< Maliro 3 >

1 Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
Je suis l’homme qui ai vu l’affliction par la verge de sa fureur.
2 Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
Il m’a conduit et amené dans les ténèbres, et non dans la lumière.
3 zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
Certes c’est contre moi qu’il a tout le jour tourné et retourné sa main.
4 Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
Il a fait vieillir ma chair et ma peau; il a brisé mes os.
5 Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
Il a bâti contre moi, et m’a environné de fiel et de peine.
6 Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
Il m’a fait habiter dans des lieux ténébreux, comme ceux qui sont morts depuis longtemps.
7 Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
Il a fait une clôture autour de moi, afin que je ne sorte point; il a appesanti mes chaînes.
8 Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
Même quand je crie et que j’élève ma voix, il ferme l’accès à ma prière.
9 Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
Il a barré mes chemins avec des pierres de taille; il a bouleversé mes sentiers.
10 Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
Il a été pour moi un ours aux embûches, un lion dans les lieux cachés.
11 Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
Il a fait dévier mes chemins et m’a déchiré; il m’a rendu désolé.
12 Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
Il a bandé son arc, et m’a placé comme un but pour la flèche.
13 Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
Il a fait entrer dans mes reins les flèches de son carquois.
14 Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
Je suis la risée de tout mon peuple, leur chanson tout le jour.
15 Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
Il m’a rassasié d’amertumes, il m’a abreuvé d’absinthe.
16 Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
Il m’a brisé les dents avec du gravier; il m’a couvert de cendre.
17 Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
Et tu as rejeté mon âme loin de la paix, j’ai oublié le bonheur;
18 Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
et j’ai dit: Ma confiance est périe, et mon espérance en l’Éternel.
19 Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
Souviens-toi de mon affliction, et de mon bannissement, de l’absinthe et du fiel.
20 Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
Mon âme s’en souvient sans cesse, et elle est abattue au-dedans de moi. –
21 Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
Je rappelle ceci à mon cœur, c’est pourquoi j’ai espérance:
22 Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
Ce sont les bontés de l’Éternel que nous ne sommes pas consumés, car ses compassions ne cessent pas;
23 Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
elles sont nouvelles chaque matin; grande est ta fidélité!
24 Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
L’Éternel est ma portion, dit mon âme; c’est pourquoi j’espérerai en lui.
25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
L’Éternel est bon pour ceux qui s’attendent à lui, pour l’âme qui le cherche.
26 nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
C’est une chose bonne qu’on attende, et dans le silence, le salut de l’Éternel.
27 Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
Il est bon à l’homme de porter le joug dans sa jeunesse:
28 Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
Il est assis solitaire, et se tait, parce qu’il l’a pris sur lui;
29 Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
il met sa bouche dans la poussière: peut-être y aura-t-il quelque espoir.
30 Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
Il présente la joue à celui qui le frappe, il est rassasié d’opprobres.
31 Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
Car le Seigneur ne rejette pas pour toujours;
32 Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
mais, s’il afflige, il a aussi compassion, selon la grandeur de ses bontés;
33 Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
car ce n’est pas volontiers qu’il afflige et contriste les fils des hommes.
34 Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
Qu’on écrase sous les pieds tous les prisonniers de la terre,
35 kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
qu’on fasse fléchir le droit d’un homme devant la face du Très-haut,
36 kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
qu’on fasse tort à un homme dans sa cause, le Seigneur ne le voit-il point?
37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
Qui est-ce qui dit une chose, et elle arrive, quand le Seigneur ne l’a point commandée?
38 Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
N’est-ce pas de la bouche du Très-haut que viennent les maux et les biens?
39 Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
Pourquoi un homme vivant se plaindrait-il, un homme, à cause de la peine de ses péchés?
40 Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
Recherchons nos voies, et scrutons-les, et retournons jusqu’à l’Éternel.
41 Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
Élevons nos cœurs avec nos mains vers Dieu dans les cieux.
42 “Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
Nous avons désobéi et nous avons été rebelles; tu n’as pas pardonné.
43 “Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
Tu t’es enveloppé de colère et tu nous as poursuivis; tu as tué, tu n’as point épargné.
44 Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
Tu t’es enveloppé d’un nuage, de manière à ce que la prière ne passe point.
45 Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
Tu nous as faits la balayure et le rebut au milieu des peuples.
46 “Adani anthu atitsekulira pakamwa.
Tous nos ennemis ont ouvert la bouche sur nous.
47 Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
La frayeur et la fosse sont venues sur nous, la destruction et la ruine.
48 Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
Des ruisseaux d’eaux coulent de mes yeux à cause de la ruine de la fille de mon peuple.
49 Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
Mon œil se fond en eau, il ne cesse pas et n’a point de relâche,
50 mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
jusqu’à ce que l’Éternel regarde et voie des cieux.
51 Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
Mon œil afflige mon âme à cause de toutes les filles de ma ville.
52 Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
Ceux qui sont mes ennemis sans cause m’ont donné la chasse comme à l’oiseau.
53 Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
Ils m’ont ôté la vie dans une fosse, et ont jeté des pierres sur moi.
54 madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
Les eaux ont coulé par-dessus ma tête; j’ai dit: Je suis retranché!
55 Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
J’ai invoqué ton nom, ô Éternel! de la fosse des abîmes.
56 Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
Tu as entendu ma voix; ne cache point ton oreille à mon soupir, à mon cri.
57 Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
Tu t’es approché au jour où je t’ai invoqué; tu as dit: Ne crains pas.
58 Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
Seigneur, tu as pris en main la cause de mon âme, tu as racheté ma vie.
59 Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
Tu as vu, Éternel, le tort qu’on me fait; juge ma cause.
60 Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
Tu as vu toute leur vengeance, toutes leurs machinations contre moi.
61 Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
Tu as entendu leurs outrages, ô Éternel! toutes leurs machinations contre moi,
62 manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
les lèvres de ceux qui s’élèvent contre moi, et ce qu’ils se proposent contre moi tout le jour.
63 Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
Regarde quand ils s’asseyent et quand ils se lèvent: je suis leur chanson.
64 Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
Rends-leur une récompense, ô Éternel! selon l’ouvrage de leurs mains.
65 Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
Donne-leur un cœur cuirassé; ta malédiction soit sur eux!
66 Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.
Poursuis-les dans ta colère et détruis-les de dessous les cieux de l’Éternel.

< Maliro 3 >