन कहे और वह पूरा हो जाए?
38 Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
३८विपत्ति और कल्याण, क्या दोनों परमप्रधान की आज्ञा से नहीं होते?
39 Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
३९इसलिए जीवित मनुष्य क्यों कुड़कुड़ाए? और पुरुष अपने पाप के दण्ड को क्यों बुरा माने?
40 Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
४०हम अपने चाल चलन को ध्यान से परखें, और यहोवा की ओर फिरें!
41 Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
४१हम स्वर्ग में वास करनेवाले परमेश्वर की ओर मन लगाएँ और हाथ फैलाएँ और कहें:
42 “Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
४२“हमने तो अपराध और बलवा किया है, और तूने क्षमा नहीं किया।
43 “Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
४३तेरा कोप हम पर है, तू हमारे पीछे पड़ा है, तूने बिना तरस खाए घात किया है।
44 Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
४४तूने अपने को मेघ से घेर लिया है कि तुझ तक प्रार्थना न पहुँच सके।
45 Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
४५तूने हमको जाति-जाति के लोगों के बीच में कूड़ा-करकट सा ठहराया है।
46 “Adani anthu atitsekulira pakamwa.
४६हमारे सब शत्रुओं ने हम पर अपना-अपना मुँह फैलाया है;
47 Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
४७भय और गड्ढा, उजाड़ और विनाश, हम पर आ पड़े हैं;
48 Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
४८मेरी आँखों से मेरी प्रजा की पुत्री के विनाश के कारण जल की धाराएँ बह रही है।
49 Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
४९मेरी आँख से लगातार आँसू बहते रहेंगे,
50 mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
५०जब तक यहोवा स्वर्ग से मेरी ओर न देखे;
51 Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
५१अपनी नगरी की सब स्त्रियों का हाल देखने पर मेरा दुःख बढ़ता है।
52 Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
५२जो व्यर्थ मेरे शत्रु बने हैं, उन्होंने निर्दयता से चिड़िया के समान मेरा आहेर किया है;
53 Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
५३उन्होंने मुझे गड्ढे में डालकर मेरे जीवन का अन्त करने के लिये मेरे ऊपर पत्थर लुढ़काए हैं;
54 madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
५४मेरे सिर पर से जल बह गया, मैंने कहा, ‘मैं अब नाश हो गया।’
55 Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
५५हे यहोवा, गहरे गड्ढे में से मैंने तुझ से प्रार्थना की;
56 Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
५६तूने मेरी सुनी कि जो दुहाई देकर मैं चिल्लाता हूँ उससे कान न फेर ले!
57 Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
५७जब मैंने तुझे पुकारा, तब तूने मुझसे कहा, ‘मत डर!’
58 Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
५८हे यहोवा, तूने मेरा मुकद्दमा लड़कर मेरा प्राण बचा लिया है।
59 Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
५९हे यहोवा, जो अन्याय मुझ पर हुआ है उसे तूने देखा है; तू मेरा न्याय चुका।
60 Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
६०जो बदला उन्होंने मुझसे लिया, और जो कल्पनाएँ मेरे विरुद्ध की, उन्हें भी तूने देखा है।
61 Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
६१हे यहोवा, जो कल्पनाएँ और निन्दा वे मेरे विरुद्ध करते हैं, वे भी तूने सुनी हैं।
62 manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
६२मेरे विरोधियों के वचन, और जो कुछ भी वे मेरे विरुद्ध लगातार सोचते हैं, उन्हें तू जानता है।
63 Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
६३उनका उठना-बैठना ध्यान से देख; वे मुझ पर लगते हुए गीत गाते हैं।
64 Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
६४हे यहोवा, तू उनके कामों के अनुसार उनको बदला देगा।
65 Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
६५तू उनका मन सुन्न कर देगा; तेरा श्राप उन पर होगा।
66 Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.
६६हे यहोवा, तू अपने कोप से उनको खदेड़-खदेड़कर धरती पर से नाश कर देगा।”

< Maliro 3 >